< Ezekiel 16 >
1 Ponovno je prišla k meni Gospodova beseda, rekoč:
Yehova anayankhula nane kuti,
2 »Človeški sin, povzroči [prestolnici] Jeruzalem, da spozna svoje ogabnosti
“Iwe mwana wa munthu, udzudzule Yerusalemu za ntchito zake zonyansa.
3 in reci: ›Tako govori Gospod Bog [prestolnici] Jeruzalem: ›Tvoj rod in tvoje rojstvo je iz kánaanske dežele; tvoj oče je bil Amoréjec, tvoja mati pa Hetejka.
Umuwuze kuti, ‘Ambuye Yehova akukuwuza, iwe Yerusalemu kuti: Kwawo kwa makolo ako ndi ku Kanaani ndipo iwe unabadwira komweko. Abambo ako anali Mwamori, amayi ako anali Mhiti.
4 Glede tvojega rojstva, na dan, ko si bila rojena, tvoj popek ni bil odrezan niti nisi bila umita v vodi, da ti omehča [kožo]; sploh nisi bila odrgnjena s soljo niti povita.
Pa tsiku lomwe unabadwa sanadule mchombo wako. Sanakusambitse mʼmadzi kuti uyere. Sanakuthire mchere kapena kukukulunga mʼnsalu.
5 Niti se te nobeno oko ni usmililo, da bi ti storilo karkoli od tega, da bi imelo do tebe sočutje; temveč si bila vržena na odprto polje, do gnusenja glede tvoje osebe, na dan, ko si bila rojena.
Palibe ndi mmodzi yemwe anakusamala kapena kukumvera chisoni kuti akuchitire zimenezi. Mʼmalo mwake anakutaya panja poyera, chifukwa ananyansidwa nawe pa tsiku lako lobadwa.
6 In ko sem šel mimo tebe in te videl oskrunjeno v svoji krvi, sem ti rekel, ko si bila v svoji krvi: ›Živi; ‹ da, rekel sem ti, ko si bila v svoji krvi: ›Živi.‹
“‘Tsono pamene ndinkadutsa, ndinakuona ukuvimvinizika mʼmagazi ako. Ndinakuyankhula uli mʼmagazi ako omwewo kuti, ‘Khala ndi moyo,’
7 Dal sem ti, da si se namnožila kakor brstje polja in povečala si se in postala velika in prišla k odličnim ornamentom. Tvoje prsi so se oblikovale in tvoji lasje so zrasli, medtem ko si bila naga in gola.
ndi kuti ukule ngati mbewu ya mʼmunda. Iwe unakula ndipo unatalika ndi kutha msinkhu. Mawere ako anayamba kumera ndi tsitsi lakonso linayamba kutalika. Komabe unali wamaliseche ndi wausiwa.
8 Torej, ko sem šel mimo tebe in pogledal nate, glej, tvoj čas je bil čas ljubezni. Razširil sem krajec svojega oblačila nad teboj in pokril tvojo nagoto. Da, prisegel sem ti in vstopil v zavezo s teboj, ‹ govori Gospod Bog ›in postala si moja.
“‘Tsono pamene ndinkadutsanso ndinaona kuti nthawi yako yomanga banja inakwana. Tsono ndinakufunditsa chovala changa ndi kubisa umaliseche wako. Ndinachita nawe pangano la ukwati ndipo unakhala wanga, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.
9 Potem sem te umil z vodo; da, temeljito sem izmil tvojo kri iz tebe in te mazilil z oljem.
“‘Ine ndinakusambitsa mʼmadzi kutsuka magazi ako ndikukudzoza mafuta.
10 Oblekel sem te tudi z izvezenim delom in ti obul jazbečevo kožo in te naokoli opasal s tankim lanenim platnom in te ogrnil s svilo.
Ndinakuveka zovala zopetapeta ndi nsapato za chikopa. Ndinakuveka zovala zabafuta ndi kukuveka zovala za bafuta.
