< 2 Mojzes 32 >
1 Ko je ljudstvo videlo, da je Mojzes odlašal priti dol z gore, se je ljudstvo skupaj zbralo k Aronu in mu reklo: »Vstani, naredi nam bogove, ki bodo šli pred nami, kajti glede tega Mojzesa, človeka, ki nas je privedel iz egiptovske dežele, ne vemo kaj je nastalo iz njega.«
Anthu ataona kuti Mose akuchedwa kutsika mʼphiri, anasonkhana kwa Aaroni ndipo anati, “Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.”
2 Aron jim je rekel: »Izdrite zlate uhane, ki so v ušesih vaših žena, vaših sinov in vaših hčera in jih prinesite k meni.«
Aaroni anawayankha kuti, “Vulani ndolo zagolide zimene avala akazi anu, ana anu aamuna ndi aakazi ndipo muzibweretse kwa ine.”
3 Vse ljudstvo je izdrlo zlate uhane, ki so bili v njihovih ušesih in jih prineslo k Aronu.
Kotero anthu onse anavula ndolo zagolide ndi kubwera nazo kwa Aaroni.
4 Ta jih je prejel iz njihove roke in to oblikoval z rezbarskim orodjem, potem ko je naredil ulito tele, in rekli so: »To so tvoji bogovi, oh Izrael, ki so te privedli iz egiptovske dežele.«
Choncho Aaroni analandira golideyo ndipo anamuwumba ndi chikombole ndi kupanga fano la mwana wangʼombe. Kenaka anthu aja anati, “Inu Aisraeli, nayu mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.”
5 Ko je Aron to videl, je pred njim zgradil oltar in Aron je naredil razglas ter rekel: »Jutri je praznovanje Gospodu.«
Aaroni ataona izi, anamanga guwa lansembe patsogolo pa mwana wangʼombeyo ndipo analengeza kuti, “Mawa kudzakhala chikondwerero cha Yehova.”
6 Naslednji dan so zgodaj vstali, darovali žgalne daritve in prinesli mirovne daritve in ljudstvo se je usedlo, da jé in da pije in vstalo, da se zabava.
Kotero tsiku linalo anthu anadzuka mmamawa ndithu ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Atatha kupereka nsembezo, anthuwo anakhala pansi nayamba kudya ndi kumwa. Kenaka anayimirira nayamba kuvina mwachilendo.
7 Gospod je rekel Mojzesu: »Pojdi, stopi dol, kajti tvoje ljudstvo, ki si ga privedel iz egiptovske dežele, se je izpridilo.
Pamenepo Yehova anati kwa Mose, “Tsika msanga, chifukwa anthu ako amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto aja adziyipitsa kwambiri.
8 Hitro so se obrnili stran iz poti, ki sem jim jo zapovedal. Naredili so si ulito tele, ga oboževali, mu žrtvovali in rekli: ›To so tvoji bogovi, oh Izrael, ki so te privedli gor iz egiptovske dežele.‹«
Iwo apatuka mwamsanga kuleka kutsatira zimene ndinawalamula. Ndiye adzipangira fano la mwana wangʼombe. Aligwadira ndi kuliperekera nsembe nʼkumati, ‘Inu Aisraeli, nayu mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.’”
9 Gospod je rekel Mojzesu: »Videl sem to ljudstvo in glej, to je trdovratno ljudstvo.
Yehova anati kwa Mose, “Ine ndikuwadziwa anthu amenewa. Iwowa ndi ankhutukumve.
10 Zdaj me torej pusti samega, da se moj bes razvname zoper njih in da jih lahko použijem. Iz tebe pa bom naredil velik narod.«
Chifukwa chake undileke kuti mkwiyo wanga uyake pa iwo ndi kuwawononga. Ndipo Ine ndidzakusandutsa kuti ukhale mtundu waukulu.”
11 Mojzes je rotil Gospoda, svojega Boga in rekel: » Gospod, zakaj se tvoj bes razvnema zoper tvoje ljudstvo, ki si ga privedel iz egiptovske dežele z veliko močjo in z mogočno roko?
Koma Mose anapempha chifundo cha Mulungu wake ndipo anati, “Chonde Yehova, chifukwa chiyani mwakwiyira anthu awa amene munawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
12 Zakaj bi Egipčani govorili in rekli: ›Zaradi zla jih je privedel ven, da jih ubije na gorah in da jih použije iz obličja zemlje?‹ Obrni se od svojega krutega besa in se pokesaj glede tega zla zoper svoje ljudstvo.
