< Jeremija 32 >

1 Beseda, ki je prišla Jeremiju od Gospoda, v desetem letu Judovega kralja Sedekíja, kar je bilo osemnajsto leto Nebukadnezarja.
Yehova anayankhula ndi Yeremiya mʼchaka chakhumi cha Zedekiya mfumu ya Yuda, chimene chinalinso chaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara.
2 Kajti takrat je kralj babilonske vojske oblegal Jeruzalem in prerok Jeremija je bil zaprt na dvorišču ječe, ki je bila v hiši Judovega kralja.
Pa nthawi imeneyi nʼkuti ankhondo a mfumu ya ku Babuloni atazinga Yerusalemu, ndipo mneneri Yeremiya ndiye anamutsekera mʼbwalo la alonda mʼnyumba yaufumu ya ku Yuda.
3 Kajti Judov kralj Sedekíja ga je zaprl, rekoč: »Zakaj prerokuješ in praviš: ›Tako govori Gospod, ›Glejte, to mesto bom izročil v roko babilonskega kralja in on ga bo zavzel.
Tsono Zedekiya mfumu ya Yuda nʼkuti itamutsekera mʼmenemo, ndipo inati, “Nʼchifukwa chiyani ukulosera motero? Iwe ukunena kuti, ‘Yehova akuti: Ndidzapereka mzinda uno kwa mfumu ya ku Babuloni, ndipo idzawulanda.
4 Judov kralj Sedekíja ne bo pobegnil iz roke Kaldejcev, temveč bo zagotovo izročen v roko babilonskega kralja in bo z njim govoril od ust do ust in njegove oči bodo gledale njegove oči,
Zedekiya mfumu ya Yuda sidzapulumuka mʼmanja mwa Ababuloni, koma idzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni. Adzayankhula naye ndi kuonana naye maso ndi maso.
5 in on bo vodil Sedekíja v Babilon in tam bo, dokler ga ne obiščem, ‹ govori Gospod. ›Čeprav se borite s Kaldejci, ne boste uspeli.‹«
Zedekiya adzatengedwa kupita naye ku Babuloni, kumene adzakhale mpaka nditamukhawulitsa, akutero Yehova. Ngakhale iye adzamenyane ndi Babuloni, koma sadzapambana.’”
6 Jeremija je rekel: »K meni je prišla Gospodova beseda, rekoč:
Yeremiya anati, “Yehova wandiwuza kuti:
7 ›Glej, Hanamél, sin tvojega strica Šalúma, bo prišel k tebi, rekoč: ›Kupi si moje polje, ki je v Anatótu, kajti pravica odkupitve je tvoja, da ga kupiš.‹«
Taonani, Hanameli mwana wa Salumu, amalume ako akubwera ndipo adzakuwuza kuti, ‘Gula munda wanga wa ku Anatoti, chifukwa iwe ndiwe mʼbale wanga ndipo ndiwe woyenera kuwuwombola.’”
8 Tako je Hanamél, sin mojega strica, prišel k meni na dvorišče ječe, glede na Gospodovo besedo in mi rekel: »Kupi moje polje, prosim te, ki je v Anatótu, ki je v Benjaminovi deželi, kajti pravica dediščine je tvoja in odkupitev je tvoja; kupi ga zase.« Potem sem vedel, da je bila to Gospodova beseda.
Ndipo monga momwe Yehova ananenera, Hanameli, msuweni wanga anabweradi ku bwalo la alonda ndipo anati, “Gula munda wanga wa ku Anatoti mʼdziko la Benjamini. Popeza ndiwe woyenera kuwugula ndi kukhala wako, gula munda umenewu kuti ukhale wako.” “Ine ndinadziwa kuti amenewa anali mawu a Yehova aja;
9 Polje sem kupil od Hanaméla, sina mojega strica, ki je bil v Anatótu in mu odtehtal denar, celó sedemnajst šeklov srebra.
choncho ndinagula munda wa ku Anatoti kwa Hanameli msuweni wanga, ndipo ndinamupatsa masekeli asiliva 17.
10 Podpisal sem dokaz, ga zapečatil, vzel priče in mu na tehtnici odtehtal denar.
Ndinasayina panganolo ndikulimata pamaso pa mboni, kenaka ndinayeza ndalama zasilivazo pa sikelo.”