11 Odel sem te tudi z ornamenti in na tvoje roke sem nataknil zapestnice in verižico na tvoj vrat.
Ndinakukongoletsa ndi zokometsera zamtengowapatali: ndinakuveka zibangiri mʼmanja mwako ndi mkanda mʼkhosi mwako,
12 Položil sem dragulj na tvoje čelo in uhane v tvoja ušesa in krasno krono na tvojo glavo.
ndipo ndinakuveka chipini pa mphuno yako, ndolo ku makutu ako ndiponso chipewa chaufumu pa mutu wako.
13 Tako si bila odeta z zlatom in srebrom, in tvoje oblačilo je bilo iz tankega lanenega platna, svile in izvezenega dela. Jedla si fino moko, med in olje. Bila si silno krasna in uspevala si v kraljestvu.
Choncho unavala zokongoletsa zagolide ndi siliva. Zovala zako zinali zabafuta, zasilika ndi za nsalu zopetapeta. Chakudya chako chinali ufa wosalala uchi ndi mafuta a olivi. Motero unakhala wokongola kwambiri ndipo unasanduka mfumukazi.
14 Tvoj ugled je zaradi tvoje lepote odšel naprej med pogane, kajti ta je bila popolna zaradi moje ljubkosti, ki sem jo položil nadte, ‹ govori Gospod Bog.
Ndipo mbiri ya kukongola kwako inawanda pakati pa anthu a mitundu ina, chifukwa ulemerero umene ndinakupatsa unapititsa patsogolo kukongola kwako, akutero Ambuye Yehova.
15 ›Toda zaupala si v svojo lastno lepoto in igrala pocestnico zaradi svojega ugleda in svoje prešuštvovanje si izlila na vsakega, ki je šel mimo; njegovo je bilo.
“‘Koma iwe unatama kukongola kwako ndipo unayamba kuchita zadama chifukwa cha kutchuka kwako. Unkachita chigololo ndi kumangodzipereka kwa aliyense wodutsa ndipo kukongola kwako kunakhala kwake.
16 Vzela si od svojih oblek in svoje visoke kraje si odela s številnimi barvami in na njih igrala pocestnico. Podobne stvari ne bodo prišle niti to ne bo tako.
Unatenga zovala zako zina nukakongoletsera malo opembedzerako mafano, ndipo kumeneko umachitirako zigololo. Zinthu izi sizinachitikepo nʼkale lomwe ndipo sizidzachitikanso.
17 Vzela si tudi svoje lepe dragocenosti od mojega zlata in od mojega srebra, ki sem ti jih dal in si si naredila moške podobe in z njimi zagrešila vlačugarstvo
Unatenga zokongoletsera zopangidwa ndi golide ndi siliva zimene ndinakupatsa ndipo unadzipangira wekha mafano aamuna amene unkachita nawo za dama.
18 in jemala si svoje izvezene obleke in jih pokrivala in prednje si postavljala moje olje in moje kadilo.
Ndipo iwe unatenga zovala zako zopetapeta ndi kuveka mafano. Mafuta anga ndi lubani wanga unapereka kwa mafanowo.
19 Tudi moja hrana, ki sem ti jo dal, fina moka, olje in med, s katero sem te hranil, celo to si postavljala prednje v prijeten vonj. In tako je to bilo, ‹ govori Gospod Bog.
Chakudya chimene ndinakupatsa, ufa, mafuta ndi uchi, zimene ndinkakudyetsa nazo unazitenga nʼkuzipereka kwa mafanowo ngati nsembe ya fungo lokoma. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
20 ›Poleg tega si jemala svoje sinove in svoje hčere, ki si mi jih rodila in te si jim žrtvovala, da bi bili požrti. Je to izmed tvojih vlačugarstev majhna zadeva,
“‘Ndipo unatenga ana ako aamuna ndi ana aakazi amene unandibalira ine, ndipo unakawapereka ngati nsembe kwa mafanowo. Kodi zigololo zakozo sizinakukwanire
21 da si morila moje otroke in jim jih izročala, da gredo zanje skozi ogenj?
kuti uziphanso ana anga ndi kuwapereka ngati nsembe kwa mafano akowo?
