< Izaija 53 >
1 Kdo je veroval našemu poročilu? In komu se je razodel Gospodov laket?
Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
2 Kajti pred njim bo pognal kakor nežna rastlina in kakor korenina iz suhih tal. Nima oblike niti ljubkosti in ko ga bomo videli, ni lepote, da bi ga želeli.
Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
3 Preziran je in zavrnjen od ljudi, mož bridkosti in seznanjen z žalostjo in mi smo, kakor bi skrili svoje obraze pred njim; bil je preziran, mi pa ga nismo cenili.
Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
4 Zagotovo je nosil naše žalosti in prenašal naše bridkosti, vendar smo ga imeli [za] zadetega, udarjenega od Boga in trpečega.
Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
5 Toda ranjen je bil zaradi naših prestopkov, poškodovan je bil zaradi naših krivičnosti. Kazen za naš mir je bila na njem in z njegovimi udarci z bičem smo ozdravljeni.
Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
6 Vsi smo zašli kakor ovce, obrnili smo se vsak k svoji lastni poti in Gospod je nanj položil krivičnost nas vseh.
Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
7 Bil je zatiran in trpel, vendar ni odprl svojih ust. Priveden je kakor jagnje h klanju in kakor je ovca pred svojimi strižci nema, tako on ne odpre svojih ust.
Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
8 Vzet je bil iz ječe in iz sodbe in kdo bo razglasil njegov rod? Kajti odrezan je bil iz dežele živih, zaradi prestopka mojega ljudstva je bil udarjen.
Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
9 Njegov grob v njegovi smrti mu je določil z zlobnimi in z bogatimi, čeprav ni storil nobenega nasilja niti ni bilo nobene prevare v njegovih ustih.
Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
10 Vendar je Gospodu ugajalo, da ga rani; položil ga je v žalost. Ko boš naredil njegovo dušo v daritev za greh, bo videl svoje seme, podaljšal bo svoje dni in Gospodovo zadovoljstvo bo uspevalo v njegovi roki.
Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
11 Videl bo muko svoje duše in bo zadovoljen. S svojim spoznanjem bo moj pravični služabnik opravičil mnoge, kajti nosil bo njihove krivičnosti.
Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
12 Zato mu bom razdelil delež z velikimi in plen bo razdelil z močnimi, zato ker je svojo dušo izlil do smrti in prištet je bil med prestopnike; nosil je greh mnogih in opravil posredovanje za prestopnike.
Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.