< Ozej 14 >
1 Oh Izrael, vrni se h Gospodu, svojemu Bogu, kajti padel si zaradi svoje krivičnosti.
Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
2 S seboj vzemite besede in se obrnite h Gospodu. Recite mu: ›Odvzemi proč vso krivičnost in nas milostljivo sprejmi, tako bomo povrnili teleta svojih ustnic.‹
Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
3 Asúr nas ne bo rešil, ne bomo jahali na konjih niti delu naših rok ne bomo več rekli: › Vi ste naši bogovi, ‹ kajti v tebi osiroteli najde usmiljenje.
Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
4 Jaz bom ozdravil njihov odpad, velikodušno jih bom ljubil, kajti moja jeza se je odvrnila od njega.
Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
5 Izraelu bom kakor rosa. Rasel bo kakor lilija in svoje korenine poganjal kakor Libanon.
Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
6 Njegove mladike se bodo razširile in njegova lepota bo kakor oljka in njegov vonj kakor Libanon.
mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
7 Tisti, ki prebivajo pod njegovo senco, se bodo vrnili; oživeli bodo kakor žito in rastli kakor trta. Njegova vonjava bo kakor libanonsko vino.
Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
8 Efrájim bo rekel: ›Kaj imam še opraviti z maliki?‹ Slišal sem ga in ga opazil. Podoben sem zeleni cipresi. Od mene je najti tvoj sad.
Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
9 Kdo je moder in bo razumel te stvari? Razsoden in jih bo spoznal? Kajti Gospodove poti so pravilne in pravični se bo ravnal po njih. Toda prestopniki bodo padli na njih.«
Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.