< 2 Kralji 3 >
1 Torej Ahábov sin Jehorám je začel kraljevati nad Izraelom, v Samariji, v osemnajstem letu Judovega kralja Józafata in kraljeval je dvanajst let.
Yoramu mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya mʼchaka cha 18 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda ndipo analamulira zaka khumi ndi ziwiri.
2 Počel je zlo v Gospodovih očeh, toda ne kakor njegov oče in kakor njegova mati, kajti odstranil je Báalovo podobo, ki jo je naredil njegov oče.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova koma sizinafanane ndi zimene anachita abambo ndi amayi ake. Iye anachotsa fano la mwala la Baala limene abambo ake anapanga.
3 Kljub temu se je trdno držal grehov Nebátovega sina Jerobeáma, ki je Izraela pripravil, da greši; ni odšel od njih.
Komabe anawumirira kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli ndipo sanafune kuwaleka.
4 Moábski kralj Meša je bil lastnik ovc in je Izraelovemu kralju dajal sto tisoč jagnjet in sto tisoč ovnov, [skupaj] z volno.
Tsono Mesa, mfumu ya ku Mowabu ankaweta nkhosa, ndipo iye ankayenera kumapereka kwa mfumu ya ku Israeli chaka ndi chaka ana ankhosa onenepa okwanira 100,000 pamodzi ndi ubweya wankhosa 100,000 zazimuna.
5 Toda pripetilo se je, ko je bil Aháb mrtev, da se je moábski kralj uprl zoper Izraelovega kralja.
Koma atamwalira Ahabu, mfumu ya ku Mowabu inawukira mfumu ya ku Israeli.
6 Kralj Jehorám je istočasno odšel iz Samarije in preštel ves Izrael.
Choncho nthawi imeneyi mfumu Yoramu inatuluka mu Samariya ndi kukasonkhanitsa Aisraeli onse.
7 Odšel je in poslal k Judovemu kralju Józafatu, rekoč: »Moábski kralj se je uprl zoper mene. Ali hočeš iti z menoj v bitko zoper Moáb?« Rekel je: »Šel bom gor. Jaz sem, kakor si ti, moje ljudstvo je kakor tvoje ljudstvo in moji konji kakor tvoji konji.«
Yoramu anatumizanso uthenga uwu kwa Yehosafati mfumu ya ku Yuda: “Mfumu ya ku Mowabu yandiwukira. Kodi ungapite nane kukamenyana ndi Mowabu?” Iye anayankha kuti, “Ine ndidzapita nawe. Iwe ndi ine ndife anthu amodzi, anthu anga ali ngati anthu ako, akavalo anga ali ngati akavalo ako.”
8 Rekel je: »Po kateri poti bomo šli gor?« Odgovoril je: »Po poti skozi edómsko divjino.«
Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi tidzera njira iti popita ku nkhondoko?” Yoramu anayankha kuti, “Tidzera ku Chipululu cha Edomu.”
9 Tako so Izraelov kralj, Judov kralj in edómski kralj odšli in zaokrožili sedemdnevno potovanje in tam ni bilo vode za vojsko in živino, ki jim je sledila.
Choncho mfumu ya ku Israeli inanyamuka pamodzi ndi mfumu ya ku Yuda ndi ya ku Edomu. Ndipo atayenda mozungulira mʼchipululu kwa masiku asanu ndi awiri, asilikali analibe madzi woti amwe kapena kumwetsa nyama zawo zosenza katundu.
10 Kralj Izraela je rekel: »Gorje, da je te tri kralje Gospod poklical skupaj, da jih izroči v roko Moába!«
Mfumu inafuwula kuti, “Nʼchiyani chomwe chikutichitikira! Kodi Yehova wasonkhanitsa mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu?”
11 Toda Józafat je rekel: » Mar ni tukaj Gospodovega preroka, da bi po njem lahko poizvedel od Gospoda?« Eden izmed služabnikov Izraelovega kralja je odgovoril in rekel: »Tukaj je Šafátov sin Elizej, ki je izlival vodo na Elijeve roke.«
Koma mfumu Yehosafati inafunsa kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wa Yehova woti tingakafunse kwa Yehova kudzera mwa iyeyo?” Mtsogoleri wa ankhondo wa mfumu ya ku Israeli anayankha kuti, “Alipo, Elisa mwana wa Safati. Iye anali mtumiki wa Eliya.”
12 Józafat je rekel: »Z njim je Gospodova beseda.« Tako so Izraelov kralj, Józafat in edómski kralj odšli dol k njemu.
Yehosafati anati, “Yehova amayankhula kudzera mwa iye.” Choncho mfumu ya ku Israeli pamodzi ndi Yehosafati ndiponso mfumu ya ku Edomu anapita kwa Elisa.
13 Elizej je rekel Izraelovemu kralju: »Kaj imam s teboj? Spravi se k prerokom svojega očeta in k prerokom svoje matere.« Izraelov kralj pa mu je rekel: »Ne, kajti Gospod je te tri kralje sklical skupaj, da jih izroči v roko Moába.«
Elisa ananena kwa mfumu ya ku Israeli kuti, “Pali ubale wanji pakati pa inu ndi ine? Pitani kwa aneneri a abambo ndi amayi anu.” Mfumu ya ku Israeli inayankha kuti, “Ayi, pakuti ndi Yehova amene anatisonkhanitsa ife mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu.”
14 Elizej je rekel: » Kakor živi Gospod nad bojevniki, pred katerim stojim, zagotovo, če se ne bi oziral na prisotnost Judovega kralja Józafata, ne bi pogledal proti tebi niti te ne bi videl.