22 In v vseh svojih ogabnostih in svojih vlačugarstvih se nisi spomnila dni svoje mladosti, ko si bila naga in gola in si bila oskrunjena v svoji krvi.‹
Chifukwa cha zadama zako zonyansazi unayiwala masiku a ubwana wako pamene unali wamaliseche, wausiwa ndiponso womangovivinizika mʼmagazi.
23 In pripetilo se je po vseh tvojih zlobnostih (gorje, gorje tebi!‹ govori Gospod Bog ),
“‘Tsoka! Tsoka kwa iwe, akutero Ambuye Yehova chifukwa powonjezera pa zoyipa zako zonse,
24 da si si zgradila tudi eminenten kraj in si si naredila visok kraj na vsaki ulici.
wadzimangira wekha nsanja ndi guwa pa mabwalo onse.
25 Visok kraj si si zgradila na vsakem začetku poti in storila si, da je bila tvoja lepota prezirana in svoja stopala si razprla vsakemu, ki je šel mimo in pomnožila si svoja vlačugarstva.
Pa msewu uliwonse wamanga nsanjazo. Motero wanyazitsa kukongola kwako podzipereka kwa aliyense amene adutsapo.
26 Prav tako si zagrešila prešuštvovanje z Egipčani, svojimi sosedi velikega uda in svoja vlačugarstva si povečala, da bi me dražila do jeze.
Umachita chigololo ndi Aigupto, anthu adama oyandikana nawe. Choncho unandikwiyitsa chifukwa unachulukitsa za dama zako.
27 Glej, zato sem nad teboj iztegnil svojo roko in zmanjšal tvojo vsakdanjo hrano in te izročil volji tistih, ki te sovražijo, hčeram Filistejcev, ki se sramujejo tvojih nespodobnih poti.
Nʼchifukwa chake ndinatambasula dzanja langa kukukantha ndi kuchepetsa dziko lako. Ndinakupereka kwa adani ako, Afilisti amene amayipidwa ndi makhalidwe ako onyansa.
28 Vlačugo si igrala tudi z Asirci, ker si bila nenasitna; da, z njimi si igrala pocestnico, pa vendar nisi mogla biti potešena.
Chifukwa cha chilakolako chako unachitanso zadama ndi Aasiriya. Ngakhale unachita nawo chigololo koma sunakhutitsidwebe.
29 Poleg tega si pomnožila svoje prešuštvovanje v kánaanski deželi do Kaldeje; in vendar nisi bila potešena s tem.
Choncho unapitirirabe kuchita chigololo ndi Ababuloni, anthu a mʼdziko lokonda zamalonda. Ngakhale unachita izi, komabe sunakhutitsidwe.
30 Kako šibko je tvoje srce, ‹ govori Gospod Bog, ›glede na to, da počneš vse te stvari, delo gospodovalne vlačugarske ženske;
“‘Ambuye Yehova akuti: Mtima wako ndi wofowoka kwambiri chifukwa unachita zonsezo monga ngati mkazi wopanga manyazi.
31 v tem, da si gradiš svoje eminentne kraje na začetku vsake poti in si delaš svoje visoke kraje na vsaki ulici; in nisi bila kot pocestnica, v tem, da preziraš plačilo,
Unamanga nsanja pa msewu uliwonse. Unamanganso kachisi pabwalo lililonse. Komabe sunachite ngati mkazi wadama chifukwa unakana malipiro.
32 temveč kakor žena, ki zagreši zakonolomstvo, ki jemlje tujce namesto svojega soproga!
“‘Iwe mkazi wachigololo! Umakonda amuna achilendo kupambana mwamuna wakowako!
33 Oni dajejo darila vsem vlačugam, toda ti daješ svoja darila vsem svojim ljubimcem in jih najemaš, da lahko pridejo k tebi na vsaki strani zaradi tvojega vlačugarstva.
Amuna ndiwo amapereka malipiro kwa mkazi wadama. Koma iwe ndi amene ukupereka mphatso kwa zibwenzi zako zonse. Choncho umazinyengerera kuti zizibwera kwa iwe kuchokera mbali zonse kudzagona nawe.
