< 5 Mojzes 21 >

1 Če je nekdo najden ubit na polju, ki ti ga Gospod, tvoj Bog, daje v last, ležeč na polju in se ne ve kdo ga je umoril,
Ngati munthu apezeka ataphedwa mʼmunda mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kukhala lanu koma inu osadziwa amene wamupha,
2 potem bodo prišli tvoje starešine in tvoji sodniki in bodo izmerili [razdaljo] do mest, ki so naokoli tega, ki je umorjen.
akuluakulu anu ndi oweruza adzapite ndi kuyeza kutalikirana kuchokera pamene pali mtembowo ndi mizinda yoyandikira.
3 Zgodilo se bo, da mesto, ki je bliže umorjenemu človeku, celo starešine tega mesta bodo vzeli telico, s katero še niso delali in ki še ni vlekla jarma,
Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzatenge ngʼombe imene sinagwirepo ntchito kapena kuvalapo goli
4 in starešine tega mesta bodo telico privedli dol v valovito dolino, ki ni niti obdelana niti posejana in tam, v dolini, bodo telici zlomili vrat
ndi kuyikusira ku chigwa chimene sichinalimidwepo ndiponso kumene kuli mtsinje woyenda. Ku chigwa kumeneko ayenera kukayithyola khosi ngʼombeyo.
5 in duhovniki, sinovi Lévijevcev, se bodo približali, kajti njih je Gospod, tvoj Bog, izbral, da mu služijo in da blagoslavljajo v Gospodovem imenu, in po njihovi besedi bo vsaka polemika in vsak udarec preizkušen
Ansembe, ana a Aaroni, adzapite patsogolo pangʼono, popeza ndiwo amene Yehova Mulungu wanu anawasankha kuti azitumikira, kupereka mdalitso mʼdzina la Yehova ndi kugamula milandu yonse yamikangano ndi yovulazana.
6 in vse starešine tega mesta, ki je bliže umorjenemu človeku, si bodo roke umili nad telico, ki je obglavljena v dolini
Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzasamba mʼmanja pamwamba pa ngʼombe yothyoledwa khosi ija,
7 in odgovorili bodo ter rekli: ›Naše roke niso prelile te krvi niti naše oči tega niso videle.
nadzatsimikiza kuti, “Manja athu sanakhetse magazi awa ndipo sitinaonerere kuphedwako.
8 Bodi usmiljen, oh Gospod, svojemu ljudstvu Izraelu, ki si ga odkupil in ne polagaj nedolžne krvi na svoje ljudstvo Izrael, ki je najbliže.‹ In kri jim bo odpuščena.
Yehova, landirani nsembe yopepesa ya anthu anu Aisraeli amene munawapulumutsa, ndipo muwakhululukire tchimo la kupha munthu wosalakwa.” Mukatero ndiye kuti adzapezeka kuti ndi osalakwa.
9 Tako boš izmed sebe odvzel krivdo nedolžne krvi, ko boš storil to, kar je pravilno v Gospodovih očeh.
Kotero mudzadzichotsera nokha tchimo lokhetsa magazi wosalakwa, popeza mwachita zoyenera pamaso pa Yehova.
10 Ko greš naprej v vojno zoper svoje sovražnike in ti jih Gospod, tvoj Bog, izroči v tvoje roke in si jih zajel kot ujetnike
Mukapita kukachita nkhondo ndi adani anu, Yehova Mulungu wanu nawapereka adani anuwo mʼmanja mwanu muwagwira ukapolo,
11 in vidiš med ujetniki lepo žensko in imaš do nje poželenje, da bi jo imel za svojo ženo,
ndiye ngati muona mkazi wokongola pakati pa ogwidwawo nakutengani mtima, mukhoza kumutenga kuti akhale mkazi wanu.
12 potem jo boš privedel domov, v svojo hišo. Ona si bo obrila svojo glavo in postrigla svoje nohte
Mumutengere ku nyumba kwanu, kumumeta tsitsi lake, mumuwenge zikhadabo zake
13 in iz sebe bo odložila oblačila svojega ujetništva in ostala bo v tvoji hiši in cel mesec bo objokovala svojega očeta in svojo mater. Potem boš šel noter k njej in boš njen soprog in ona bo tvoja žena.
ndipo avulidwe zovala zimene anagwidwa nazo. Atakhala mʼnyumba mwanu nalira maliro a abambo ndi amayi ake kwa mwezi wathunthu, ndiye mukhoza kupita kwa iye ndi kukhala mwamuna wake ndipo iyeyo adzakhala mkazi wanu.
