< 1 Mojzes 13 >

1 Abram se je dvignil iz Egipta na jug, on in njegova žena in vse, kar je imel in Lot z njim.
Choncho Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo, anachoka ku Igupto kupita ku Negevi. Loti naye anapita nawo.
2 Abram je bil zelo bogat z živino, s srebrom in z zlatom.
Abramu anali wolemera kwambiri; anali ndi ziweto ndiponso siliva ndi golide.
3 Odšel je na svoja potovanja od juga celó do Betela, na kraj, kjer je bil od začetka njegov šotor, med Betelom in Ajem,
Atachoka ku Negevi, anayenda malo osiyanasiyana mpaka anafika ku Beteli, ku malo a pakati pa Beteli ndi Ai, kuja kumene anamanga tenti poyamba,
4 na kraj z oltarjem, ki ga je tam najprej naredil in tam je Abram klical h Gospodovemu imenu.
ndiponso kumene Abramu anamangira Yehova guwa lansembe kwa nthawi yoyamba ndi kupemphera mʼdzina la Yehova.
5 Tudi Lot, ki je odšel z Abramom, je imel trope, črede in šotore.
Loti amene ankayendayenda ndi Abramu nayenso anali ndi ziweto zosiyanasiyana ndi matenti.
6 Zemlja pa ju ni mogla podpirati, da bi lahko prebivala skupaj, kajti njuno imetje je bilo veliko, tako da nista mogla prebivati skupaj.
Motero dziko linayamba kuwachepera kuti onse nʼkukhala pamodzi, popeza katundu wawo anali wochuluka kwambiri moti sakanatha kukhala pamodzi.
7 Bil pa je prepir med čredniki Abramove živine in čredniki Lotove živine, in takrat so v deželi prebivali Kánaanci in Perizéjci.
Mikangano inayambika pakati pa abusa a Abramu ndi abusa a Loti. Nthawi imeneyo nʼkuti Akanaani ndi Aperezi akukhalanso mʼdziko lomwelo.
8 Abram je rekel Lotu: »Naj ne bo prepira, prosim te, med menoj in teboj in med mojimi čredniki in med tvojimi čredniki, kajti mi smo bratje.
Tsono Abramu anati kwa Loti, “Pasakhale mikangano pakati pa iwe ndi ine kapena pakati pa abusa ako ndi anga, popeza ndife abale.
9 Mar ni vsa dežela pred teboj? Prosim te, loči se od mene. Če boš vzel levico, potem bom odšel na desno, ali če ti odideš na desnico, potem bom jaz odšel na levo.«
Kodi dziko lonseli silili pamaso pako? Tiye tisiyane. Iwe ukalowera kumanzere, ine ndilowera kumanja; ukalowera kumanja, ine ndipita kumanzere.”
10 Lot je povzdignil svoje oči in pogledal vso jordansko ravnino, ki je bila, preden je Gospod uničil Sódomo in Gomóro, vsepovsod dobro namakana, kakor Gospodov vrt, podobna egiptovski deželi, ko prideš do Coarja.
Loti atamwazamwaza maso anaona kuti chigwa chonse cha mtsinje wa Yorodani chinali chothiriridwa bwino ngati munda wa Yehova, kapena ngati dziko la ku Igupto mpaka ku Zowari. (Nthawi iyi nʼkuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora).
11 Potem si je Lot izbral vso Jordansko ravnino in Lot je odpotoval vzhodno in ločila sta se drug od drugega, eden od drugega.
Choncho Loti anadzisankhira yekha chigwa chonse cha Yorodani nanyamuka kulowera cha kummawa. Choncho anthu awiriwa anasiyana.
12 Abram je prebival v kánaanski deželi, Lot pa je prebival v mestih ravnine in svoj šotor postavljal v smeri Sódome.
Abramu anakhala mʼdziko la Kanaani, pamene Loti anakakhala pakati pa mizinda ikuluikulu ya mʼchigwamo. Anamanga tenti yake pafupi ndi Sodomu.
13 Toda sódomski možje so bili zlobni in silni grešniki pred Gospodom.
Tsono anthu a ku Sodomu anali oyipa ndiponso ankachimwira Yehova kwambiri.
14 Gospod je rekel Abramu, potem ko je bil Lot ločen od njega: »Dvigni torej svoje oči in poglej, od kraja, kjer si, proti severu, proti jugu, proti vzhodu in proti zahodu.
Loti atachoka, Yehova anati kwa Abramu, “Kuchokera pamene ulipo tayangʼanayangʼana cha kumpoto, kummwera, kummawa ndi kumadzulo.
15 Kajti vso deželo, ki jo vidiš, bom dal tebi in tvojemu potomstvu na veke.
Dziko lonse ukulionalo ndidzalipereka kwa iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.
16 Tvojega semena bom naredil kakor zemeljskega prahu, tako da če človek lahko prešteje zemeljski prah, potem bo prešteto tudi tvoje seme.
Ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati fumbi lapansi moti amene angathe kuwerenga fumbilo ndiye kuti angathenso kuwerenga zidzukulu zako.
17 Vstani, prehodi deželo po njeni dolžini in po njeni širini, kajti tebi jo bom dal.«
Dzuka ndipo uyendere dziko lonseli mulitali ndi mulifupi pakuti ndalipereka kwa iwe.”
18 Potem je Abram odstranil svoj šotor in prišel ter prebival na mamrejski ravnini, ki je v Hebrónu in tam zgradil oltar Gospodu.
Choncho Abramu anasamutsa tenti yake napita kukakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ija ya thundu ya ku Mamre ku Hebroni, kumene anamangira Yehova guwa lansembe.

< 1 Mojzes 13 >