< Jeremija 6 >

1 »Oh vi, Benjaminovi otroci, zberite se, da zbežite iz srede Jeruzalema in trobite na šofar v Tekói in postavite znamenje ognja v Bet Keremu. Kajti zlo se pojavlja iz severa in veliko uničenje.
“Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
2 Hčer sionsko sem primerjal z ljubko in prefinjeno žensko.
Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
3 Pastirji s svojimi tropi bodo prišli k njej, svoje šotore bodo postavili naokoli nje, vsak bo pasel na svojem kraju.‹«
Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
4 »Pripravite vojno zoper njo. Vstanimo in gremo gor opoldan. Gorje nam! Kajti dan mineva, kajti sence večera so podaljšane.«
Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
5 »Vstanimo in gremo gor ponoči in uničimo njene palače.«
Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
6 Kajti tako je rekel Gospod nad bojevniki: »Posekajte drevesa in nasujte nasip zoper [prestolnico] Jeruzalem. To je mesto, ki bo obiskano; ona je celotno zatiranje v njeni sredi.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
7 Kakor studenec bruha svoje vode, tako ona bruha svojo zlobnost. Nasilje in plen je slišati v njej; žalost in rane so nenehno pred menoj.
Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
8 Bodi poučena, oh [prestolnica] Jeruzalem, da ne bi moja duša odšla od tebe; da te ne bi naredil zapuščeno, deželo, ki ni naseljena.«
Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
9 Tako govori Gospod nad bojevniki: »Temeljito bodo paberkovali Izraelov preostanek kakor trto. Svojo roko obrni nazaj kakor obiralci grozdja v košare.
Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
10 Komu naj govorim in dam svarilo, da bi lahko slišali? Glej, njihovo uho je neobrezano in ne morejo prisluhniti. Glej, Gospodova beseda jim je graja; v njej nimajo veselja.
Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
11 Zato sem poln Gospodove razjarjenosti; izmučen sem z zadrževanjem. Izlil jo bom ven na otroke naokoli in skupaj na zbor mladeničev, kajti vzet bo celo soprog z ženo, ostarel s tistim, ki je izpolnjen z dnevi.
Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
12 Njihove hiše bodo obrnjene k drugim, skupaj z njihovimi polji in ženami, kajti svojo roko bom iztegnil nad prebivalce dežele, « govori Gospod.
Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
13 »Kajti od najmanjših izmed njih, celo do največjih izmed njih, je vsak predan pohlepu, in od preroka, celo do duhovnika, vsak krivo postopa.
“Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
14 Kajti površno so ozdravili rano hčere mojega ljudstva, rekoč: ›Mir, mir, ‹ ko tam ni miru.
Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
15 Mar so bili osramočeni, ko so zagrešili ogabnost? Ne, sploh niso bili osramočeni niti niso mogli zardeti. Zato bodo padli med tistimi, ki padajo. Ob času, ko jih obiščem, bodo vrženi dol, « govori Gospod.
Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
16 Tako govori Gospod: »Ustavite se na poteh in glejte ter vprašajte za starimi stezami, kje je dobra pot, hodite po njej in našli boste počitek svojim dušam.« Rekli pa so: »Mi ne bomo hodili po njej.«
Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
17 Prav tako sem nad vami postavil stražarje, rekoč: »Prisluhnite zvoku šofarja.« Toda rekli so: »Ne bomo prisluhnili.«
Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
18 Zato poslušajte, vi narodi in vedite, oh skupnost, kaj je med njimi.
Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
19 Poslušaj, oh zemlja. Glej, nad to ljudstvo bom privedel zlo, celó sad njihovih misli, ker niso prisluhnili mojim besedam niti moji postavi, temveč so jo zavrnili.
Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
20 S kakšnim namenom prihaja k meni kadilo iz Sabe in prijeten trst iz daljne dežele? Vaše žgalne daritve mi niso sprejemljive niti mi vaše klavne daritve niso prijetne.«
Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
21 Zato tako govori Gospod: »Glej, pred to ljudstvo bom položil kamne spotike in očetje in sinovi bodo skupaj padli nanje; sosed in njegov prijatelj se bosta pogubila.«
Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
22 Tako govori Gospod: »Glej, ljudstvo prihaja iz severne dežele in velik narod bo dvignjen od zemljinih strani.
Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
23 Prijeli bodo lok in sulico; kruti so in nimajo usmiljenja; njihov glas rjovi kakor morje; in jahajo na konjih, postavljeni v vrste kakor možje za vojno zoper tebe, oh sionska hči.
Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
24 »Slišali smo o njihovi slavi. Naše roke so oslabele. Tesnoba se nas je polastila in bolečina kakor žensko v porodnih mukah.
A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
25 Ne pojdi naprej na polje niti ne hodi po poti, kajti sovražnikov meč in strah sta na vsaki strani.«
Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
26 Oh hči mojega ljudstva, opaši se z vrečevino in se valjaj v pepelu. Naredi si žalovanje kakor za edinim sinom, najbolj grenko žalovanje, kajti plenilec bo nenadoma prišel nad nas.
Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
27 Postavil sem te za stolp in trdnjavo med svojim ljudstvom, da lahko spoznaš in preizkusiš njihovo pot.
“Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
28 Vsi so nadležni puntarji, hodijo z obrekovalci. Bron so in železo, vsi so izprijenci.
Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
29 Mehovi so požgani, svinec je použit z ognjem; livar zaman tali, kajti zlobni niso izločeni.
Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
30 Ljudje jih bodo imenovali zavrženo srebro, ker jih je Gospod zavrnil.«
Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”

< Jeremija 6 >