14 In zgodilo se bo, če z njo ne boš imel veselja, potem jo boš pustil oditi kamor ona hoče. Toda, ker si jo ponižal, je nikakor ne boš prodal za denar, iz nje ne boš naredil trgovskega blaga.
Ngati simukukondweretsedwa naye, muloleni kuti apite kumene afuna. Musamugulitse kapena kumuzunza ngati kapolo, popeza mwamuchotsa ulemu.
15 Če ima mož dve ženi, eno ljubljeno in drugo osovraženo in sta mu rodili otroke, obe, ljubljena in osovražena in če je prvorojenec od tiste, ki je bila osovražena,
Ngati munthu ali ndi akazi awiri, nakonda wina koposa mnzake, onsewa ndikubereka ana aamuna koma woyamba nakhala mwana wa mkazi amene samukondayo,
16 potem se bo zgodilo, ko daje svojim sinovom podedovati to, kar ima, da ne sme narediti sina ljubljene prvorojenca pred sinom osovražene, ki je zares prvorojenec,
akamagawa chuma chake akanali moyo kwa ana akewo, asapereke ufulu wa mwana woyamba kubadwa kwa mwana wamwamuna wa mkazi amene amamukonda mʼmalo mwa mwana wake woyamba kubadwa weniweni amene ndi mwana wamkazi amene samukonda.
17 temveč bo sina osovražene priznal za prvorojenca s tem, da mu da dvojni delež od vsega, kar ima, kajti on je začetek njegove moči; pravica prvorojenca je njegova.
Iye ayenera kuonetsa kuti mwana wake wamwamuna wa mkazi wosakondedwayo ndiye woyamba kubadwa pomupatsa miyeso iwiri ya zonse zimene ali nazo. Mwana wamwamuna ameneyo ndiye chizindikiro cha mphamvu za abambo ake. Ufulu wokhala mwana wamwamuna woyamba ndi wake.
18 Če ima človek trmoglavega in upornega sina, ki noče ubogati glasu svojega očeta ali glasu svoje matere in ko sta ga karala, da ju noče poslušati,
Ngati munthu ali ndi mwana wamwamuna wosamvera ndi wowukira amene samvera a abambo ake ndi amayi ake akamuweruza,
19 potem naj ga njegov oče in njegova mati primeta in ga privedeta k starešinam njegovega mesta in k velikim vratom njegovega kraja
abambo ndi amayi ake amugwire ndi kupita naye kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda wake ndipo
20 in starešinam mesta bosta rekla: ›Ta najin sin je trmoglav in uporen, noče ubogati najinega glasu. Požeruh je in pijanec.‹
akawawuze akuluakuluwo kuti, “Mwana wathu wamwamunayu ndi wosamva ndi wowukira. Iyeyu satimvera. Ndi mwana wadyera komanso ndi chidakwa.”
21 In vsi ljudje iz njegovega mesta ga bodo kamnali s kamni, da ta umre. Tako boš zlo odstranil proč izmed vas in ves Izrael bo slišal in se bal.
Pamenepo anthu onse a mu mzinda wake adzamuphe ndi miyala. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu. Aisraeli onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha.
22 Če je moški zagrešil greh, vreden smrti, in bo usmrčen in ga obesiš na drevo,
Ngati munthu wopezeka ndi mlandu wopha mnzake waphedwa ndipo mtembo wake wapachikidwa pamtengo,
23 naj njegovo truplo ne ostane vso noč na drevesu, temveč ga boš vsekakor tisti dan pokopal (kajti ta, ki je obešen, je preklet od Boga), da tvoja dežela, ki ti jo Gospod, tvoj Bog, daje za dediščino, ne bo omadeževana.
musasiye mtembowo pa mtengopo usiku wonse. Muonetsetse kuti mwakawukwirira tsiku lomwelo, chifukwa aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa ndi Mulungu. Musayipitse dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani ngati cholowa chanu.

< 5 Mojzes 21 >