Kodi mukufuna kuti Aigupto azinena kuti, ‘Munali ndi cholinga choyipa chofuna kuwaphera ku mapiri kuno ndi kuwawonongeratu pa dziko lapansi pamene munkawatulutsa ku Igupto kuja?’ Ayi, chonde mkwiyo wanu woyaka ngati motowu ubwezeni ndipo sinthani maganizo ofunira zoyipa anthu anu.
13 Spomni se Abrahama, Izaka in Izraela, svojih služabnikov, ki si jim prisegel pri samem sebi in jim rekel: ›Vaše seme bom pomnožil kakor zvezd neba in vso to deželo, o kateri sem govoril, bom dal tvojemu semenu in podedovali jo bodo na veke.‹«
Kumbukirani atumiki anu, Abrahamu, Isake, Israeli ndi zija munawalonjeza polumbira pa dzina lanu kuti, ‘Ine ndidzachulukitsa zidzukulu zanu ndipo zidzakhala zambiri ngati nyenyezi zakumwamba. Zidzukulu zanuzo ndidzazipatsa dziko lonseli limene ndinalonjeza. Dziko limeneli lidzakhala lawo nthawi zonse.’”
14 Gospod se je pokesal glede zla, ki ga je mislil storiti svojemu ljudstvu.
Choncho Yehova analeka ndipo sanawachitire choyipa anthu ake monga anaopsezera.
15 Mojzes se je obrnil in odšel dol z gore in v njegovi roki sta bili dve plošči pričevanja. Plošči sta bili popisani na obeh njunih straneh; na eni strani in na drugi sta bili popisani.
Mose anatembenuka ndi kutsika phiri miyala iwiri ya pangano ili mʼmanja mwake. Miyalayi inalembedwa mbali zonse, kutsogolo ndi kumbuyo komwe.
16 Plošči sta bili Božje delo in pisanje je bilo pisanje od Boga, vgravirano na plošči.
Miyalayi anayikonza ndi Mulungu. Malembawo analemba ndi Mulungu mozokota pa miyalapo.
17 Ko je Józue slišal hrup ljudstva, medtem ko so kričali, je Mojzesu rekel: » Tam, v taboru, je vojni hrup.«
Pamene Yoswa anamva phokoso la anthu anati kwa Mose, “Ku msasa kuli phokoso la nkhondo.”
18 Ta je rekel: » To ni glas tistih, ki vpijejo zaradi zmage niti to ni glas tistih, ki vpijejo, ker so bili premagani, temveč slišim hrup tistih, ki pojejo.«
Mose anayankha kuti, “Phokoso limeneli sindikulimva ngati phokoso la opambana nkhondo, kapena kulira kwa ongonjetsedwa pa nkhondo. Koma ndikulimva ngati phokoso la anthu amene akuyimba.”
19 Takoj ko je prišel blizu tabora, se je pripetilo, da je zagledal tele in ples. Mojzesova jeza se je vnela, tabli je vrgel iz svojih rok ter ju zlomil pod goro.
Mose atayandikira msasa ndi kuona mwana wangʼombe ndiponso kuvina, anakwiya kwambiri ndipo anaponya pansi miyala imene inali mʼmanja mwake, ndi kuyiphwanya pa tsinde la phiri.
20 Vzel je tele, ki so ga naredili, ga sežgal v ognju, ga zmlel v prah in ga posul nad vodo in Izraelove otroke primoral, da so pili od tega.
Ndipo iye anatenga mwana wangʼombe amene anthu anapanga uja ndi kumuwotcha pa moto ndi kumuperapera ndikukhala ngati fumbi. Kenaka anawaza fumbilo mʼmadzi ndi kuwamwetsa Aisraeli madziwo.
21 Mojzes je Aronu rekel: »Kaj ti je storilo to ljudstvo, da si nadnje privedel tako velik greh?«
Tsono Mose anafunsa Aaroni kuti, “Kodi anthu awa anakuchita chiyani kuti uwachimwitse koopsa chotere?”
22 Aron je rekel: »Ne dopusti, da se razvname jeza mojega gospoda. Ti poznaš ljudstvo, da so postavljeni v zlo.
Aaroni anayankha kuti, “Musakwiye mbuye wanga. Inu mukudziwa kuti anthu awa ndi ovuta.
23 Kajti rekli so mi: ›Naredi nam bogove, ki bodo šli pred nami, kajti glede tega Mojzesa, človeka, ki nas je privedel iz egiptovske dežele, ne vemo kaj je nastalo iz njega.‹
Iwo anati kwa ine, ‘Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitulutsa ife mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.’
