< 2 Samuel 14 >
1 Torej Cerújin sin Joáb je zaznal, da je bilo kraljevo srce [nagnjeno] k Absalomu.
Yowabu mwana wa Zeruya anadziwa kuti maganizo a mfumu ali pa Abisalomu.
2 Joáb je poslal v Tekóo in od tam privedel modro žensko ter ji rekel: »Prosim te, hlini se, da si žalovalka in sedaj si nadeni žalovalno obleko in se ne mazili z oljem, temveč bodi kakor ženska, ki je dolgo časa žalovala za mrtvim
Kotero Yowabu anatuma munthu wina kupita ku Tekowa ndi kukatengako mkazi wanzeru. Yowabu anati kwa mkaziyo, “Ukhale ngati namfedwa. Uvale zovala zaumasiye ndipo usadzole mafuta ena aliwonse. Ukhale ngati mkazi amene wakhala akulira masiku ambiri.
3 in pojdi h kralju in mu govori na ta način.« Tako je Joáb položil besede v njena usta.
Kenaka upite kwa mfumu ndipo ukayankhule mawu awa.” Ndipo Yowabu anamuwuza mawu oti akanene.
4 Ko je ženska iz Tekóe govorila kralju, je padla na svoj obraz do tal in se globoko priklonila ter rekla: »Pomagaj, oh kralj.«
Mkazi wochokera ku Tekowa uja atapita kwa mfumu anadzigwetsa pansi, napereka ulemu kwa mfumu nati, “Thandizeni mfumu!”
5 Kralj ji je rekel: »Kaj te pesti?« Odgovorila je: »Res sem vdova in moj soprog je mrtev.
Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi chikukusautsa iwe nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga anamwalira.
6 Tvoja pomočnica je imela dva sinova in skupaj sta se prepirala na polju in tam ni bilo nobenega, da ju loči, temveč je eden udaril drugega in ga usmrtil.
Ine wantchito wanu ndinali ndi ana aamuna awiri. Iwo anayamba kumenyana mʼmunda, ndipo panalibe woti awaleretse. Wina anakantha mnzakeyo mpaka kumupha.
7 Glej, celotna družina je vstala zoper tvojo pomočnico in rekli so: ›Izroči tega, ki je usmrtil svojega brata, da ga bomo lahko ubili za življenje njegovega brata, ki ga je usmrtil in tudi dediča bomo uničili.‹ Tako bodo pogasili moj ogorek, ki je ostal in mojemu soprogu ne bodo pustili niti imena niti ostanka na tej zemlji.«
Tsono banja lonse landiwukira ine, wantchito wanu. Iwo akuti, ‘Utipatse mwana amene anakantha mʼbale wakeyo kuti timuphe chifukwa cha moyo wa mʼbale wake amene anaphedwayo. Ife tidzaphanso mlowamʼmalo.’ Anthuwo adzapha mwana wanga amene wanditsalira, ndipo dzina la mwamuna wanga silidzakumbukika pakuti sipadzakhalanso mwana pa banja lathu.”
8 Kralj je rekel ženski: »Pojdi k svoji hiši in glede tebe dal bom zadolžitev.«
Mfumu inati kwa mkaziyo, “Pitani ku nyumba kwanu ndipo ine ndidzalamula mʼmalo mwanu.”
9 Ženska iz Tekóe je rekla kralju: »Moj gospod, oh kralj, krivičnost bodi na meni in na hiši mojega očeta, kralj in njegov prestol pa naj bosta brez krivde.«
Koma mkazi wochokera ku Tekowayo anati kwa mfumu, “Mbuye wanga mfumu, kulakwa kukhale pa ine ndi banja la abambo anga ndipo mfumu ndi mpando wanu waufumu mukhale osalakwa.”
10 Kralj je rekel: »Kdorkoli ti karkoli reče, ga privedi k meni in ne bo se te več dotaknil.«
Mfumu inayankha kuti, “Ngati wina aliyense anene kanthu kwa iwe, umubweretse kwa ine, ndipo sadzakuvutitsanso.”
11 Potem je rekla: »Prosim te, naj se kralj spomni Gospoda, svojega Boga, da ti nočeš trpeti, da krvni maščevalci še naprej uničujejo, da ne bi uničili mojega sina.« Rekel je: »Kakor Gospod živi niti en las tvojega sina ne bo padel k zemlji.«
Mkaziyo anati, “Mfumu ipemphe kwa Yehova Mulungu wake kuti aletse wobwezera imfa asaphenso wina kuti mwana wanga asawonongedwe.” Mfumu inati, “Pali Yehova wamoyo ngakhale tsitsi limodzi la pamutu pa mwana wako silidzathotholedwa.”
12 Potem je ženska rekla: »Naj tvoja pomočnica, prosim te, spregovori eno besedo mojemu gospodu kralju.« In ta je rekel: »Povej.«
Kenaka mkaziyo anati, “Lolani kuti wantchito wanu ayankhule mawu kwa inu mbuye wanga mfumu.” Iye anayankha kuti, “Yankhula.”
