< 2 Mojzes 3 >

1 Torej Mojzes je varoval trop svojega tasta Jitra, midjánskega duhovnika in vodil trop k zadnjemu delu puščave in prišel h gori Boga, k Horebu.
Tsono Mose amaweta ziweto za mpongozi wake Yetero, wansembe uja wa ku Midiyani. Tsiku lina iye anazitsogolera kupita ku chipululu ndipo anafika ku phiri la Mulungu lotchedwa Horebu.
2 Gospodov angel se mu je prikazal v ognjenem plamenu iz srede grma in pogledal je in glej, grm je gorel z ognjem, pa grm ni bil použit.
Kumeneko mngelo wa Yehova anaonekera kwa iye mʼmalawi amoto mʼchitsamba. Mose anaona kuti ngakhale chitsambacho chimayaka koma sichimanyeka.
3 Mojzes je rekel: »Sedaj se bom obrnil vstran in pogledal ta velik prizor, zakaj grm ne zgori.«
Tsono Mose anati mu mtima mwake, “Ine ndipita komweko ndikaone zodabwitsazi, chitsamba sichikunyeka chifukwa chiyani?”
4 Ko je Gospod videl, da se je obrnil vstran, da bi videl, je Bog iz srede grma zaklical k njemu ter rekel: »Mojzes, Mojzes.« Ta je rekel: »Tukaj sem.«
Yehova ataona kuti Mose anapatuka kuti adzaonetsetse, Mulungu anamuyitana Mose kuchokera mʼchitsambamo nati, “Mose! Mose!” Ndipo anayankha, “Wawa.”
5 Rekel je: »Ne približaj se, svoje čevlje sezuj s svojih stopal, kajti prostor, na katerem stojiš, je sveta zemlja.«
Mulungu anati, “Usayandikire kuno. Vula nsapato zako, pakuti malo amene wayimapo ndi opatulika.”
6 Poleg tega je rekel: »Jaz sem Bog tvojega očeta, Bog Abrahama, Bog Izaka in Bog Jakoba.« In Mojzes je skril svoj obraz, kajti bal se je, da bi pogledal na Boga.
Mulungu anati, “Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo.” Atamva zimenezi, Mose anaphimba nkhope yake chifukwa anaopa kuona Mulungu.
7 Gospod je rekel: »Zagotovo sem videl stisko svojega ljudstva, ki je v Egiptu in slišal njihovo vpitje zaradi njihovih preddelavcev, kajti poznam njihove bridkosti
Yehova anati, “Ine ndaona ndithu mazunzo a anthu anga amene ali ku Igupto. Ndamva kulira kwawo chifukwa cha anthu amene akuwapsinja, ndipo ndakhudzidwa ndi masautso awo.
8 in prišel sem dol, da jih osvobodim iz roke Egipčanov in jih privedem iz te dežele gor v dobro in veliko deželo, deželo, kjer tečeta mleko in med, v deželo Kánaancev, Hetejcev, Amoréjcev, Perizéjcev, Hivéjcev in Jebusejcev.
Choncho ndabwera kuti ndiwapulumutse mʼdzanja la Aigupto, kuwatulutsa mʼdzikolo ndi kukawalowetsa mʼdziko labwino ndi lalikulu, dziko loyenda mkaka ndi uchi, kwawo kwa Akanaani, Ahiti, Aamori, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
9 Zdaj torej, glej, k meni je prišlo vpitje Izraelovih otrok in videl sem tudi zatiranje, s kakršnim so jih Egipčani zatirali.
Ine ndamva ndithu kulira kwa Aisraeli, ndipo ndaona mmene Aigupto akuwazunzira.
10 Pridi torej zdaj in jaz te bom poslal k faraonu, da lahko privedeš moje ljudstvo, Izraelove otroke, iz Egipta.«
Kotero tsopano, pita. Ine ndikukutuma kwa Farao kuti ukatulutse anthu anga, Aisraeli mʼdziko la Igupto.”
11 Mojzes pa je Bogu rekel: »Kdo sem jaz, da bi šel k faraonu in da bi lahko Izraelove otroke privedel iz Egipta?«
Koma Mose anafunsa Mulungu, “Ine ndine yani kuti ndipite kwa Farao ndi kukatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto?”
12 Rekel je: »Zagotovo bom s teboj in to ti bodi simbol, da sem te jaz poslal. Ko boš ljudstvo privedel iz Egipta, boste na tej gori služili Bogu.«
Ndipo Mulungu anati, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro kwa iwe kuti ndine amene ndakutuma; Ukadzatulutsa anthu anga mʼdziko la Igupto, udzapembedza Mulungu pa phiri lino.”