24 Rekel sem jim: ›Kdorkoli ima kakršnokoli zlato, naj ga izdere.‹ Tako so ga dali meni. Potem sem ga vrgel v ogenj in izšlo je to tele.«
Choncho ine ndinawawuza kuti, ‘Aliyense amene ali ndi zokometsera zagolide azivule.’ Choncho iwo anandipatsa golide, ndipo ndinamuponya pa moto ndi kupanga fano la mwana wangʼombeyu.”
25 Ko je Mojzes videl, da je bilo ljudstvo nago, (kajti Aron jih je storil nage v njihovo sramoto med njihovimi sovražniki)
Mose anaona kuti anthuwo anali osokonezekadi chifukwa Aaroni anawalekerera mpaka kusanduka anthu osekedwa pakati pa adani awo.
26 potem je Mojzes stal v velikih vratih tabora in rekel: »Kdo je na Gospodovi strani? Naj pride k meni.« In k njemu so se zbrali vsi sinovi Lévijevcev.
Choncho iye anayima pa chipata cholowera mu msasa ndipo anati, “Aliyense amene ali mbali ya Yehova abwere kwa ine.” Ndipo Alevi onse anapita mbali yake.
27 Rekel jim je: »Tako govori Gospod, Izraelov Bog: ›Vsak mož naj svoj meč pripaše k svoji strani in gre noter in ven, od velikih vrat do velikih vrat, skozi tabor in naj vsak mož ubije svojega brata in vsak mož svojega družabnika in vsak mož svojega bližnjega.‹«
Ndipo iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena, ‘Pitani ku misasa konse, mulowe ku zipata zonse ndipo aliyense akaphe mʼbale wake, kapena mnzake kapena mnansi wake.’”
28 Otroci Lévijevcev so storili glede na Mojzesovo besedo in tam je ta dan izmed ljudstva padlo okoli tri tisoč mož.
Alevi anachita zomwe Mose analamula, ndipo tsiku limenelo panafa anthu pafupifupi 3,000.
29 Kajti Mojzes je rekel: »Uméstite se danes Gospodu, celo vsak mož za svojega sina in za svojega brata, da lahko ta dan nad vas podeli blagoslov.«
Kenaka Mose anati, “Lero mwadzipatula nokha kukhala ansembe otumikira Yehova. Mwachita izi popeza aliyense wa inu wapha mwana wake kapena mʼbale wake. Tsono lero Yehova wakudalitsani.”
30 Naslednji dan se je pripetilo, da je Mojzes rekel ljudstvu: »Zagrešili ste velik greh. Sedaj bom šel gor h Gospodu, morda bom storil spravo za vaš greh.«
Mmawa mwake Mose anati kwa anthu onse, “Inu mwachita tchimo lalikulu. Koma tsopano ine ndipita ku phiri kwa Yehova mwina ndikatha kukupepeserani chifukwa cha tchimo lanu.”
31 Mojzes se je vrnil h Gospodu ter rekel: »Oh, to ljudstvo je zagrešilo velik greh in si naredilo bogove iz zlata.
Kotero Mose anabwereranso kwa Yehova ndipo anati, “Aa! Anthu awa achita tchimo lalikulu! Iwo adzipangira milungu yagolide.
32 Vendar sedaj, če hočeš odpusti njihov greh ― in če ne, me izbriši, prosim te, iz svoje knjige, ki si jo napisal.«
Koma tsopano, chonde akhululukireni tchimo lawo. Ngati simutero, ndiye mundifute ine mʼbuku limene mwalemba.”
33 Gospod je rekel Mojzesu: »Kdorkoli je grešil zoper mene, tistega bom izbrisal iz svoje knjige.
Yehova anamuyankha Mose kuti, “Ndidzafuta mʼbuku aliyense amene wandichimwira.
34 Zato sedaj pojdi, vodi ljudstvo na kraj, o katerem sem ti govoril. Glej, moj Angel bo šel pred teboj. Kljub temu bom na dan, ko obiščem, obiskal njihov greh na njih.«
Tsopano pita ukawatsogolere anthu kumalo kumene ine ndinanena, ndipo mngelo wanga adzakutsogolerani. Komabe, nthawi yanga ikadzafika kuti ndiwalange, ndidzawalanga chifukwa cha tchimo lawo.”
35 Gospod je trpinčil ljudstvo, ker so naredili tele, ki ga je naredil Aron.
Ndipo Yehova anawakantha anthuwo ndi mliri chifukwa anawumiriza Aaroni kuti awapangire fano la mwana wangʼombe.