34 In v tvojem vlačugarstvu je v tebi nasprotje od drugih žensk, da zagrešiš vlačugarstva, medtem ko ti nihče ne sledi, in pri tem ti daješ nagrado, tebi pa ni dana nobena nagrada, zato si nasprotje.‹
Chotero iwe ukusiyana ndi akazi ena achigololo, pakuti palibe amene ankakunyengerera kuti uchite naye chigololo. Iweyo ndiye unkapereka ndalama osati ena kukupatsa ndalama ayi. Motero unalidi wosiyana kwambiri ndi akazi ena.
35 Zatorej, oh pocestnica, poslušaj besedo od Gospoda:
“‘Tsono mkazi wachigololo iwe, imva mawu a Yehova!
36 ›Tako govori Gospod Bog: ›Ker je bila tvoja umazanost izlita in tvoja nagota odkrita zaradi tvojega vlačugarstva s tvojimi ljubimci in z vsemi maliki tvojih ogabnosti in s krvjo tvojih otrok, ki si jim jih dala;
Ambuye Yehova akuti, popeza unavula ndi kuonetsa umaliseche wako mopanda manyazi, unachita chigololo ndi zibwenzi zako pamodzi ndi mafano ako onyansa, komanso popeza unapereka ana ako kuti aphedwe ngati nsembe zoperekedwa kwa mafano,
37 glej, zato bom zbral vse tvoje ljubimce, s katerimi si uživala in vse tiste, ki si jih ljubila, z vsemi tistimi, ki si jih sovražila; jaz jih bom celo zbral naokoli tebe zoper tebe in jim odkril tvojo nagoto, da bodo lahko videli vso tvojo nagoto.
nʼchifukwa chake Ine ndidzasonkhanitsa zibwenzi zako zonse, zimene unkasangalala nazo, amene unkawakonda ndi amene unkawada. Ndidzawasonkhanitsa motsutsana nawe kuchokera ku madera onse okuzungulira ndipo Ine ndidzakuvula pamaso pawo, ndipo iwo adzaona umaliseche wako wonse.
38 Sodil te bom, kakor so sojene ženske, ki prelomijo zakonsko zvezo in prelijejo kri; in dal ti bom kri v razjarjenosti in ljubosumnosti.
Ine ndidzakulanga monga mmene amalangira akazi amene amachita chigololo ndiponso opha anthu. Chifukwa cha ukali wanga ndi nsanje yanga, ndidzakhetsa magazi ako mokwiya kwambiri.
39 Prav tako te bom izročil v njihovo roko in zrušili bodo tvoj eminenten kraj in zlomili tvoje visoke kraje. Slekli te bodo tudi iz tvojih oblačil in vzeli tvoje lepe dragocenosti in te pustili nago in golo.
Ndidzakupereka mʼmanja mwa zibwenzi zako ndi kuwononga nyumba zopembedzera mafano ako. Iwo adzakuvula zovala zako ndi kutenga zodzikometsera zako zabwino. Choncho adzakusiya wa maliseche ndi wausiwa.
40 Prav tako bodo zoper tebe privedli skupino in te bodo kamnali s kamni in te prebodli s svojimi meči.
Iwo adzabweretsa gulu la anthu limene lidzakuponya miyala ndi kukutematema ndi malupanga awo.
41 Tvoje hiše bodo požgali z ognjem in izvršili sodbe nad teboj v očeh mnogih žensk. Povzročil ti bom, da prenehaš z igranjem pocestnice in tudi nobenega plačila ne boš več dajala.
Adzatentha nyumba zako ndi kukulanga iwe pamaso pa akazi ambiri. Ndidzathetsa chigololo chako, ndipo sudzalipiranso zibwenzi zako.
42 Tako bom svoji razjarjenosti zoper tebe naredil, da počiva in moja ljubosumnost bo odšla od tebe in bom miren in ne bom več jezen.
Ukali wanga udzalekera pamenepo ndipo sindidzakuchitiranso nsanje. Ndidzakhala chete osakwiyanso.
43 Ker se nisi spomnila dni svoje mladosti, temveč si me razburjala v vseh teh stvareh; glej, zato bom tudi jaz poplačal tvojo pot na tvoji glavi, ‹ govori Gospod Bog: ›in ne boš zagrešila te nespodobnosti nad vsemi svojimi ogabnostmi.