11 Tako sem vzel dokaz o nakupu, tako tistega, ki je bil zapečaten glede na postavo in običaj in tistega, ki je bil odprt.
Pambuyo pake ndinatenga makalata anga a pangano, imodzi yomatidwa mʼmene munali malamulo onse a panganolo ndi ina yosamatidwa.
12 Dokaz o nakupu sem dal Nerijájevemu sinu Baruhu, Maasejájevemu sinu, pred očmi Hanaméla, sina mojega strica in v prisotnosti prič, ki so podpisali knjigo o nakupu pred vsemi Judi, ki so sedeli na dvorišču ječe.
Ndinapereka makalatawo kwa Baruki mwana wa Neriya, mdzukulu wa Maseya pamaso pa Hanameli msuweni wanga, pamaso pa mboni zimene zinasayina panganoli ndiponso pamaso pa Ayuda onse okhala mʼbwalo la alonda.
13 Vpričo njih sem Baruhu naročil, rekoč:
“Ndinamulangiza Baruki pamaso pa onsewo kuti,
14 »Tako govori Gospod nad bojevniki, Izraelov Bog: ›Vzemi te dokaze, ta dokaz o nakupu, oba, [tega], ki je zapečaten in ta dokaz, ki je odprt, in ju daj v lončeno posodo, da se bosta lahko ohranila mnogo dni.
‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Tenga makalata awa a umboni wapangano, iyi yokhala ndi chizindikiro ndi yopanda chizindikiro, uwasunge mʼmbiya kuti akhale nthawi yayitali.
15 Kajti tako govori Gospod nad bojevniki, Izraelov Bog: ›V tej deželi boste ponovno imeli v lasti hiše, polja in vinograde.‹«
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Anthu adzagulanso nyumba, minda ndi mitengo yamphesa mʼdziko lino.’”
16 Torej ko sem dokaz o nakupu izročil Nerijájevemu sinu Baruhu, sem molil h Gospodu, rekoč:
Nditamupatsa makalata a panganowa Baruki mwana wa Neriya, ndinapemphera kwa Yehova:
17 »Ah, Gospod Bog! Glej, naredil si nebo in zemljo s svojo veliko močjo in iztegnjenim laktom in zate ni nič pretežko.
“Aa, inu Ambuye Yehova, munalenga dziko lakumwamba ndi dziko lapansi. Munazilenga ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo palibe chokulakani.
18 Ti izkazuješ ljubečo skrbnost tisočim in poplačaš krivičnost očetov v naročje njihovih otrok za njimi. Veliki, Mogočni Bog, Gospod nad bojevniki je njegovo ime,
Mumaonetsa chikondi chanu kwa anthu osawerengeka koma mumalanga ana chifukwa cha machimo a makolo awo. Inu ndinu Mulungu Wamkulu ndi Wamphamvu. Dzina lanu ndinu Yehova Wamphamvuzonse.
19 velik v nasvetu in mogočen v delu, kajti tvoje oči so odprte na vseh poteh človeških sinov, da daš vsakemu glede na njegove poti in glede na sad njegovih ravnanj,
Zolinga zanu ndi zazikulu ndipo zochita zanu ndi zamphamvu. Maso anu amaona zonse zimene anthu amachita. Mumapereka mphotho kwa munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndi ntchito zake.
20 ki si postavil znamenja in čudeže v egiptovski deželi, celó do današnjega dne in v Izraelu in med drugimi ljudmi, in si si naredil ime, kakor na ta dan.
Inu munachita zizindikiro zozizwitsa ku Igupto, ndipo mwakhala mukuzichita mpaka lero, pakati pa Aisraeli ndiponso pakati pa anthu onse. Choncho mwadzitchukitsa mpaka lero lino.
21 Svoje ljudstvo Izrael si izpeljal iz egiptovske dežele, z znamenji in s čudeži, z močno roko, z iztegnjenim laktom in z veliko strahoto
Munatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu pochita zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene zinaopseza adani anu.
22 in jim dal to deželo, ki si jo prisegel njihovim očetom, da jim jo daš, deželo, kjer tečeta mleko in med.
Munawapatsa dziko lino limene munalonjeza mwalumbiro kulipereka kwa makolo awo, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
23 Vstopili so vanjo in jo vzeli v last, toda niso ubogali tvojega glasu niti hodili po tvoji postavi. Od vsega, kar si jim zapovedal storiti, niso storili ničesar. Zato si storil, da pride nadnje vse to zlo.