13 Ženska je rekla: »Zakaj si potem mislil storiti takšno stvar zoper Božje ljudstvo? Kajti kralj govori to stvar kakor nekdo, ki je pomanjkljiv, v tem, da kralj ne privede ponovno domov svojega pregnanega.
Mkaziyo anati, “Nʼchiyani tsono chimene mwaganiza kuchitira zimenezi anthu a Mulungu? Pamene mfumu yanena izi, kodi sikudzitsutsa yokha, pakuti mfumu sinayitanitse mwana amene anamupirikitsa?
14 Kajti mi moramo umreti in smo kakor voda, razlita na tla, ki ne more biti ponovno zbrana niti Bog ne upošteva nobene osebe, vendar snuje način, da njegov pregnani ne bo izključen od njega.
Koma poti madzi akatayika sawoleka, ndiye tonsefe tiyenera kufa ndithu. Koma Mulungu safuna kuti moyo wa munthu utayike kotero anakonza njira yakuti wopirikitsidwayo asakhale wotayikiratu.
15 Zdaj torej, ko sem prišla, da o tej stvari govorim mojemu gospodu kralju, je to zato, ker me je ljudstvo prestrašilo. Tvoja pomočnica je rekla: ›Spregovorila bom torej kralju. Lahko se zgodi, da bo kralj izpolnil zahtevo svoje pomočnice.‹
“Tsopano ine ndabwera kudzanena izi kwa inu mbuye wanga mfumu chifukwa anthu andichititsa mantha. Mdzakazi wanu anaganiza kuti, ‘Ndikayankhula kwa mfumu, mwina adzachita zimene mdzakazi wake adzamupempha.
16 Kajti kralj bo slišal, da svojo pomočnico osvobodi iz roke človeka, ki hoče skupaj uničiti tako mene in mojega sina iz Božje dediščine.
Mwina mfumu idzavomereza kupulumutsa mdzakazi wake mʼdzanja la munthu amene akufuna kupha ine pamodzi ndi mwana wanga kutichotsa pa cholowa chimene Mulungu anatipatsa.’
17 Potem je tvoja pomočnica rekla Gospodu: ›Beseda mojega gospoda kralja bo sedaj tolažilna, kajti kakor angel od Boga, tako je moj gospod kralj, da razlikuje dobro in slabo, zato bo Gospod, tvoj Bog, s teboj.‹«
“Ndipo tsopano mtumiki wanu akuti, ‘Lolani mawu a mbuye wanga mfumu abweretse mpumulo kwa ine, pakuti mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu pozindikira chabwino ndi choyipa. Yehova Mulungu wanu akhale nanu.’”
18 Potem je kralj ženski odgovoril in rekel: »Ne skrivaj pred menoj, prosim te, stvari, ki jo bom vprašal.« Ženska je rekla: »Naj moj gospod kralj sedaj spregovori.«
Kenaka mfumu inati kwa mkaziyo, “Usandibisire chilichonse pondiyankha chimene ndidzakufunsa.” Mkaziyo anati, “Mbuye wanga mfumu yankhulani.”
19 Kralj je rekel: » Mar ni v vsem tem s teboj Joábova roka?« Ženska je odgovorila ter rekla: » Kakor živi tvoja duša, moj gospod kralj, nihče se ne more izogniti ne na desno ne na levo od tega, kar je moj gospod kralj govoril, kajti tvoj služabnik Joáb mi je zaukazal in on je položil vse te besede v usta tvoje pomočnice,
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi zimenezi sukuchita motsogozedwa ndi Yowabu?” Mkaziyo anayankha kuti, “Pali inu wamoyo, mbuye wanga mfumu, palibe munthu angakhotere kumanja kapena kumanzere pa chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mwanena. Inde, ndi mtumiki wanu Yowabu amene wandilangiza ine kuchita zimenezi ndipo ndi amene anandipatsa mawu onsewa woti ine mtumiki wanu ndiyankhule.
20 da privleče na dan to obliko govora, je tvoj služabnik Joáb storil to stvar. In moj gospod je moder, glede na modrost Božjega angela, da ve vse stvari, ki so na zemlji.«
Mtumiki wanu Yowabu anachita zimenezi kuti asinthe mmene zinthu zilili lero. Mbuye wanga muli ndi nzeru ngati za mngelo wa Mulungu. Mumadziwa zonse zimene zikuchitika mʼdziko.”
21 Kralj je rekel Joábu: »Glej torej, jaz sem storil to stvar, zato pojdi, ponovno privedi mladeniča Absaloma.«
Mfumu inati kwa Yowabu, “Chabwino, ine ndichita zimenezi. Pita kamutenge Abisalomuyo.”
