< 2 Mojzes 23 >
1 Ne boš dvignil napačnega poročila. Svoje roke ne podaj z zlobnim, da bi bil nepravična priča.
“Usafalitse mbiri yabodza. Usathandize munthu wolakwa pomuchitira umboni wonama.
2 Ne boš sledil množici, da počneš zlo. Niti ne boš govoril v zadevi, da se ne nagneš za mnogimi, ki pačijo sodbo.
“Usatsate gulu la anthu ndi kuchita choyipa. Pamene ukupereka umboni mʼbwalo lamilandu, usakhotetse mlandu chifukwa chofuna kukondweretsa anthu ambiri.
3 Niti ne boš podpiral reveža v njegovi zadevi.
Ndipo poweruza mlandu wa munthu wosauka usamukondere.
4 Če srečaš vola svojega sovražnika ali njegovega osla zaiti, mu ga boš zagotovo ponovno privedel nazaj k njemu.
“Ngati ukumana ndi ngʼombe kapena bulu wa mdani wako zitasochera, uwonetsetse kuti wazitenga kupita nazo kwa mwini wakeyo.
5 Če vidiš osla tistega, ki te sovraži, ležati pod svojim bremenom in odlašaš, da mu pomagaš, mu boš zagotovo z njim vred pomagal.
Ngati uwona bulu wa munthu wina amene amakuda atagwa ndi katundu, usamusiye pomwepo, uwonetsetse kuti wamuthandiza.
6 Ne boš pačil sodbe ubogega v njegovi zadevi.
“Usakhotetse milandu ya anthu osauka.
7 Drži se proč od napačne stvari. Nedolžnega in pravičnega ne ubij, kajti zlobnega ne bom opravičil.
Upewe zabodza ndipo usaphetse munthu wosalakwa ndi wolungama, chifukwa Ine sindidzakhululukira wochimwa.
8 In ti ne boš prejel nobenega daru, kajti dar slepi modrega in izkrivlja besede pravičnega.
“Musamalandire chiphuphu, pakuti chiphuphu chimadetsa mʼmaso anthu oweruza ndi kusintha mawu awo kuti mlandu uyipire osalakwa.
9 Tudi ne boš zatiral tujca, kajti poznate srce tujca, glede na to, da ste bili tujci v egiptovski deželi.
“Usamuzunze mlendo, pakuti inu nomwe mukudziwa mmene amamvera mlendo chifukwa nanunso munali alendo mʼdziko la Igupto.
10 Šest let boš sejal svojo zemljo in zbiral njene sadove,
“Muzidzala mbewu zanu mʼmunda ndi kumakolola mbewuzo kwa zaka zisanu ndi chimodzi.
11 toda sedmo leto jo boš pustil počivati in mirno ležati, da ubogi izmed tvojega ljudstva lahko jedo. Kar bodo pustili, naj pojedo živali polja. Na podoben način boš postopal s svojim vinogradom in s svojim oljčnim nasadom.
Koma chaka chachisanu ndi chiwiri muzisiya osalima mindayo kuti anthu osauka pakati panu azipezamo chakudya, ndipo nyama zakuthengo zizidya zotsalazo. Muzichita chimodzimodzi ndi minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi.
12 Šest dni boš opravljal svoje delo, na sedmi dan pa boš počival, da bosta tvoj vol in tvoj osel lahko počivala in bosta sin tvoje pomočnice in tujec lahko osvežena.
“Muzigwira ntchito masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri musagwire ntchito kuti ngʼombe yanu ndi bulu wanu apume ndiponso kuti kapolo wobadwira mʼnyumba yanu ndi mlendo yemwe apezenso mphamvu.
13 V vseh stvareh, ki sem ti jih rekel, bodi preudaren. In ne omenjaj imena drugih bogov niti naj tega ne bo slišati iz tvojih ust.
“Samalani pochita zonse zimene ine ndanena. Musamapemphere kwa milungu ina ndipo mayina awo musamawatchule.
14 Trikrat v letu mi boš ohranjal praznovanje.
“Muzichita zikondwerero zolemekeza Ine katatu pa chaka.
15 Ohranjal boš praznik nekvašenega kruha (sedem dni boš jedel nekvašeni kruh, kakor sem ti zapovedal, v določenem času meseca abíba, kajti v njem si prišel iz Egipta in nihče se pred menoj ne bo prikazal prazen)
“Muzichita Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti monga ndinakulamulirani. Muzichita zimenezi mwezi wa Abibu pa nthawi yomwe ndayika, pakuti mʼmwezi umenewu munatuluka mʼdziko la Igupto. “Pasapezeke munthu wobwera pamaso panga wopanda kanthu mʼmanja.
16 in praznik žetve, prve sadove svojih trudov, ki si jih posejal na polju in praznik spravljanja, ki je ob koncu leta, ko si svoje trude pospravil s polja.
“Muzichita Chikondwerero cha Masika pogwiritsa ntchito zipatso zoyambirira kucha zimene munadzala mʼmunda. “Muzichitanso Chikondwerero cha Zokolola pakutha pa chaka, pamene mukututa zokolola zanu mʼmunda.
17 Trikrat na leto naj se vsi tvoji možje prikažejo pred Gospodom Bogom.
“Amuna onse azionekera pamaso pa Ambuye Yehova katatu pa chaka.
