< Ezekiel 26 >
1 In pripetilo se je v enajstem letu, na prvi dan meseca, da je prišla k meni Gospodova beseda, rekoč:
Pa chaka cha khumi ndi chimodzi, tsiku loyamba la mwezi, Yehova anandiyankhula kuti:
2 »Človeški sin, zato ker je Tir zoper [prestolnico] Jeruzalem rekel: ›Aha, zlomljena je tista, ki je bila velika vrata ljudstvom, obrnjena je k meni: ›Na novo bom napolnjena, ‹ sedaj je opustošena.‹
“Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Turo ananyogodola Yerusalemu kuti ‘Hii! Uja amene anali chipata choloweramo anthu a mitundu ina wawonongeka. Zitseko zake zatsekukira ife. Tidzalemera popeza wasanduka bwinja.’
3 Zato tako govori Gospod Bog: ›Glej, jaz sem zoper tebe, oh Tir in povzročil bom, da bodo zoper tebe prišli številni narodi, kakor morje povzroči svojim valovom, da se vzdignejo gor.
Nʼchifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulangani, inu anthu a ku Turo. Ndidzakuyitanirani anthu a mitundu ina kuti adzakulangeni monga momwe mafunde amawombera pa Nyanja.
4 In uničili bodo zidove Tira in porušili njegove stolpe. Prav tako bom iz njega postrgal prah in ga naredil podobnega vrhu skale.
Anthuwo adzawononga makoma a Turo ndi kugwetsa nsanja zake. Ndidzapala dothi lake ndipo ndidzamusandutsa thanthwe losalala.
5 To bo kraj za razprostiranje mrež sredi morja, kajti jaz sem to govoril, ‹ govori Gospod Bog: ›in bo postal plen narodom.
Udzakhala poyanikapo makoka pakati pa nyanja. Ine Ambuye Yehova ndayankhula zimenezo. Udzasanduka chofunkha cha anthu a mitundu ina.
6 In njegove hčere, ki so na polju, bodo umorjene z mečem; in spoznali bodo, da jaz sem Gospod.‹
Anthu okhala ku mtunda adzasakazidwa ndi lupanga. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
7 Kajti tako govori Gospod Bog: ›Poglej, nad Tir bom privedel babilonskega kralja Nebukadnezarja, kralja kraljev, iz severa, s konji in bojnimi vozovi in s konjeniki in skupinami in mnogo ljudstva.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Iwe Turo, ndidzakubweretsera Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni mfumu ya mafumu, kuchokera kumpoto pamodzi ndi akavalo ndiponso magaleta, anthu okwera pa akavalo ndi gulu lalikulu la ankhondo.
8 Na polju bo z mečem ubil tvoje hčere in naredil bo utrdbo zoper tebe in zoper tebe nasul nasip in zoper tebe vzdignil majhen ščit.
Anthu okhala ku mtunda adzawapha ndi lupanga. Adzapanga mitumbira yankhondo ndi kukukwezera zishango kuti alimbane nawe.
9 Svoje vojne stroje bo uperil zoper tvoje zidove in s svojimi sekirami bo porušil tvoje stolpe.
Adzagwetsa makoma ako ndi zida zogumulira khoma ndi kugwetsa nsanja zako ndi nkhwangwa zake.
10 Zaradi obilja njegovih konj te bo pokril njihov prah. Tvoji zidovi se bodo tresli ob hrupu konjenikov, koles in bojnih vozov, ko bo vstopil v tvoja velika vrata, kakor možje vstopijo v mesto, v katerem je narejena vrzel.
Akavalo ake adzakhala ochuluka kwambiri kotero kuti adzakukwirira ndi fumbi lawo. Makoma ako adzagwedezeka ndi mdidi wa akavalo, ngolo ndi magaleta pamene iye adzalowa pa zipata monga mmene amalowera mu mzinda umene makoma ake agwetsedwa.
11 S kopiti svojih konj bo pomendral vse tvoje ulice. Tvoje ljudstvo bo pobil z mečem in tvoje močne posadke bodo popadale na tla.
Akavalo ake adzapondaponda mʼmisewu yako yonse ndi ziboda zawo. Adzapha anthu ako ndi lupanga. Mizati yako yolimba idzagwetsedwa.
12 Iz tvojih bogastev bodo naredili plen in zaplenili bodo tvoje trgovanje in porušili bodo tvoje zidove in uničili tvoje prijetne hiše in tvoje kamne, tvoj les in tvoj prah bodo pometali v sredo voda.