22 Joáb je padel k tlom, na svoj obraz, se upognil in zahvalil kralju in Joáb je rekel: »Danes tvoj služabnik vé, da sem našel milost v tvojem pogledu, moj gospod, oh kralj, v tem, da je kralj izpolnil zahtevo svojega služabnika.«
Yowabu anawerama pansi kupereka ulemu kwa mfumu. Yowabuyo anati, “Lero mtumiki wanu wadziwa kuti wapeza chifundo pamaso panu, mbuye wanga mfumu, chifukwa mwavomera pempho lakeli.”
23 Tako je Joáb vstal in odšel v Gešur in Absaloma privedel v Jeruzalem.
Choncho Yowabu anapita ku Gesuri ndipo anamubweretsa Abisalomu ku Yerusalemu.
24 Kralj je rekel: »Naj se obrne k svoji lastni hiši in naj ne vidi mojega obraza.« Tako se je Absalom vrnil k svoji lastni hiši in ni videl kraljevega obraza.
Koma mfumu inati, “Iye apite ku nyumba yake; asaone nkhope yanga.” Kotero Abisalomu anapita ku nyumba yake ndipo sanakumane ndi mfumu.
25 Toda v vsem Izraelu ni bilo nikogar, da bi bil tako zelo hvaljen zaradi svoje lepote kakor Absalom. Od podplata svojega stopala, celo do krone njegove glave, ni bilo na njem nobenega madeža.
Mʼdziko lonse la Israeli munalibe munthu amene anayamikidwa chifukwa cha maonekedwe ake wokongola ngati Abisalomu. Kuyambira kumutu mpaka ku mapazi ake, analibe chilema.
26 In ko je ostrigel svojo glavo (kajti ob koncu vsakega leta si jo je ostrigel, ker so bili lasje na njem težki, zato jo je ostrigel) si je stehtal lase svoje glave, dvesto šeklov po kraljevi teži.
Nthawi ina iliyonse akamameta tsitsi lake, ankameta pamene layamba kumulemera. Akatero amaliyeza, ndipo limalemera makilogalamu awiri pa sikelo yaufumu.
27 Absalomu so se tam rodili trije sinovi in ena hči, ki ji je bilo ime Tamara. Bila je ženska lepega obličja.
Abisalomu anali ndi ana aamuna atatu ndi wamkazi mmodzi. Mwana wamkazi dzina lake linali Tamara, ndipo anali mkazi wokongola kwambiri.
28 Tako je Absalom dve polni leti prebival v Jeruzalemu in ni videl kraljevega obraza.
Abisalomu anakhala zaka ziwiri mu Yerusalemu osaonekera kwa mfumu.
29 Zato je Absalom poslal po Joába, da ga pošlje h kralju, toda ta ni hotel priti k njemu in ko je drugič ponovno poslal, ta ni hotel priti.
Kenaka Abisalomu anatumiza mawu kwa Yowabu, kumutuma kuti apite kwa mfumu, koma Yowabu anakana kubwera. Kotero anatumizanso mawu kachiwiri, koma Yowabu anakananso.
30 Zato je rekel svojim služabnikom: »Glejte, Joábovo polje je v bližini mojega in tam ima ječmen. Pojdite in ga požgite.« In Absalomovi služabniki so zažgali polje.
Tsono Abisalomu anati kwa antchito ake, “Taonani, munda wa Yowabu uli pafupi ndi wanga ndipo muli barele mʼmenemo. Pitani mukawutenthe mundawo.” Ndipo antchito a Abisalomu anawutentha mundawo.
31 Potem je Joáb vstal in prišel k Absalomu v njegovo hišo ter mu rekel: »Zakaj so tvoji služabniki zažgali moje polje?«
Ndipo Yowabu anapita ku nyumba ya Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani antchito ako atentha munda wanga?”
32 Absalom je odgovoril Joábu: »Glej, poslal sem k tebi, rekoč: ›Pridi sèm, da te lahko pošljem h kralju, da rečem: ›Zakaj sem prišel iz Gešurja?‹‹ Zame bi bilo dobro, da bi bil še vedno tam. Sedaj mi torej pusti videti kraljev obraz in če bo kakršnakoli krivičnost v meni, naj me ubije.«
Abisalomu anati kwa Yowabu, “Taona, ine ndinatumiza mawu kwa iwe ndipo ndinati, ‘Bwera kuno kuti ndikutume kwa mfumu kukafunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ine ndinabwera kuchokera ku Gesuri? Zikanakhala bwino ndikanakhala komweko!’ Tsono pano ndikufuna kuonana ndi mfumu, ndipo ngati ndili olakwa mfumuyo indiphe.’”
33 Tako je Joáb prišel h kralju in mu povedal in ko je dal poklicati Absaloma, je ta prišel h kralju in se pred kraljem priklonil na svoj obraz do tal in kralj je poljubil Absaloma.
Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anayiwuza zimenezi. Ndipo mfumu inamuyitanitsa Abisalomu, ndipo analowa nawerama kugunditsa nkhope yake pansi pamaso pa mfumu. Tsono mfumu inapsompsona Abisalomu.