< Jona 1 >

1 Torej Gospodova beseda je prišla k Jonu, Amitájevemu sinu, rekoč:
Yehova anayankhula ndi Yona mwana wa Amitai kuti,
2 »Vstani, pojdi v Ninive, to veliko mesto in kliči zoper njega, kajti njihova zlobnost je prišla predme.«
“Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire motsutsana nawo, chifukwa zoyipa zawo zafika pamaso panga.”
3 Toda Jona se je dvignil, da pred Gospodovo prisotnostjo zbeži v Taršíš in je odšel dol v Jopo in našel ladjo, ki je šla v Taršíš. Tako je plačal njeno voznino in odšel dol vanjo, da gre z njimi v Taršíš, proč od Gospodove prisotnosti.
Koma Yona anathawa Yehova ndi kulowera ku Tarisisi. Anapita ku Yopa, kumene anapeza sitima yapamadzi yopita ku Tarisisi. Atagula chiphaso, anakwera sitimayo kupita ku Tarisisi kuthawa Yehova.
4 Toda Gospod je na morje odposlal velik veter in tam na morju je bil mogočen vihar, tako da je ladjo hotel zlomiti.
Koma Yehova anatumiza chimphepo champhamvu pa nyanja, ndipo panauka namondwe wamphamvu amene anafuna kuphwanya sitimayo.
5 Potem so bili mornarji prestrašeni in vsak je klical k svojemu bogu in odvrgli [so] blago, ki je bilo na ladji, v morje, da jo olajšajo. Jona pa je odšel dol med ladijske boke in legel ter trdno zaspal.
Onse oyendetsa sitimayo anachita mantha ndipo aliyense anayamba kupemphera kwa mulungu wake. Ndipo anaponya katundu mʼnyanja kuti sitimayo ipepuke. Koma Yona pa nthawiyi nʼkuti atatsikira mʼkatikati mwa sitimayo kumene anagona tulo tofa nato.
6 Tako je kapitan prišel k njemu in mu rekel: »Kaj ti misliš, oh zaspanec? Vstani, kliči k svojemu Bogu, če je tako, da bo Bog mislil na nas, da se ne pogubimo.«
Mkulu wa oyendetsa sitimayo anapita kwa iye ndipo anati, “Kodi iwe, nʼchifukwa chiyani ukugona? Dzuka pemphera kwa mulungu wako! Mwina adzatithandiza, ndipo sitidzawonongeka.”
7 In rekli so vsak svojemu tovarišu: »Pridimo in mečimo žrebe, da bomo lahko izvedeli zaradi čigavega vzroka je nad nami to zlo.« Tako so metali žrebe in žreb je padel na Jona.
Ndipo oyendetsa sitimayo anayamba kuwuzana kuti, “Bwerani, tichite maere kuti tipeze amene wabweretsa tsoka limeneli.” Iwo anachita maerewo ndipo anagwera Yona.
8 Potem so mu rekli: »Povej nam, prosimo te, zaradi čigavega vzroka je nad nami to zlo. Kakšen je tvoj poklic? In od kod prihajaš? Katera je tvoja dežela? In iz katerega ljudstva si?«
Tsono anamufunsa kuti, “Tatiwuze, tsoka limeneli latigwera chifukwa chiyani? Umagwira ntchito yanji? Ukuchokera kuti? Kwanu nʼkuti? Ndiwe mtundu wanji wa anthu?”
9 Rekel jim je: »Jaz sem Hebrejec in se bojim Gospoda, Boga nebes, ki je naredil morje in kopno zemljo.«
Iye anayankha kuti, “Ndine Mhebri, ndipo ndimapembedza Yehova, Mulungu Wakumwamba, amene analenga nyanja ndi mtunda.”
10 Potem so bili ljudje silno prestrašeni in mu rekli: »Zakaj si to storil?« Kajti ljudje so vedeli, da je pobegnil izpred Gospodovega obličja, ker jim je povedal.
Izi zinawachititsa mantha kwambiri ndipo anafunsa kuti, “Kodi wachita chiyani?” (Iwo ankadziwa kuti iyeyo amathawa Yehova, chifukwa nʼkuti atawawuza kale).
11 Potem so mu rekli: »Kaj naj ti storimo, da se nam morje lahko umiri?« Kajti morje se je maščevalo in bilo viharno.
Namondwe ananka nakulirakulirabe pa nyanjapo. Tsono anamufunsa iye kuti, “Kodi tikuchite chiyani kuti nyanjayi ikhale bata?”
12 Rekel jim je: »Vzemite me in me vrzite v morje. Tako se vam bo morje umirilo, kajti vem, da je zaradi mene ta veliki vihar nad vami.«
Iye anayankha kuti, “Nyamuleni ndi kundiponya mʼnyanjamu ndipo nyanjayi ikhala bata. Ndikudziwa kuti wolakwa ndine nʼchifukwa chake chimphepo champhamvuchi chabwera pa inu.”
13 Kljub temu so možje trdo veslali, da jo privedejo k obali, toda niso mogli, kajti morje se je maščevalo in bilo viharno proti njim.
Komabe oyendetsa sitimayo anayesetsa kupalasa kwambiri kuti abwerere ku mtunda koma analephera ndithu poti nyanja inawinduka kwambiri kuposa poyamba paja
14 Zato so klicali h Gospodu in rekli: »Rotimo te, oh Gospod, rotimo te, naj se ne pogubimo zaradi življenja tega moža in ne položi na nas nedolžne krvi, kajti ti, oh Gospod, si storil, kakor ti je ugajalo.«
Pamenepo iwo anafuwulira kwa Yehova nati, “Inu Yehova, musalole kuti ife tife chifukwa cha moyo wa munthu uyu. Musatizenge mlandu wa kupha munthu wosalakwa, pakuti ife tachita monga mwakufuna kwanu, Inu Yehova.”
15 Tako so vzeli Jona in ga vrgli v morje in morje je odnehalo od svojega besnenja.
Ndipo anatenga Yona namuponya mʼnyanja, ndipo nyanja yowindukayo inakhala bata.
16 Potem so se možje silno zbali Gospoda in Gospodu darovali klavno daritev in naredili zaobljube.
Anthuwo ataona zimenezi anachita mantha akulu ndi Yehova, ndipo anapereka nsembe kwa Yehova nalumbira kuti adzatumikira Yehovayo.
17 Torej Gospod je pripravil veliko ribo, da je pogoltnila Jona. In Jona je bil v ribjem trebuhu tri dni in tri noči.
Koma Yehova anatuma nsomba yayikulu kuti imeze Yona. Motero Yona anakhala mʼmimba mwa nsombayo masiku atatu, usana ndi usiku.

< Jona 1 >