Elisa anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse amene ndimamutumikira, pakanapanda kuti ndimamuchitira ulemu Yehosafati mfumu ya ku Yuda, sindikanakulabadirani kapena kukuyangʼanani nʼkomwe.
15 Toda sedaj mi privedi glasbenika, ki igra na strune.« In pripetilo se je, ko je glasbenik igral, da je nadenj prišla Gospodova roka.
Koma tsopano ndiyitanireni munthu wodziwa kuyimba bwino zeze.” Munthuyo akuyimba zeze, mphamvu ya Yehova inafika pa Elisa,
16 Rekel je: »Tako govori Gospod: ›To dolino naredite polno jarkov.‹
ndipo anati, “Yehova akuti, ‘Kumbani ngalande mʼchigwa chonse.’
17 Kajti tako govori Gospod: ›Ne boste videli vetra niti ne boste videli dežja, vendar bo ta dolina napolnjena z vodo, da boste lahko pili, tako vi, vaše govedo in vaše živali.‹
Pakuti Yehova akunena kuti, ‘Simudzaona mphepo kapena mvula, komabe chigwa ichi chopanda madzi chidzadzaza ndi madzi, ndipo inu mudzamwa pamodzi ndi ngʼombe zanu ndiponso nyama zanu zonse.’
18 To pa je le majhna stvar v Gospodovih očeh. Tudi Moábce bo izročil v vašo roko.
Izi ndi zosavuta pamaso pa Yehova. Ndipo adzaperekanso Amowabu mʼmanja mwanu.
19 Udarili boste vsako utrjeno mesto in vsako izbrano mesto in posekali vsako dobro drevo in zamašili vse vodnjake in vsak dober kraj dežele oškodovali s kamni.«
Mudzagonjetsa mizinda yawo yonse yotetezedwa ndiponso mizinda yawo ikuluikulu. Mudzagwetsa mtengo wabwino uliwonse, mudzatseka akasupe onse amadzi, ndiponso mudzawononga minda yawo yonse yachonde poponyamo miyala.”
20 Pripetilo se je zjutraj, ko je bila darovana jedilna daritev, glej, da je prišla voda po poti iz Edóma in dežela je bila napolnjena z vodo.
Mmawa mwake, nthawi yopereka nsembe ili pafupi, anangoona madzi akutuluka kuchokera ku Edomu, ndipo malo onse anadzaza ndi madzi.
21 Ko so vsi Moábci slišali, da so prišli gor kralji, da se bojujejo zoper njih, so zbrali vse, ki so si bili zmožni nadeti bojno opremo in starejše in so se razpostavili na meji.
Tsono nʼkuti Amowabu onse atamva kuti mafumu abwera kudzachita nawo nkhondo. Kotero, anayitana munthu aliyense, wamkulu ndi wamngʼono amene ankatha kugwira chida chankhondo ndipo anakayima ku malire a dziko lawo.
22 Vstali so zgodaj zjutraj in sonce je sijalo na vodo in Moábci so vodo na drugi strani videli tako rdečo kakor kri.
Amowabu atadzuka mmamawa, dzuwa likuwala pa madziwo, anaona madziwo akuoneka wofiira ngati magazi patsogolo pawo.
23 Rekli so: »To je kri. Kralji so zagotovo umorjeni in so udarili drug drugega. Sedaj torej Moáb, k plenu.«
Ndipo iwo anati, “Taonani magazi! Mafumu aja amenyana okhaokha ndipo aphana. Amowabu, tsopano ndi nthawi yofunkha!”
24 Ko pa so prišli k taboru Izraelcev, so se Izraelci dvignili in udarili Moábce, tako da so le-ti pred njimi pobegnili. Toda šli so naprej in pobijali Moábce, celo v njihovi deželi.
Koma Amowabu atafika ku misasa ya Israeli, Aisraeli ananyamuka ndi kumenyana nawo mpaka anathawa. Ndipo Aisraeli analowa mʼdzikolo ndi kupha Amowabu.
25 Podirali so mesta in na vsak dober kos dežele je vsak mož vrgel svoj kamen in napolnili so jo in zamašili so vse vodnjake in podrli vsa dobra drevesa, samo v Kir Heresu so pustili njegovo kamenje, vendar so okrog njega šli pračarji in ga udarili.
Aisraeli anagumula mizinda yawo ndipo munthu aliyense anaponya mwala pa munda uliwonse wachonde mpaka utadzaza ndi miyala. Iwo anatseka akasupe onse amadzi ndiponso anadula mtengo wabwino uliwonse. Mzinda wa Kiri Hareseti wokha ndiye unatsala wotetezedwa koma anthu oponya miyala anawuzungulira nawuthiranso nkhondo.
26 Ko je moábski kralj videl, da je bila bitka zanj prehuda, je s seboj vzel sedemsto mož, ki so izdirali meče, da se prebijejo k edómskemu kralju. Toda niso mogli.
Mfumu ya ku Mowabu itaona kuti nkhondo ikumulaka, inatenga anthu 700 a malupanga kuti athawe modutsa mfumu ya ku Edomu, koma inalephera.
27 Potem je vzel svojega najstarejšega sina, ki naj bi zakraljeval namesto njega in ga na obzidju daroval v žgalno daritev. In tam je bilo veliko ogorčenje zoper Izrael in odšli so od njega in se vrnili k svoji lastni deželi.
Choncho inatenga mwana wake wamwamuna woyamba kubadwa, amene akanalowa ufumu mʼmalo mwake, ndi kumupereka nsembe pa khoma la mzinda. Zimenezi zinachititsa kuti mkwiyo ndi ukali wa Amowabu ukule kwambiri pa Aisraeli ndipo Aisraeliwo anathawa nabwerera ku dziko la kwawo.