Iwo adzafunkha chuma chako ndipo adzalanda zinthu zako za malonda. Adzagwetsa makoma ako ndi kuwononga nyumba zako zabwino. Adzaponya miyala yako, matabwa ako ndi dothi lako mʼnyanja.
13 In povzročil bom, da bo hrup tvojih pesmi prenehal, in zvoka tvojih harf ne bo več slišati.
Choncho ndidzathetsa phokoso la nyimbo zanu, ndipo kulira kwa apangwe ako sikudzamvekanso.
14 In naredil te bom kakor vrh skale. Ti boš kraj, na katerem se razprostirajo mreže; ne boš več pozidan, kajti jaz, Gospod, sem to govoril, ‹ govori Gospod Bog.
Ndidzakusandutsa thanthwe losalala, ndipo udzakhala malo woyanikapo makoka a nsomba. Sudzamangidwanso, pakuti Ine Yehova ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
15 Tako govori Gospod Bog Tiru: ›Mar se ne bodo otoki stresli ob zvoku tvojega padca, ko bodo ranjeni jokali, ko bo v tvoji sredi narejen pokol?
“Ine Ambuye Yehova ndikukuwuza, iwe mzinda wa Turo, kuti zilumba zidzagwedezeka pakumva za kugwa kwako ndiponso poona anthu opweteka akubuwula ndipo anthu akuphedwa pakati pako.
16 Potem bodo vsi morski princi stopili dol iz svojih prestolov in odložili svoja svečana oblačila in slekli svoje izvezene obleke. Oblekli se bodo s trepetanjem. Sedeli bodo na tleh in trepetali bodo vsak trenutek in osupli bodo nad teboj.
Pamenepo mafumu a mʼmbali mwa nyanja adzatsika pa mipando yawo yaufumu. Adzayika pambali mikanjo yawo ndi kuvala zovala zawo zamakaka. Adzachita mantha ndipo adzakhala pansi akunjenjemera kosalekeza. Adzathedwa nzeru poona zimene zakugwera.
17 In zate bodo povzdignili žalostinko in ti rekli: ›Kako si uničen, ki si bil naseljen s pomorščaki, ugledno mesto, ki je bilo močno na morju, ono in njegovi prebivalci, ki so svoji strahoti povzročili, da je bila na vseh, ki so ga strašili!
Pamenepo adzayimba nyimbo yokudandaula ndipo adzati kwa iwe: “‘Nʼkuchita kuwonongeka chotere, iwe mzinda wotchuka, wodzaza ndi anthu a ku nyanja! Unali wamphamvu pa nyanja, iwe ndi nzika zako; unkaopseza anthu onse amene ankakhala kumeneko.
18 Sedaj bodo otoki trepetali na dan tvojega padca; da, otoki, ki so na morju, bodo vznemirjeni ob tvojem odhodu.‹
Tsopano mayiko a mʼmbali mwa nyanja akunjenjemera chifukwa cha kugwa kwako; okhala pa zilumba nawonso agwidwa ndi mantha aakulu chifukwa cha kugwa kwako.’
19 Kajti tako govori Gospod Bog: ›Ko te bom naredil [za] zapuščeno mesto, podobno mestom, ki niso naseljena; ko bom nadte privedel globino in te bodo pokrile velike vode,
“Mawu a Ine Ambuye Yehova ndi awa: Ndidzakusandutsa bwinja, ngati mizinda imene anthu sangathe kukhalamo. Ndidzakuphimba ndi madzi ozama a mʼnyanja, madzi amphamvu woti akumize.
20 ko te bom privedel dol s tistimi, ki se spuščajo v jamo, z ljudstvom iz starih časov in te bodo postavili v spodnje kraje zemlje, na kraje, ki so zapuščeni od davnine, s tistimi, ki gredo dol do jame, da ne boš naseljen, in jaz bom postavil slavo v deželi živih;
Ndidzakugwetsa pansi kuti ukhale pamodzi ndi anthu amvulazakale amene akutsikira ku manda. Ine ndidzakusunga ku dzenjeko ngati ku bwinja losiyidwa kalekale, pamodzi ndi anthu amene anafa kale motero sudzabwererako kukhala pakati pa anthu amoyo.
21 naredil te bom strahoto in tebe ne bo več. Čeprav te bodo iskali, vendar nikoli več ne boš najden, ‹ govori Gospod Bog.‹«
Ine ndidzakuthetsa mochititsa mantha, ndipo sudzakhalaponso. Anthu adzakufunafuna, koma sudzapezekanso, akutero Ambuye Yehova.”