Iwo analowa nʼkulitenga kukhala lawo, koma sanamvere Inu kapena kutsatira lamulo lanu; ndipo sanachite zomwe munawalamula. Choncho inu mwawagwetsera masautso onsewa.”
24 Glej okope, prišli so v mesto, da ga zavzamejo; in mesto je izročeno v roko Kaldejcem, ki se borijo zoper njega zaradi meča, zaradi lakote in zaradi kužne bolezni in kar si govoril, se je zgodilo; in glej, ti to vidiš.
“Onani momwe adani azingira ndi mitumbira yankhondo mzindawu kuti awulande ndipo akuwuthira nkhondo. Chifukwa cha lupanga, njala ndi mliri. Mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni anthu atafowoka ndi nkhondo, njala ndi mliri. Zimene munkanena zija zachitikadi monga mukuzionera tsopano.
25 Ti, oh Gospod Bog, si mi rekel: ›Kupi si polje za denar in vzemi priče, kajti mesto je izročeno v roko Kaldejcem.‹«
Ngakhale mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni, komabe Inu Ambuye Yehova, munandiwuza kuti, ‘Gula munda ndi siliva ndipo upereke ndalamazo pali mboni.’”
26 Potem je prišla beseda od Gospoda Jeremiju, rekoč:
Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti,
27 »›Glej, jaz sem Gospod, Bog vsega mesa, ali je zame katerakoli stvar pretežka?‹
“Taonani, Ine ndine Yehova, Mulungu wa anthu onse. Kodi chilipo chinthu choti Ine nʼkundikanika?
28 Zato tako govori Gospod: ›Glej, to mesto bom izročil v roko Kaldejcev in v roko babilonskega kralja Nebukadnezarja in ta ga bo zavzel.
Nʼchifukwa chake ine Yehova ndikuti: Ndidzawupereka mzinda uno kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulanda.
29 Kaldejci, ki se borijo zoper to mesto, bodo prišli in vžgali ogenj nad tem mestom in ga zažgali, s hišami, na katerih strehah so darovali kadilo Báalu in izlivali pitne daritve drugim bogovom, da me dražijo do jeze.
Ndipo Ababuloni amene akuwuthira nkhondo mzinda uno adzalowa ndi kuwutentha; adzatentha ndi kugwetsa nyumba zimene pa denga pake anthu ankandipsetsa mtima pofukiza lubani kwa Baala ndi popereka chopereka cha chakumwa kwa milungu ina.
30 Kajti Izraelovi otroci in Judovi otroci so od svoje mladosti pred menoj počeli zgolj zlo, kajti Izraelovi otroci so me z deli svojih rok samo dražili do jeze, ‹ govori Gospod.
“Aisraeli ndi Ayuda akhala akuchita zoyipa zokhazokha pamaso panga kuyambira ubwana wawo. Kunena zoona Aisraeli akumandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa, akutero Yehova.
31 ›Kajti to mesto mi je bilo kakor izzivanje moje jeze in moje razjarjenosti od dneva, ko so ga zgradili, celo do današnjega dne, da bi ga odstranil izpred svojega obraza,
Kuyambira tsiku limene mzindawu unamangidwa mpaka lero, wakhala ukuwutsa mkwiyo wanga ndi ukali wanga. Nʼchifukwa chake ndiyenera kuwuchotsa pamaso panga.
32 zaradi vsega zla Izraelovih otrok in Judovih otrok, ki so ga storili, da me dražijo k jezi, oni, njihovi kralji, njihovi princi, njihovi duhovniki, njihovi preroki, Judovi možje in prebivalci Jeruzalema.
Aisraeli ndi Ayuda, anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, mafumu awo, nduna zawo, ansembe ndi aneneri awo anandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa.
33 Obrnili so mi hrbet in ne obraza, čeprav sem jih učil, zgodaj vzdigoval in jih učil, vendar niso prisluhnili, da bi sprejeli poučevanje.
Anandifulatira ndipo ngakhale ndinakhala ndikuwaphunzitsa kawirikawiri, sanamve kapena kuphunzirapo kanthu.
34 Temveč so v hišo, ki je imenovana z mojim imenom, postavili svoje ogabnosti, da jo omadežujejo.
Iwo anayika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi dzina langa ndipo anayipitsa.
