< Izaija 41 >
1 Molčite pred menoj, oh otoki in naj ljudstvo obnavlja svojo moč. Naj pridejo bliže, potem jim pustite govoriti. Pridimo blizu skupaj k sodbi.
“Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja! Alekeni ayandikire ndi kuyankhula; tiyeni tikhale pamodzi kuti atiweruze.
2 Kdo je dvignil pravičnega človeka od vzhoda in ga poklical k svojemu stopalu, dal predenj narode in ga naredil, [da] vlada nad kralji? Izročil jih je kakor prah njegovemu meču in kakor slamo gnano k njegovemu loku.
“Ndani anadzutsa wochokera kummawa uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita? Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
3 Zasledoval jih je in varno prešel; celó po poti, [po] kateri [še] ni šel s svojimi stopali.
Amawalondola namayenda mosavutika, mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
4 Kdo je delal in to storil, kličoč rodove od začetka? Jaz, Gospod, prvi in s poslednjimi; jaz sem ta.
Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza, si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu? Ine Yehova, ndine chiyambi ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”
5 Otoki so to videli in se bali; konci zemlje so bili prestrašeni, se približali in prišli.
Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa; anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera. Akuyandikira pafupi, akubwera;
6 Pomagali so vsak svojemu sosedu in vsak je svojemu bratu rekel: »Bodi odločnega poguma.«
aliyense akuthandiza mnzake ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
7 Tako je tesar hrabril zlatarja in kdor gladi s kladivom, tistega, ki udarja nakovalo, rekoč: »Ta je pripravljen za spajanje« in ga pritrdil z žeblji, da ta ne bi bil premaknjen.
Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide, ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala. Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.” Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.
8 Toda ti, Izrael, si moj služabnik, Jakob, ki sem ga izbral, seme Abrahama, mojega prijatelja.
“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga, Yakobo amene ndakusankha, Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
9 Ti, ki sem te vzel od koncev zemlje in te poklical od njihovih glavnih mož in ti rekel: »Ti si moj služabnik, izbral sem te in te nisem zavrgel.
Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi, ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi. Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’ Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
10 Ne boj se, kajti jaz sem s teboj. Ne bodi potrt, kajti jaz sem tvoj Bog. Okrepil te bom, da, jaz ti bom pomagal, da, podpiral te bom z desnico svoje pravičnosti.
Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe; usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.
11 Glej, vsi tisti, ki so bili ogorčeni zoper tebe, bodo osramočeni in zbegani. Oni bodo kakor nič in tisti, ki se prepirajo s teboj, bodo propadli.
“Onse amene akupsera mtima adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa; onse amene akukangana nawe sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
12 Iskal jih boš in jih ne boš našel, celó tiste, ki so se pričkali s teboj. Tisti, ki se vojskujejo zoper tebe, bodo kakor nič in kakor stvar ničnosti.
Udzafunafuna adani ako, koma sadzapezeka. Iwo amene akuchita nawe nkhondo sadzakhalanso kanthu.
13 Kajti jaz, Gospod, tvoj Bog, bom držal tvojo desnico, rekoč ti: »Ne boj se, jaz ti bom pomagal.«
Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako, amene ndikukugwira dzanja lako lamanja ndipo ndikuti, usaope; ndidzakuthandiza.
14 Ne boj se, ti ličinka Jakob in vi, Izraelovi možje, pomagal ti bom, govori Gospod in tvoj odkupitelj, Sveti Izraelov.
Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi, iwe wochepa mphamvu Israeli, chifukwa Ine ndidzakuthandiza,” akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
15 Glej, naredil te bom [za] novo ostro mlatilno pripravo z zobmi. Mlatil boš gore, jih razdrobil in hribe boš naredil kakor pleve.
“Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri. Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya, ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
16 Vejál jih boš in veter jih bo odnesel proč in vrtinčast veter jih bo razkropil, ti pa se boš razveseljeval v Gospodu in slavil boš v Svetem Izraelovem.
Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso adzamwazika ndi kamvuluvulu. Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako, ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:
17 Kadar ubogi in pomoči potrebni iščejo vode in je tam ni in njihov jezik odpoveduje zaradi žeje, jih bom jaz, Gospod, uslišal in jaz, Izraelov Bog, jih ne bom zapustil.
“Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi, koma sakuwapeza; ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu. Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo; Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
18 Odprl bom reke na visokih krajih in studence v sredi dolin. Divjino bom spremenil [v] vodni ribnik in suho deželo [v] izvire voda.
Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma, ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa. Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
19 V divjini bom zasadil cedro, akacijevo drevo, mirto in olivno drevo; v puščavi bom skupaj posadil cipreso, bor in pušpan,
Mʼchipululu ndidzameretsa mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi. Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
20 da bodo lahko videli, spoznali, preudarili in skupaj razumeli, da je to storila Gospodova roka in Sveti Izraelov je to ustvaril.
kuti anthu aone ndi kudziwa; inde, alingalire ndi kumvetsa, kuti Yehova ndiye wachita zimenezi; kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.
21 Prinesite svojo pravdo, ‹ govori Gospod; ›prinesite naprej svoje močne razloge, govori Kralj Jakobov.
“Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’ Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
22 Naj jih prinesejo naprej in nam pokažejo kaj se bo zgodilo. Naj nam pokažejo prejšnje stvari, kakršne so, da jih lahko preudarimo in spoznamo njihov zadnji konec; ali nam oznanite stvari, ki pridejo.
Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze zomwe zidzachitike mʼtsogolo. Tifotokozereni zinthu zamakedzana tiziganizire ndi kudziwa zotsatira zake. Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
23 Pokažite stvari, ki bodo odslej, da bomo lahko vedeli, da ste vi bogovi. Da, delajte dobro ali delajte zlo, da bomo lahko zaprepadeni in to skupaj gledali.
tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani, ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu. Chitani chinthu chabwino kapena choyipa, ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
24 Glejte, vi ste od ničnosti in vaše delo je ničevo; ogabnost je, kdor vas izbere.
Koma inu sindinu kanthu ndipo zochita zanu nʼzopandapake; amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.
25 Dvignil sem nekoga iz severa in bo prišel. Od sončnega vzhoda bo klical moje ime in prišel bo nad prince kakor nad malto in kakor lončar gnete ilo.
“Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera, munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana. Amapondaponda olamulira ngati matope, ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
26 Kdo je razglasil od začetka, da bi mi lahko vedeli? In poprej, da bi lahko rekli: » On je pravičen?« Da, tam ni nikogar, ki kaže; da, tam ni nikogar, ki razglaša; da, tam ni nikogar, ki sliši vaše besede.
Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe, kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’ Palibe amene ananena, palibe analengeza zimenezi, palibe anamva mawu anu.
27 Prvi bo rekel Sionu: »Poglej, poglej jih.« In Jeruzalemu bom dal nekoga, ki prinaša dobre novice.
Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’ Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
28 Kajti gledal sem in tam ni bilo človeka, celo med njimi in tam ni bilo svetovalca, da bi lahko, ko sem jih povprašal, odgovoril besedo.
Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe, palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu, palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
29 Glej, vsi so ničnost, njihova dela so nič. Njihove ulite podobe so veter in zmešnjava.
Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo! Zochita zawo si kanthu konse; mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.