< 2 Kralji 14 >
1 V drugem letu Jehoáša, Joaházovega sina, Izraelovega kralja, je zakraljeval Amacjá, sin Judovega kralja Joáša.
Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Petindvajset let je bil star, ko je začel kraljevati in v Jeruzalemu je kraljeval devetindvajset let. Ime njegove matere je bilo Joadána iz Jeruzalema.
Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
3 Delal je to, kar je bilo pravilno v Gospodovih očeh, vendar ne tako kakor njegov oče David. Delal je glede na vse stvari, kakor jih je delal njegov oče Joáš.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake.
4 Vendar visoki kraji niso bili odstranjeni. Ljudstvo je na visokih krajih še vedno žrtvovalo in zažigalo kadilo.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 Takoj, ko je bilo kraljestvo v njegovi roki potrjeno, se je pripetilo, da je umoril svoja služabnika, ki sta umorila kralja, njegovega očeta.
Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija.
6 Toda otrok morilcev ni usmrtil, glede na to, kakor je pisano v knjigi Mojzesove postave, v kateri je Gospod zapovedal, rekoč: »Očetje ne bodo usmrčeni zaradi otrok niti ne bodo otroci usmrčeni zaradi očetov, temveč bo vsak človek usmrčen zaradi svojega lastnega greha.«
Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”
7 Izmed Edóma jih je v solni dolini usmrtil deset tisoč in v vojni zavzel Selo in njeno ime imenoval Jokteél do današnjega dne.
Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.
8 Potem je Amacjá poslal poslance k Jehoášu, sinu Joaháza, sinu Jehúja, Izraelovega kralja, rekoč: »Pridite, drug drugemu poglejmo v obraz.«
Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”
9 Izraelov kralj Jehoáš je poslal k Judovemu kralju Amacjáju, rekoč: »Osat, ki je bil na Libanonu, je poslal k cedri, ki je bila na Libanonu, rekoč: ›Daj svojo hčer mojemu sinu za ženo, ‹ pa je tam mimo šla divja zver, ki je bila na Libanonu in pomendrala osat.
Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo.
10 Zares si udaril Edóma in tvoje srce te je povzdignilo. Uživaj v tem in ostani doma, kajti zakaj bi se vmešaval v svojo bolečino, da bi padel ti in Juda s teboj?«
Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
11 Toda Amacjá ni hotel poslušati. Zato je Izraelov kralj Jehoáš odšel gor in on in Judov kralj Amacjá sta si drug drugemu pogledala v obraz pri Bet Šemešu, ki pripada Judu.
Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda.
12 Juda je bil premagan pred Izraelom in pobegnili so vsak mož k svojim šotorom.
Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
13 Izraelov kralj Jehoáš je ujel Judovega kralja Amacjája, sina Joáša, sina Ahazjája, pri Bet Šemešu, prišel v Jeruzalem in porušil jeruzalemsko obzidje od Efrájimskih velikih vrat do Vogalnih velikih vrat, štiristo komolcev.
Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180.
14 Vzel je vse zlato, srebro in vse posode, ki so se našle v Gospodovi hiši, v zakladnicah kraljeve hiše in talce ter se vrnil v Samarijo.
Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.
15 Torej ostala izmed Jehoáševih dejanj, ki jih je storil, njegova moč in kako se je boril z Judovim kraljem Amacjájem, mar niso zapisana v kroniški knjigi Izraelovih kraljev?
Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
16 Jehoáš je zaspal s svojimi očeti in z Izraelovimi kralji je bil pokopan v Samariji in namesto njega je zakraljeval njegov sin Jerobeám.
Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.
17 Judov kralj Amacjá, Joášev sin, je po smrti Jehoáša, Izraelovega kralja, Joaházovega sina, živel petnajst let.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
18 Ostala Amacjájeva dela, mar niso zapisana v kroniški knjigi Judovih kraljev?
Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
19 Torej zoper njega so v Jeruzalemu skovali zaroto in pobegnil je v Lahíš, toda za njim so poslali v Lahíš in ga tam usmrtili.
Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko.
20 Prinesli so ga na konjih in pokopan je bil s svojimi očeti v Jeruzalemu, v Davidovem mestu.
Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.
21 Vse Judovo ljudstvo je vzelo Azarjája, ki je bil star šestnajst let in ga postavilo [za] kralja namesto njegovega očeta Amacjája.
Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya.
22 Zgradil je Elát in ga povrnil Judu, potem je kralj zaspal s svojimi očeti.
Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.
23 V petnajstem letu Judovega kralja Amacjája, Joáševega sina, je v Samariji začel kraljevati Jerobeám, Jehoášev sin, Izraelov kralj in kraljeval je enainštirideset let.
Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41.
24 Počel je to, kar je bilo zlo v Gospodovih očeh. Ni se oddvojil od vseh grehov Nebátovega sina Jerobeáma, ki je Izraela pripravil, da greši.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
25 Povrnil je Izraelovo pokrajino od vstopa v Hamát do morja ravnine, glede na besedo od Gospoda, Izraelovega Boga, ki jo je govoril po roki svojega služabnika Jona, Amitájevega sina, preroka, ki je bil iz Gat Heferja.
Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.
26 Kajti Gospod je videl Izraelovo stisko, da je bila ta zelo grenka, kajti tam ni bilo nobenega zaprtega, niti nobeden ni ostal, niti ni bilo pomočnika za Izrael.
Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli.
27 Gospod ni rekel, da bo Izraelovo ime izbrisal izpod neba, temveč jih je rešil po roki Jehoáševega sina Jerobeáma.
Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.
28 Torej preostala izmed Jerobeámovih dejanj in vse, kar je storil in njegova moč, kako se je bojeval in kako je za Izrael obnovil Damask in Hamát, ki je pripadal Judu, mar niso zapisana v kroniški knjigi Izraelovih kraljev?
Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
29 Jerobeám je zaspal s svojimi očeti, z Izraelovimi kralji in namesto njega je zakraljeval njegov sin Zaharija.
Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.