< Izaija 43 >

1 Toda sedaj tako govori Gospod, ki te je ustvaril, oh Jakob in tisti, ki te je oblikoval, oh Izrael: »Ne boj se, kajti odkupil sem te, poklical sem te s tvojim imenom, moj si.
Koma tsopano, Yehova amene anakulenga, iwe Yakobo, amene anakuwumba, iwe Israeli akuti, “Usaope, pakuti ndakuwombola; Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
2 Ko hodiš skozi vode, bom s teboj in skozi reke, te ne bodo preplavile. Ko hodiš skozi ogenj, ne boš ožgan niti se plamen ne bo vnel na tebi.
Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe; ndipo pamene ukuwoloka mitsinje, sidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto, sudzapsa; lawi la moto silidzakutentha.
3 Kajti jaz sem Gospod, tvoj Bog, Sveti Izraelov, tvoj Odrešenik. Egipt sem dal za tvojo odkupnino, Etiopijo in Sebo zate.
Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako, Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako. Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe, ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
4 Ker si bil dragocen v mojem pogledu, bil si častitljiv in jaz sem te ljubil. Zato bom zate dal ljudi in ljudstva za tvoje življenje.
Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga, ndipo chifukwa ndimakukonda, ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe, ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
5 Ne boj se, kajti jaz sem s teboj. Tvoje seme bom privedel od vzhoda in te zbral od zahoda.
Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe; ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa, ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
6 Severu bom rekel: ›Izroči‹ in jugu: ›Ne zadržuj.‹ Moje sinove privedi od daleč in moje hčere od koncev zemlje,
Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’ ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’ Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali, ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
7 celó vsakega, ki je klican z mojim imenom, kajti jaz sem ga ustvaril za svojo slavo, jaz sem ga oblikoval; da, jaz sem ga naredil.
onsewo amadziwika ndi dzina langa; ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndinawawumba, inde ndinawapanga.”
8 Privedi slepo ljudstvo, ki ima oči in gluhe, ki imajo ušesa.
Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya, anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.
9 Naj bodo vsi narodi zbrani skupaj in naj bo ljudstvo zbrano. Kdo izmed njih lahko to razglasi in nam pokaže prejšnje stvari? Naj privedejo naprej svoje priče, da bodo lahko opravičeni. Ali naj slišijo in rečejo: › To je resnica.‹
Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi, anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu. Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi? Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale? Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona, kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”
10 Vi ste moje priče, ‹ govori Gospod in moj služabnik, ki sem ga izbral, da me boste lahko poznali in mi verjeli in razumeli, da jaz sem ta. Pred menoj ni bil oblikovan noben Bog niti ne bo za menoj.
Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga, ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha, kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina, ngakhale pambuyo panga sipadzakhalaponso wina.”
11 Jaz, celó jaz sem Gospod in poleg mene ni rešitelja.
Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova, ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.
12 Razglasil sem, rešil in pokazal, ko med vami ni bilo nobenega tujega boga. Zato ste vi moje priče, ‹ govori Gospod, ›da jaz sem Bog.
Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa; ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu. Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.
13 Da, preden je bil dan, jaz sem in nobenega ni, ki lahko osvobodi iz moje roke. Delal bom in kdo bo to dopustil?‹
“Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse. Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga, ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”
14 Tako govori Gospod, vaš odkupitelj, Sveti Izraelov: ›Zaradi vas sem poslal v Babilon in ponižal vse njihove plemiče in Kaldejce, katerih vpitje je na ladjah.
Yehova akuti, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni ndi kukupulumutsani. Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
15 Jaz sem Gospod, vaš Sveti, stvarnik Izraela, vaš Kralj.‹
Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”
16 Tako govori Gospod, ki dela pot v morju in stezo v mogočnih vodah,
Yehova anapanga njira pa nyanja, anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.
17 ki privede naprej bojni voz in konja, vojsko in moč; skupaj se bodo ulegli, ne bodo vstali. Izumrli so, pogašeni so kakor predivo.
Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo, gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu, ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,
18 Ne spominjajte se prejšnjih stvari niti ne preudarjajte stvari od davnine.
“Iwalani zinthu zakale; ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
19 Glejte, storil bom novo stvar. Sedaj bo ta vzbrstela; mar tega ne boste spoznali? Naredil bom celo pot v divjini in reke v puščavi.
Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano! Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona? Ine ndikulambula msewu mʼchipululu ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
20 Divja žival polja me bo spoštovala, zmaji in sove, ker dam vode v divjino in reke v puščavo, da dam piti svojemu ljudstvu, svojim izbranim.
Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi zinandilemekeza. Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma kuti ndiwapatse madzi anthu anga osankhidwa.
21 To ljudstvo sem oblikoval zase, naznanjali bodo mojo hvalo.
Anthu amene ndinadziwumbira ndekha kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.
22 Toda ti nisi klical k meni, oh Jakob, temveč si se me naveličal, oh Izrael.
“Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo, munatopa nane, Inu Aisraeli.
23 Nisi mi privedel majhne živine od svojih žgalnih daritev niti me nisi častil s svojimi klavnimi daritvami. Nisem ti storil, da služiš z daritvijo niti te nisem mučil s kadilom.
Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza, kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu. Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
24 Z denarjem mi nisi kupil nobenega sladkornega trsta niti me nisi nasičeval s tolščo svojih klavnih daritev, temveč si me s svojimi grehi primoral, da služim; izmučil si me s svojimi krivičnostmi.
Simunandigulire bango lonunkhira kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu. Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.
25 Jaz, celó jaz, sem tisti, ki zaradi sebe izbrisujem tvoje prestopke in se ne bom spominjal tvojih grehov.
“Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini, ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
26 Spomni me, skupaj se pravdajva. Ti razglasi, da boš lahko opravičen.
Mundikumbutse zakale, ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi; fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.
27 Tvoj prvi oče je grešil in tvoji učitelji so se pregrešili zoper mene.
Kholo lanu loyamba linachimwa; ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.
28 Zato sem oskrunil prince svetišča in dal Jakoba v prekletstvo in Izraela v graje.
Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero, ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”

< Izaija 43 >