< Ezekiel 30 >

1 Beseda Gospodova je ponovno prišla k meni, rekoč:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 »Človeški sin, prerokuj in reci: ›Tako govori Gospod Bog: ›Tulite: ›Dan, vreden gorja!‹‹
“Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena. “‘Ufuwule mawu awa akuti, ‘Kalanga, tsiku lafika!’
3 Kajti dan je blizu, celo Gospodov dan je blizu, oblačen dan; to bo čas poganov.
Pakuti tsiku layandikira, tsiku la Yehova lili pafupi, tsiku la mitambo yakuda, tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.
4 Meč bo prišel nad Egipt in velika bolečina bo v Etiopiji, ko bodo umorjeni padli v Egiptu in bodo proč odpeljali njegovo množico in njegovi temelji bodo zrušeni.
Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto ndipo mavuto adzafika pa Kusi. Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto, chuma chake chidzatengedwa ndipo maziko ake adzagumuka.
5 Etiopija, Libija in Ludéja in vsa pomešana ljudstva in Kub in možje dežele, ki je v zavezi, bodo z njimi padli pod mečem.‹
Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.
6 Tako govori Gospod: ›Tudi tisti, ki podpirajo Egipt, bodo padli; in ponos njegove oblasti se bo zrušil. Od siénskega stolpa bodo v njem padli pod mečem, ‹ govori Gospod Bog.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu. Adzaphedwa ndi lupanga kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’” ndikutero Ine Ambuye Yehova.
7 ›In opustošeni bodo v sredi dežel, ki so opustošene in njegova mesta bodo v sredi mest, ki so opustošena.
“‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja kupambana mabwinja ena onse opasuka, ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka kupambana mizinda ina yonse.
8 In spoznali bodo, da jaz sem Gospod, ko sem dal ogenj v Egipt in ko bodo vsi njegovi pomočniki uničeni.
Nditatha kutentha Igupto ndi kupha onse omuthandiza, pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
9 Na tisti dan bodo poslanci šli pred menoj na ladjah, da prestrašijo brezskrbne Etiopijce in velika bolečina bo prišla nadnje kakor na dan Egipta, kajti, glej, ta prihaja.‹
“‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.
10 Tako govori Gospod Bog: ›Tudi egiptovski množici bom storil, da odneha po roki babilonskega kralja Nebukadnezarja.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.
11 On in njegovo ljudstvo z njim, strašni izmed narodov, bodo privedeni, da uničijo deželo in svoje meče bodo izvlekli zoper Egipt in deželo napolnili z umorjenimi.
Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja adzabwera kudzawononga dzikolo. Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.
12 Posušil bom reke in deželo prodal v roko zlobnega, in deželo in vse, kar je v njej, bom naredil opustošenje po roki tujcev. Jaz, Gospod sem to govoril.‹
Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa. Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo. Ine Yehova ndayankhula.
13 Tako govori Gospod Bog: ›Prav tako bom uničil malike in njihovim podobam bom povzročil, da bodo izginile iz Nofa; in tam ne bo nič več princa iz egiptovske dežele, in na egiptovsko deželo bom položil strah.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzawononga mafano ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi. Simudzakhalanso mfumu mu Igupto, ndipo ndidzaopseza dziko lonse.
14 Patrós bom naredil zapuščen in prižgal bom ogenj na Coanu in izvršil bom sodbe v Noju.
Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi, ndi kutentha mzinda wa Zowani. Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.
15 In svojo razjarjenost bom izlil nad Sin, moč Egipta; in iztrebil bom množico iz Noja.
Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu, linga lolimba la Igupto, ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.
16 Zanetil bom ogenj v Egiptu. Sin bo imel veliko bolečino in No bo raztrgan in Nof bo imel dnevne tegobe.
Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto; Peluziumu adzazunzika ndi ululu. Malinga a Thebesi adzagumuka, ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.
17 Mladeniči iz Avena in iz Pi Beseta bodo padli pod mečem, in ta mesta bodo šla v ujetništvo.
Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti adzaphedwa ndi lupanga ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.
18 Tudi v Tahpanhésu bo dan otemnel, ko bom tam zlomil egiptovske jarme, in pomp njegove moči bo prenehal v njem. Kar se tiče njega, oblak ga bo pokril in njegove hčere bodo šle v ujetništvo.
Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima pamene ndidzathyola goli la Igupto; motero kunyada kwake kudzatha. Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda, ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.
19 Tako bom izvršil sodbe v Egiptu, in spoznali bodo, da jaz sem Gospod.‹«
Kotero ndidzalanga dziko la Igupto, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
20 In pripetilo se je v enajstem letu, v prvem mesecu, na sedmi dan meseca, da je prišla k meni Gospodova beseda, rekoč:
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
21 »Človeški sin zlomil sem laket faraonu, egiptovskemu kralju; in glej, ta ne bo obvezan, da bi bil ozdravljen, da položi povoj, da ga poveže, da ga naredi močnega za držanje meča.
“Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga.
22 Zato tako govori Gospod Bog: ›Glej jaz sem zoper faraona, egiptovskega kralja in zlomil bom njegova lakta, zdravega in tistega, ki je bil zlomljen; in storil bom, da iz njegove roke pade meč.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake.
23 Egipčane bom razkropil med narode in jih razpodil po deželah.
Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri.
24 Okrepil pa bom lakte babilonskega kralja in v njegovo roko položim svoj meč. Toda faraonova lakta bom zlomil in pred njim bo stokal s stokanjem smrtno ranjenega moža.
Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo.
25 Toda okrepil bom lakta babilonskega kralja, faraonova lakta pa bosta upadla in spoznali bodo, da jaz sem Gospod, ko bom svoj meč položil v roko babilonskega kralja in iztegnil ga bo nad egiptovsko deželo.
Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto.
26 In Egipčane bom razkropil med narode in jih razpodil med dežele; in spoznali bodo, da jaz sem Gospod.‹«
Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ezekiel 30 >