< 2 Samuel 24 >

1 In ponovno je bila vžgana Gospodova jeza zoper Izrael in zoper njih je napeljal Davida, da reče: »Pojdite, preštejte Izraela in Juda.«
Nthawi inanso Yehova anawakwiyira Aisraeli ndipo anawutsa mtima wa Davide kuti awavutitse ndipo anati, “Pita kawerenge Aisraeli ndi Ayuda.”
2 Kajti kralj je rekel Joábu, poveljniku vojske, ki je bila z njim: »Pojdite sedaj skozi vse Izraelove rodove, od Dana, celo do Beeršébe in preštejte ljudstvo, da bom lahko vedel število ljudstva.«
Choncho mfumu inati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali nawo. “Pitani pakati pa mafuko onse a Israeli kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba kuti mukawerenge anthu omenya nkhondo ndi cholinga choti ndidziwe chiwerengero chawo.”
3 Joáb pa je rekel kralju: »Torej Gospod, tvoj Bog, [naj] doda ljudstvu, kolikokrat že, stokratno in da bodo oči mojega gospoda kralja lahko to videle, toda zakaj se moj gospod kralj razveseljuje v tej stvari?«
Koma Yowabu anayankha mfumu kuti, “Yehova Mulungu wanu achulukitse ankhondo anu kukhala miyandamiyanda, ndipo alole inu mbuye wanga mfumu mudzazione zimenezi. Koma nʼchifukwa chiyani inu mbuye wanga mfumu mukufuna kuchita zimenezi?”
4 Vendar je kraljeva beseda prevladala zoper Joába in zoper poveljnike vojske. In Joáb in poveljniki vojske so odšli izpred kraljeve prisotnosti, da preštejejo Izraelsko ljudstvo.
Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu ndi atsogoleri a ankhondo. Choncho anachoka pamaso pa mfumu kupita kukawerenga anthu omenya nkhondo mu Israeli.
5 Prečkali so Jordan in se utaborili v Aroêrju, na desni strani mesta, ki leži v sredi reke Gad in proti Jazêrju.
Atawoloka Yorodani, iwo anamanga misasa yawo pafupi ndi Aroeri kummwera kwa mzinda wa ku chigwa ndipo kenaka iwo anapita ku dziko la Gadi mpaka ku Yazeri.
6 Potem so prišli v Gileád in v deželo Tahtím Hodší; in prišli so v Dan Jáan in okoli k Sidónu
Iwo anapita ku Giliyadi ndi ku chigwa cha Tahitimu Hodisi ndipo anapitirira mpaka ku Dani Yaani ndi madera ozungulira Sidoni.
7 in prišli so k močnemu oporišču Tir in k vsem mestom Hivéjcev in Kánaancev in odšli so ven k južnemu Judu, celó do Beeršébe.
Kenaka iwo anapita molunjika linga la ku Turo ndi ku mizinda yonse ya Ahivi ndi Akanaani. Pomaliza anapita ku Beeriseba ku Negevi wa ku Yuda.
8 Torej ko so šli skozi vso deželo, so ob koncu devetih mesecev in dvajsetih dni prišli v Jeruzalem.
Atayendayenda mʼdziko lonse anabwerera ku Yerusalemu patapita miyezi isanu ndi inayi ndi masiku makumi awiri.
9 Joáb je kralju izročil vsoto števila ljudstva. Tam je bilo v Izraelu osemsto tisoč hrabrih mož, ki so izdirali meč in Judovih mož je bilo petsto tisoč mož.
Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa mfumu: Mu Israeli munali anthu 800,000 amphamvu amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga ndipo mu Yuda munali anthu 500,000.
10 Davidovo srce pa ga je udarilo, potem ko je imel ljudstvo prešteto. David je rekel Gospodu: »Silno sem grešil v tem, kar sem storil in sedaj te rotim, oh Gospod, odvzemi krivičnost svojega služabnika, kajti postopal sem zelo nespametno.«
Davide anatsutsika mu mtima mwake atatha kuwerenga anthuwo ndipo anapemphera kwa Yehova kuti, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono Yehova, ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”
11 Kajti ko je bil David zjutraj pokonci, je k Davidovemu vidcu, preroku Gadu, prišla beseda od Gospoda, rekoč:
Davide asanadzuke mmawa mwake mawu a Yehova anafika kwa mneneri Gadi, mlosi wa Davide kuti,
12 »Pojdi in reci Davidu: ›Tako govori Gospod, ponujam ti tri stvari. Izberi eno izmed njih, da ti jo lahko storim.‹«
“Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’”
13 Tako je Gad prišel k Davidu in mu povedal ter mu rekel: »Ali naj pride k tebi, v tvojo deželo, sedem let lakote? Ali hočeš tri mesece bežati pred svojimi sovražniki, medtem ko te zasledujejo? Ali, da bo v tvoji deželi tridnevna kužna bolezen? Sedaj se posvetuj in glej, kakšen odgovor naj vrnem tistemu, ki me je poslal.«
Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa iye, “Kodi mungakonde kuti mʼdziko mwanu mukhale njala kwa zaka zitatu? Kapena kuti mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu? Kapena kuti mʼdziko muno mukhale mliri kwa masiku atatu? Tsopano, ganizirani bwino ndipo musankhe chomwe mudzamuyankhe amene wandituma.”