35 Zgradili so visoke kraje Báalu, ki so v dolini sina Hinómovega, da svojim sinovom in svojim hčeram povzročijo, da gredo skozi ogenj k Molohu; kar jim nisem zapovedal niti mi ni prišlo na misel, da storijo to ogabnost, da Judu povzročijo, da greši.‹
Anamanga malo opembedzerapo Baala mʼChigwa cha Hinomu kuti aziperekapo ana awo aamuna ndi aakazi ngati nsembe kwa Moleki. Ine sindinawalamulire kutero, ndipo sindinaganizepo nʼkomwe kuti iwo angachite chinthu chonyansa chotero, ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda.
36 Sedaj torej tako govori Gospod, Izraelov Bog, glede tega mesta, o katerem pravite: ›Izročen bo v roko babilonskega kralja, z mečem, z lakoto in s kužno boleznijo.
“Anthu ponena za mzindawu akuti udzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni mwa nkhondo, njala ndi mliri, koma Yehova Mulungu wa Israeli akuti,
37 Glejte, zbral jih bom iz vseh dežel, kamor sem jih pognal v svoji jezi, v svoji razjarjenosti in v velikem besu; in ponovno jih bom privedel na ta kraj in povzročil jim bom, da varno prebivajo.
Ine ndidzawasonkhanitsadi anthuwa kuchokera ku mayiko onse kumene ndinawapirikitsira ndili wokwiya ndi waukali kwambiri. Ndidzabwera nawo ku malo ano ndipo ndidzawalola kukhala mwamtendere.
38 Oni bodo moje ljudstvo in jaz bom njihov Bog.
Iwo adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
39 Dal jim bom eno srce in eno pot, da se me bodo lahko bali na veke, v dobro njim in njihovim otrokom za njimi.
Ndidzawapatsa mtima umodzi ndi khalidwe limodzi kotero kuti azidzandiopa nthawi zonse ndipo iwo pamodzi ndi zidzukulu zawo zinthu zidzawayendera bwino.
40 Z njimi bom sklenil večno zavezo, da se ne bom odvrnil proč od njih, da jim delam dobro; toda svoj strah bom položil v njihova srca, da ne bodo odšli od mene.
Ndidzachita nawo pangano losatha: sindidzaleka kuwachitira zabwino, ndipo ndidzawapatsa mtima woti azidzandiopa, kuti asadzandisiyenso.
41 Da, razveseljeval se bom nad njimi, da jim delam dobro in v tej deželi jih bom zagotovo sadil s svojim celotnim srcem in s svojo celotno dušo.‹
Ndidzakondwera powachitira zabwino, ndipo ndidzawakhazikitsa ndithu mʼdziko lino ndi mtima wanga wonse ndi moyo wanga wonse.
42 Kajti tako govori Gospod: ›Kakor sem privedel vse to veliko zlo nad to ljudstvo, tako bom nadnje privedel vse dobro, ki sem jim ga obljubil.
“Yehova akuti: Monga momwe ndinagwetsera masautso aakulu onsewa pa anthuwa, momwemonso ndidzawapatsa zinthu zonse zabwino zimene ndinawalonjeza.
43 Polja se bodo kupovala v tej deželi, o kateri pravite: › Ta je zapuščena, brez človeka ali živali; ta je izročena v roko Kaldejcem.‹
Adzagulanso minda mʼdziko muno, limene inu mukuti, ‘Ndi dziko losiyidwa, lopanda anthu kapena nyama, pakuti linaperekedwa kwa Ababuloni.’
44 Ljudje bodo polja kupovali za denar, podpisovali dokaze, jih pečatili in jemali priče v Benjaminovi deželi in v krajih okoli Jeruzalema, v Judovih mestih, gorskih mestih, dolinskih mestih in v mestih na jugu, kajti jaz bom njihovemu ujetništvu povzročil, da se vrne, ‹ govori Gospod.«
Adzagula minda ndi ndalama zasiliva, ndipo achita pangano, ndi kumata pamaso pa mboni. Izi zidzachitika mʼdziko la Benjamini, ku malo ozungulira Yerusalemu, mʼmizinda ya Yuda, mʼmizinda ya ku mapiri, mʼmizinda ya kuchigwa ndi yakummwera ku Negevi. Zoona, ndidzabwezera ufulu wawo, akutero Yehova.”

< Jeremija 32 >