“‘Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako koma unandikwiyitsa ndi zinthu zonsezi, Ine ndidzakubwezera ndithu chilango pamutu pako chifukwa cha zimene wachita, akutero Ambuye Yehova. Paja unawonjezera chigololo pa machitidwe ako onyansa.
44 Glej, vsak, kdor uporablja pregovore, bo ta pregovor uporabil zoper tebe, govoreč: ›Kakršna je mati, takšna je njena hči.‹
“‘Taona, onse onena miyambi adzakuphera mwambi wakuti, ‘Make mbuu, mwana mbuu.’
45 Ti si hči svoje matere, ki prezira svojega soproga in svoje otroke; in ti si sestra svojih sestrá, ki so prezirale svoje soproge in svoje otroke. Tvoja mati je bila Hetejka in tvoj oče Amoréjec.
Ndiwedi mwana weniweni wamkazi wa mayi wako, amene amanyoza mwamuna wake ndi ana ake. Ndiwe mʼbale weniweni wa abale ako, amene amanyoza amuna awo ndi ana awo. Amayi ako anali Mhiti ndipo abambo ako anali Mwamori.
46 Tvoja starejša sestra je Samarija, ona in njene hčere, ki prebivajo na tvoji levici. Tvoja mlajša sestra, ki prebiva pri tvoji desnici, je Sódoma in njene hčere.
Mkulu wako anali Samariya, ndipo iye pamodzi ndi ana ake aakazi ankakhala cha kumpoto kwako. Mngʼono wako, Sodomu ankakhala cha kummwera kwako pamodzi ndi ana ake aakazi.
47 Vendar nisi hodila po njihovih poteh niti storila po njihovih ogabnostih. Temveč kot bi bila to malenkost, si bila bolj izprijena kakor one na vseh svojih poteh.
Iwe sunangotsatira kokha njira zawo zoyipa ndi kuchita zonyansa zawo, koma patangopita nthawi pangʼono machitidwe ako oyipa anaposa awo.
48 Kakor jaz živim, ‹ govori Gospod Bog, ›niti tvoja sestra Sódoma niti njene hčere niso počele, kakor si storila ti in tvoje hčere.
Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ngakhale mʼbale wako Sodomu ndi ana ake aakazi sanachitepo zimene iwe ndi ana ako aakazi munachita.
49 Glej, to je bila krivičnost tvoje sestre Sódome, ponos, polnost kruha, obilje brezdelja v njej in v njenih hčerah niti ni krepila roke ubogega in pomoči potrebnega.
“‘Tsono tchimo la mʼbale wako Sodomu linali ili: Iye ndi ana ake aakazi ankanyadira kuchuluka kwa chakudya ndi chuma chawo. Koma sanalabadireko kuthandiza osauka ndi aumphawi.
50 Bile so ošabne in zagrešile ogabnost pred menoj, zato sem jih vzel proč, kakor se mi je videlo dobro.
Anali odzitukumula ndipo ankachita zonyansa pamaso panga. Nʼchifukwa chake ndinawachotsa monga mmene waoneramu.
51 Niti ni Samarija zagrešila polovice tvojih grehov, temveč si pomnožila svoje ogabnosti bolj kakor oni [dve] in opravičila si svoji sestri v vseh svojih ogabnostih, ki si jih storila.
Samariya sanachite ngakhale theka la machimo amene unachita. Iwe wachita zinthu zonyansa zambiri kuposa iwo, motero kuti abale ako awiriwo amaoneka ngati olungama kuyerekeza ndi iye.
52 Tudi ti, ki si sodila svoji sestri, nosi svojo lastno sramoto za svoje grehe, ki si jih zagrešila bolj gnusno kakor oni [dve]. Oni sta pravičnejši kakor ti. Da, tudi ti bodi zbegana in nosi svojo sramoto v tem, da si opravičila svoji sestri.