14 David je Gadu rekel: »V veliki stiski sem. Naj torej pademo v Gospodovo roko, kajti njegova usmiljenja so velika in naj ne padem v roko človeka.«
Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ife atilange ndi Yehova pakuti chifundo chake ndi chachikulu, koma ndisalangidwe ndi anthu.”
15 Tako je Gospod nad Izrael poslal kužno bolezen od jutra celo do določenega časa in tam je umrlo izmed ljudstva, od Dana, celo do Beeršébe, sedemdeset tisoč mož.
Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, kuyambira mmawa mpaka pa nthawi imene anafuna mwini wake, ndipo unapha anthu 70,000 kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba.
16 Ko je angel svojo roko iztegnil nad Jeruzalem, da ga uniči, se je Gospod pokesal od zla in rekel angelu, ki je uničeval ljudstvo: »Dovolj je. Zadrži sedaj svojo roko.« Gospodov angel pa je bil pri kraju mlatišča Jebusejca Arávna.
Pamene mngelo anatambasula dzanja lake kuti awononge Yerusalemu, Yehova anamva chisoni chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
17 David je spregovoril Gospodu, ko je videl angela, ki je udaril ljudstvo in rekel: »Glej! Grešil sem, storil sem zlobno. Toda te ovce, kaj so storile? Naj bo tvoja roka, prosim te, zoper mene in zoper hišo mojega očeta.«
Davide ataona mngelo amene ankakantha anthu uja, anati kwa Yehova, “Ine ndi amene ndachimwa. Ine mʼbusa ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Langani ineyo pamodzi ndi banja langa.”
18 Gad je ta dan prišel k Davidu in mu rekel: »Pojdi gor, zgradi oltar Gospodu na mlatišču Jebusejca Arávna.«
Tsiku limenelo Gadi anapita kwa Davide ndi kukanena kuti, “Pitani kamangeni guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.”
19 David je, glede na Gadovo izjavo, odšel gor, kakor je Gospod ukazal.
Ndipo Davide anapita monga momwe Yehova anamulamulira kudzera mwa Gadi.
20 Arávna je pogledal in zagledal kralja ter njegove služabnike prihajati proti njemu. Arávna je odšel ven in se upognil pred kraljem na svoj obraz k tlom.
Arauna atayangʼana ndi kuona mfumu ndi anthu ake akubwera kumene kunali iye, iyeyo anatuluka ndi kuwerama pamaso pa mfumu mpaka nkhope yake kugunda pansi.
21 Arávna je rekel: »Čemu je moj gospod kralj prišel k svojemu služabniku?« David je rekel: »Da od tebe kupim mlatišče, da zgradim oltar Gospodu, da bo kuga lahko ustavljena pred ljudstvom.«
Arauna anati, “Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mfumu mwabwera kwa mtumiki wanu?” Davide anayankha kuti, “Kudzagula malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe kuti mliri uli pa anthuwa usiye.”
22 Arávna je rekel Davidu: »Naj moj gospod kralj vzame in daruje, kar se mu zdi dobro. Glej, tukaj so voli za žgalno daritev in mlatilne priprave in druge volovske priprave za drva.«
Arauna anati kwa Davide, “Mbuye wanga mfumu mutenge chilichonse chimene chikukondweretseni ndi kuchipereka nsembe. Nazi ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, nazi zopunthira tirigu ndi magoli angʼombe kuti zikhale nkhuni.
23 Vse te stvari je Arávna, kakor kralj, dal kralju. In Arávna je rekel kralju: » Gospod, tvoj Bog, [naj] te sprejme.«
Inu mfumu, Arauna akupereka zonsezi kwa inu mfumu.” Arauna anatinso kwa iye, “Yehova Mulungu wanu akuvomerezeni.”
24 Kralj pa je Arávnu rekel: »Ne; temveč bom to zagotovo kupil od tebe za ceno. Niti ne bom daroval žgalne daritve Gospodu, svojemu Bogu od tega, kar me nič ne stane.« Tako je David kupil mlatišče in vole za petdeset šeklov srebra.
Koma mfumu inayankha Arauna kuti, “Ayi, Ine ndikunenetsa kuti ndikulipira. Sindidzapereka kwa Yehova Mulungu wanga nsembe yopsereza imene sindinavutikire.” Kotero Davide anagula malo wopunthira tiriguwo ndi ngʼombe ndipo anapereka kwa Araunayo masekeli asiliva makumi asanu.
25 David je tam zgradil oltar Gospodu in daroval žgalne daritve in mirovne daritve. Tako je bil Gospod izprošen za deželo in kuga se je ustavila pred Izraelom.
Davide anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Ndipo Yehova anayankha pempherolo mʼmalo mwa dziko lonse, ndipo mliri unatha pa Aisraeli.

< 2 Samuel 24 >