13 Mojzes je Bogu rekel: »Glej, ko pridem k Izraelovim otrokom in jim bom rekel: ›K vam me je poslal Bog vaših očetov, ‹ pa mi bodo rekli: ›Kakšno je njegovo ime?‹ Kaj naj jim rečem?«
Mose anati kwa Mulungu, “Ngati ndipita kwa Aisraeli ndi kukawawuza kuti, ‘Mulungu wa makolo anu wandituma kwa inu,’ ndipo iwo nʼkukandifunsa kuti ‘Dzina lake ndi ndani?’ Tsono ine ndikawawuze chiyani?”
14 Bog je Mojzesu rekel: »JAZ SEM, KI SEM.« Rekel je: »Tako boš govoril Izraelovim otrokom: ›JAZ SEM me je poslal k vam.‹«
Mulungu anati kwa Mose, “NDINE AMENE NDILI. Izi ndi zimene ukanene kwa Aisraeli: ‘NDINE wandituma kwa inu.’”
15 Bog je Mojzesu poleg tega povedal: »Tako boš rekel Izraelovim otrokom: ›K vam me je poslal Gospod, Bog vaših očetov, Bog Abrahama, Bog Izaka in Bog Jakoba. To je moje ime na veke in to je moj spomin vsem rodovom.‹
Mulungu anatinso kwa Mose, “Ukanene kwa Aisraeli kuti ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo, wandituma kwa inu.’ Ili ndilo dzina langa mpaka muyaya, ndipo mibado ya mʼtsogolomo izidzanditchula ndi dzina limeneli.
16 Pojdi in zberi skupaj vse Izraelove starešine ter jim reci: ›Prikazal se mi je Gospod, Bog vaših očetov, Bog Abrahama, Izaka in Jakoba, rekoč: ›Zagotovo sem vas obiskal in videl to, kar vam je storjeno v Egiptu.‹«
“Pita, ukawasonkhanitse akuluakulu a Israeli ndipo ukati kwa iwo, ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, anandionekera ndipo akuti Iye wadzakuyenderani ndipo waona mmene Aigupto akukuzunzirani.
17 In rekel sem: »Jaz vas bom privedel gor iz egiptovske stiske v deželo Kánaancev, Hetejcev, Amoréjcev, Perizéjcev, Hivéjcev in Jebusejcev, v deželo, kjer tečeta mleko in med.
Choncho wanenetsa kuti adzakutulutsani mʼdziko la Igupto, dziko la masautsoli kupita ku dziko la Akanaani, Ahiti, Aamori Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’
18 Prisluhnili bodo tvojemu glasu in ti boš prišel, ti in Izraelove starešine, k egiptovskemu kralju in mu boste rekli: › Gospod, Bog Hebrejcev, se je srečal z nami in sedaj nas pusti iti, rotimo te, tri dni potovanja v divjino, da bomo lahko žrtvovali Gospodu, našemu Bogu.‹
“Akuluakulu a Israeli akakumvera. Kenaka iwe ndi akuluakuluwo mukapite kwa mfumu ya Igupto ndipo mukanene kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Ahebri, wakumana nafe. Tsono tikukupemphani kuti mutilole tipite pa ulendo wa masiku atatu mʼchipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu.’
19 Prepričan pa sem, da vam egiptovski kralj ne bo pustil oditi, ne, niti z mogočno roko ne.
Koma Ine ndikudziwa kuti mfumu ya Igupto sikakulolani kuti mupite pokhapokha Ine nditayikakamiza.
20 Svojo roko bom iztegnil in Egipt udaril z vsemi čudeži, ki jih bom storil v njihovi sredi in nató vas bo pustil oditi.
Tsono Ine ndidzatambasula dzanja langa ndi kukantha Aigupto ndi zodabwitsa zanga zimene ndidzazichita pakati pawo. Zikadzatha izi, Iye adzakulolani kuti mupite.
21 Temu ljudstvu bom dal naklonjenost v očeh Egipčanov in zgodilo se bo, ko greste, da ne boste odšli prazni,
“Ndipo ine ndidzafewetsa mtima wa Aigupto pa anthu anga, kotero kuti mukadzatuluka simudzapita wopanda kanthu.
22 temveč si bo vsaka ženska izposodila od sosede in od tiste, ki začasno biva v njeni hiši, dragocenosti iz srebra in dragocenosti iz zlata in oblačil, in vi jih boste nadeli na svoje sinove in na svoje hčere in boste oplenili Egipčane.«
Mkazi aliyense adzapemphe Mwigupto woyandikana naye ndiponso mkazi amene akukhala mʼnyumba yake, kuti amupatse ziwiya za siliva ndi golide ndiponso zovala zimene mudzaveka ana anu aamuna ndi aakazi. Ndipo potero mudzawalanda zonse Aiguptowo.”

< 2 Mojzes 3 >