Tsono iwenso uyenera kuchita manyazi popeza waonetsa abale ako ngati osachimwa. Popeza kuti machimo ako ndi onyansa kwambiri kupambana awo, tsonotu iwowo akuoneka olungama kupambana iweyo. Choncho iwenso uchite manyazi ndi kunyozedwa popeza unaonetsa abale ako ngati olungama.
53 Ko bom ponovno privedel njihovo ujetništvo, ujetništvo Sódome in njenih hčera in ujetništvo Samarije in njenih hčera, takrat bom ponovno privedel ujetništvo tvojih ujetnikov v njihovi sredi,
“‘Koma, ndidzadalitsanso Sodomu ndi ana ake aakazi. Ndidzadalitsanso Samariya ndi ana ake aakazi. Pa nthawi yomweyo ndidzakudalitsanso iwe Yerusalemu.
54 da boš lahko nosila svojo lastno sramoto in boš lahko zbegana v vsem, kar si storila, v tem, da si jima tolažba.
Ndidzatero kuti uchite manyazi ndi kunyozeka chifukwa cha zonse zimene unachita powatonthoza anthuwa.
55 Ko se bodo tvoje sestre, Sódoma in njene hčere, vrnile k svojemu prejšnjemu stanju in se bodo Samarija in njene hčere vrnile k svojemu prejšnjemu stanju, takrat se boste ti in tvoje hčere vrnile k svojemu prejšnjemu stanju.
Motero mʼbale wako Sodomu ndi ana ake akadzakhala monga mmene analili poyamba paja, ndiponso mʼbale wako Samariya akadzakhalanso monga mmene anali poyamba paja, ndiye kuti iwenso ndi ana ako mudzakhala monga mmene munalili payamba paja.
56 Kajti tvoja sestra Sódoma ni bila omenjena s tvojimi usti na dan tvojega ponosa,
Kale lija pamene unkanyada, suja unkanyogodola mʼbale wako Sodomu
57 preden je bila odkrita tvoja zlobnost, kakor ob času, ko so te grajale sirske hčere in vsi tisti, ki so okrog nje, hčere Filistejcev, ki te prezirajo vsenaokrog.
kuyipa kwako kusanadziwike? Koma tsopano wafanana naye. Wasandukano chinthu chonyozeka kwa anthu a ku Edomu ndi kwa onse owazungulira ndiponso kwa Afilisti. Ndithu onse amene akuzungulira amakunyoza.
58 Nosila si svojo nespodobnost in svoje ogabnosti, ‹ govori Gospod.
Choncho udzalangidwa chifukwa cha zigololo zako ndi machitidwe anu onyansa, akutero Yehova.
59 Kajti tako govori Gospod Bog: ›S teboj bom postopal celo kakor si ti storila, ki si prezirala prisego v prelamljanju zaveze.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulanga molingana ndi zimene unachita. Iwe unanyoza lumbiro lako pophwanya pangano langa.
60 Kljub temu se bom spomnil svoje zaveze s teboj v dneh tvoje mladosti in osnoval ti bom večno zavezo.
Komabe, Ine ndidzakumbukira pangano limene ndinachita nawe mʼmasiku a unyamata wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha ndi iwe.
61 Potem se boš spomnila svojih poti in boš osramočena, ko boš sprejela svoje sestre, svoje starejše in svoje mlajše, in dal ti jih bom za hčere, toda ne s tvojo zavezo.
Tsono udzakumbukira njira zako zakale. Udzachita manyazi polandiranso abale ako, wamkulu ndi wamngʼono yemwe. Ndidzawaperekanso kwa iwe kuti akhale ngati ana ako ngakhale kuti sali a mʼpangano langa ndi iwe.
62 S teboj bom utrdil svojo zavezo in vedela boš, da jaz sem Gospod,
Kotero ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
63 da se lahko spomniš in boš zbegana in zaradi svoje sramote nikoli več ne boš odprla svojih ust, ko bom pomirjen proti tebi za vse, kar si storila, ‹ govori Gospod Bog.‹«
Ndikadzakukhululukira zoyipa zako zonse zimene unachita, udzazikumbukira ndipo udzachita manyazi kwambiri, kotero kuti sudzatha nʼkuyankhula komwe, akutero Ambuye Yehova.’”