< Pridigar 11 >

1 Svoj kruh vrzi na vode, kajti našel ga boš po mnogih dneh.
Ponya chakudya chako pa madzi, udzachipezanso patapita masiku ambiri.
2 Daj delež sedmim in tudi osmemu, kajti ne veš kakšno zlo bo na zemlji.
Ndalama zako uzisungitse kwa anthu asanu ndi awiri, inde kwa anthu asanu ndi atatu, pakuti sudziwa ndi tsoka lanji limene likubwera pa dziko.
3 Če so oblaki polni dežja, se izlijejo na zemljo, in če drevo pade proti jugu ali proti severu, na kraj, kamor drevo pade, tam bo.
Ngati mitambo yadzaza ndi madzi, imagwetsa mvula pa dziko lapansi. Mtengo ukagwera cha kummwera kapena cha kumpoto, ndiye kuti udzagonera kumene wagwerako.
4 Kdor opazuje veter, ne bo sejal in kdor se ozira na oblake, ne bo žel.
Amene amayangʼana mphepo sadzadzala; amene amayangʼana mitambo sadzakolola.
5 Kakor ne veš kakšna je pot duha niti kako rastejo kosti v maternici tiste, ki je z otrokom; tako ne poznaš del Boga, ki dela vse.
Momwe sudziwira mayendedwe a mphepo, kapena momwe mzimu umalowera mʼthupi la mwana mʼmimba mwa amayi, momwemonso sungathe kudziwa ntchito za Mulungu, Mlengi wa zinthu zonse.
6 Zjutraj sej svoje seme in zvečer ne zadržuj svoje roke, kajti ne veš, ali bo uspevalo to ali ono, ali pa bosta oba enako dobra.
Dzala mbewu zako mmawa ndipo madzulo usamangoti manja lobodo, pakuti sudziwa chimene chidzapindula, mwina ichi kapena icho, kapena mwina zonse ziwiri zidzachita bwino.
7 Resnično, svetloba je prijazna in prijetna stvar je za oči, da gledajo sonce,
Kuwala nʼkwabwino, ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.
8 toda če človek živi mnogo let in se veseli v njih vseh, naj se vendar spomni dni teme, kajti mnogo jih bo. Vse, kar prihaja, je ničevost.
Munthu akakhala wa zaka zambiri, mulekeni akondwerere zaka zonsezo, koma iye azikumbukira masiku a mdima, pakuti adzakhala ochuluka. Chilichonse chimene chikubwera ndi chopanda phindu.
9 Razveseli se, oh mladenič, v svoji mladosti in naj te tvoje srce spodbuja v dneh tvoje mladosti in hodi po poteh svojega srca in za pogledom svojih oči; toda vedi, da te bo Bog zaradi vseh teh stvari privedel v obsodbo.
Kondwera mnyamata iwe, pamene ukanali wamngʼono, ndipo mtima wako usangalale pa nthawi ya unyamata wako. Tsatira zimene mtima wako ukufuna, ndiponso zimene maso ako akuona, koma dziwa kuti pa zinthu zonsezo Mulungu adzakuweruza.
10 Zatorej od svojega srca odstrani bridkost in odloži zlo od svojega mesa, kajti otroštvo in mladost sta ničevost.
Choncho uchotse zokusautsa mu mtima mwako, upewe zokupweteka mʼthupi mwako, pakuti unyamata ndi ubwana ndi zopandapake.

< Pridigar 11 >