< Jona 2 >
1 Potem je Jona iz ribjega trebuha molil h Gospodu, svojemu Bogu
Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
2 in rekel: »Zaradi razloga svoje stiske sem klical h Gospodu in me je slišal. Ven iz trebuha pekla sem klical in ti si slišal moj glas. (Sheol )
Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol )
3 Kajti vrgel si me v globino, v sredo morij, in poplave so me obkrožile. Vsi tvoji veliki valovi in tvoji valovi so me preleteli.«
Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
4 Potem sem rekel: »Vržen sem iz tvojega pogleda, vendar bom ponovno gledal k tvojemu svetemu templju.
Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
5 Vode so me obkrožile, celó do duše, globine so me zaprle naokoli, plevel je bil zavit okoli moje glave.
Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
6 Odšel sem navzdol, k vznožjem gora. Zemlja, s svojimi zapahi, je bila okoli mene na veke, vendar si ti moje življenje privedel gor iz trohnenja, oh Gospod, moj Bog.
Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
7 Ko je moja duša slabela znotraj mene, sem se spomnil Gospoda. Moja molitev je vstopila k tebi, v tvoj sveti tempelj.
“Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
8 Tisti, ki obeležujejo lažnive ničevosti, zapuščajo svoje lastno usmiljenje.
“Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
9 Toda jaz ti bom žrtvoval z glasom zahvaljevanja; plačal bom to, kar sem se zaobljubil. Rešitev duš je od Gospoda.«
Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
10 In Gospod je spregovoril ribi in izbljuvala je Jona na kopno zemljo.
Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.