18 Krvi moje klavne daritve ne boš žrtvoval z vzhajanim kruhom niti naj maščoba mojega darovanja ne ostane do jutra.
“Musapereke magazi anyama ngati nsembe kwa Ine pamodzi ndi chilichonse chimene chili ndi yisiti. “Ndipo musasunge mafuta anyama yansembe ya pa chikondwerero mpaka mmawa.
19 Prvine od prvih sadov svoje zemlje boš prinesel v hišo Gospoda, svojega Boga. Kozlička ne boš zavrel v mleku njegove matere.
“Muzibwera ndi zipatso zoyambirira kucha zabwino kwambiri ku Nyumba ya Yehova Mulungu wanu. “Musamaphike kamwana kambuzi mu mkaka wa mayi wake.
20 Glej, pred teboj pošiljam Angela, da te varuje na poti in te privede na kraj, ki sem ga pripravil.
“Taona Ine ndikutuma mngelo wanga patsogolo panu kuti akutetezeni mʼnjiramo ndi kukakufikitsani ku malo amene ndakonza.
21 Pazi se ga in ubogaj njegov glas, ne izzivaj ga, kajti ne bo oprostil tvojih prestopkov, kajti moje ime je v njem.
Muzimumvera ndi kumvetsetsa zimene akunena. Musamuwukire chifukwa sadzakhululuka kuwukira kwanu, pakuti akuchita zimenezi mʼdzina langa.
22 Toda če boš zares ubogal njegov glas in storil vse, kar ti govorim, potem bom sovražnik tvojih sovražnikov in nasprotnik tvojih nasprotnikov.
Ngati mudzamvera iyeyu ndi kuchita zonse zimene Ine ndikunena, Ine ndidzakhala mdani wa adani anu ndipo ndidzatsutsana ndi onse otsutsana nanu.
23 Kajti moj Angel bo šel pred teboj in te privede k Amoréjcem, Hetejcem, Perizéjcem, Kánaancem, Hivéjcem in Jebusejcem, in jaz jih bom odrezal.
Mngelo wanga adzakhala patsogolo panu ndipo adzakufikitsani mʼdziko la Aamori, Ahiti, Aperezi, Akanaani, Ahivi ndi Ayebusi, ndipo ndidzawapheratu onsewo.
24 Ne boš se priklanjal njihovim bogovom niti jim služil niti počel po njihovih delih, temveč jih boš popolnoma premagal in popolnoma zlomil njihove podobe.
Musagwadire milungu yawo kapena kuyipembedza. Ndipo musatsatire zinthu zomwe amachita. Koma inu mukawononge milungu yawo ndi kuphwasula malo amene amapembedzerapo.
25 Služili boste Gospodu, svojemu Bogu in on bo blagoslovil tvoj kruh in tvojo vodo, in iz tvoje srede bom odvzel bolezen.
Muzipembedza Yehova Mulungu wanu ndipo adzakudalitsani ndi chakudya ndi madzi ndiponso ndidzachotsa nthenda pakati panu.
26 V tvoji deželi nič ne bo zavrglo svojih mladih niti ne bo jalovo. Število tvojih dni bom izpolnil.
Palibe mkazi amene adzapite padera kapena kukhala wosabereka mʼdziko mwanu. Ndidzakupatsani moyo wautali.
27 Pred teboj bom poslal svoj strah in uničil bom vsa ljudstva, h katerim boš prišel in vsem tvojim sovražnikom bom storil, da svoje hrbte obrnejo k tebi.
“Ine ndidzawachititsa mantha ndi kusokoneza anthu onse amene adzalimbana ndi inu ndipo adani anu onse adzakuthawani.
28 Pred teboj bom poslal sršene, ki bodo izpred tebe napodili Hivéjce, Kánaance in Hetejce.
Ahivi, Akanaani ndi Ahiti adzathawa ngati kuti ndawatumizira mavu.
29 Izpred tebe jih ne bom pognal v enem letu, da ne bi zemlja postala zapuščena in bi se zoper tebe namnožile poljske zveri.
Komabe sindidzawachotseratu onse mʼchaka chimodzi chifukwa dziko lingadzakhale lopanda anthu ndipo nyama zakuthengo zidzakuchulukirani.
30 Po malo in malo jih bom podil izpred tebe, dokler ne boš narasel in podedoval dežele.
Ndidzawathamangitsa pangʼonopangʼono mpaka inu mutachuluka kokwanira mwakuti nʼkutenga dzikolo.
31 Tvoje meje bom postavil od Rdečega morja, celo do morja Filistejcev in od puščave do reke, kajti jaz bom prebivalce dežele izročil v tvojo roko, ti pa jih boš pognal pred seboj.
“Malire a dziko lanu adzakhala kuyambira ku Nyanja Yofiira mpaka ku nyanja ya Afilisti, ndiponso kuyambira ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yufurate. Anthu onse okhala mʼdziko limeneli ndidzawapereka mʼmanja mwanu ndipo mudzawathamangitsa.
32 Z njimi ne boš sklenil nobene zaveze niti z njihovimi bogovi.
Musachite pangano ndi iwo kapena ndi milungu yawo.
33 Naj ne prebivajo v tvoji deželi, da te ne bi pripravili grešiti zoper mene, kajti če boš služil njihovim bogovom, ti bodo le-ti zagotovo zanka.«
Asadzakhale mʼdziko lanu chifukwa angadzakuchimwitseni ndi kuyamba kupembedza milungu yawo. Mukadzatero ndiye kuti mwakodwa mu msampha.”