< 2 Kralji 10 >
1 Aháb je imel v Samariji sedemdeset sinov. Jehú je napisal pisma in jih poslal v Samarijo k vladarjem Jezreéla, k starešinam in tistim, ki so vzgajali Ahábove otroke, rekoč:
Tsono Ahabu anali ndi ana aamuna 70 a ku Samariya. Ndipo Yehu analemba makalata nawatumiza ku Samariya kwa atsogoleri a mu mzinda wa Yezireeli, kwa akuluakulu ndiponso kwa amene ankalera ana a Ahabu, nati,
2 »Torej takoj, ko to pismo pride k vam, glede na to, da so sinovi vašega gospodarja z vami in so tam z vami bojni vozovi in konji, tudi utrjeno mesto in bojna oprema,
“Inu mukangolandira kalatayi, popeza ana a mbuye wanu ali ndi inu ndiponso muli ndi magaleta ndi akavalo, mzinda wotetezedwa ndi zida zankhondo,
3 izberite najboljšega in najprimernejšega izmed sinov svojega gospodarja in ga postavite na prestol njegovega očeta in se borite za hišo svojega gospodarja.«
sankhani mwana wa mbuye wanu amene ndi wooneka bwino ndiponso woyenera, mulowetseni ufumu wa abambo ake. Kenaka muchite nkhondo kuteteza nyumba ya mbuye wanu.”
4 Toda silno so se bali in rekli: »Glej, dva kralja nista obstala pred njim, kako bomo torej obstali mi?«
Koma anthuwo anachita mantha kwambiri ndipo anati, “Taonani, mafumu awiri sanathe kulimbana naye, nanga ife tingathe bwanji?”
5 In ta, ki je bil nad hišo in ta, ki je bil nad mestom, tudi starešine in vzgojitelji otrok, so poslali k Jehúju, rekoč: »Tvoji služabniki smo in storili bomo vse, kar nam boš naročil. Ne bomo postavili nobenega kralja. Stôri to, kar je dobro v tvojih očeh.«
Choncho woyangʼanira nyumba ya mfumu, bwanamkubwa wa mzinda, akuluakulu ena ndiponso olera anawo anatumiza uthenga uwu kwa Yehu: “Ife ndife atumiki anu ndipo tidzachita chilichonse chomwe mutiwuze. Sitidzasankha munthu wina aliyense kukhala mfumu ndipo chitani chimene mukuganiza kuti nʼchabwino kwa inu.”
6 Potem jim je drugič napisal pismo, rekoč: »Če ste moji in če boste prisluhnili mojemu glasu, vzemite glave mož sinov svojega gospodarja in do jutri ob tem času pridite k meni v Jezreél.« Torej kraljevi sinovi, ki jih je bilo sedemdeset oseb, so bili z mestnimi velikaši, ki so jih vzgajali.
Ndipo Yehu anawalembera kalata yachiwiri yonena kuti, “Ngati inu muli mbali yanga ndi kuti mudzandimvera, mudule mitu ya ana a mbuye wanu ndipo mubwere nayo kwa ine ku Yezireeli mawa nthawi ngati yomwe ino.” Tsono ana a mfumu onse 70 anali pamodzi ndi akuluakulu a mu mzindamo, amene ankawalera.
7 Pripetilo se je, ko je pismo prišlo do njih, da so vzeli kraljeve sinove in usmrtili sedemdeset oseb in njihove glave dali v košare in mu jih poslali v Jezreél.
Kalatayo itafika, anthuwo anatenga ana a mfumu 70 aja ndi kuwapha onse. Anayika mitu yawo mʼmadengu ndi kuyitumiza ku Yezireeli kwa Yehu.
8 Tja je prišel poslanec in mu povedal, rekoč: »Prinesli so glave kraljevih sinov.« Rekel je: »Do jutra jih naložite na dva kupa ob vhodu v velika vrata.«
Mthenga uja atafika, anamuwuza Yehu kuti, “Abweretsa mitu ya ana a mfumu.” Ndipo Yehu analamula kuti, “Unjikani mituyo mʼmilu iwiri pa chipata cha mzinda ndipo ikhale pamenepo mpaka mmawa.”
9 Zjutraj se je pripetilo, da je odšel ven, obstal in vsemu ljudstvu rekel: » Bodite pravični. Glejte, koval sem zaroto zoper svojega gospodarja in ga usmrtil, toda kdo je usmrtil vse te?
Mmawa mwake Yehu anatuluka. Iye anayimirira pamaso pa anthu onse ndipo anati, “Inu ndinu osalakwa. Ndine amene ndinachita chiwembu mbuye wanu ndi kumupha, koma kodi wapha anthu onsewa ndani?
10 Vedite torej, da ne bo padlo na zemljo ničesar od Gospodove besede, ki jo je Gospod govoril glede Ahábove hiše, kajti Gospod je storil to, kar je govoril po svojem služabniku Eliju.«
Koma dziwani tsono, kuti mawu amene Yehova anayankhula kunena za banja la Ahabu sadzapita padera. Yehova wachita chimene analonjeza kudzera mwa mtumiki wake Eliya.”
11 Tako je Jehú usmrtil vse, kar je od Ahábove hiše ostalo v Jezreélu, vse njegove velikaše, njegovo žlahto in njegove duhovnike, dokler mu ni preostal niti eden.
Choncho Yehu anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Yezireeli, pamodzinso ndi akuluakulu ake onse, abwenzi ake ndiponso ansembe ake, sanasiyeko ndi mmodzi yemwe wamoyo.
12 Vstal je, odšel in prišel v Samarijo. In ko je bil pri strižni hiši ob poti,
Kenaka Yehu ananyamuka kupita ku Samariya. Atafika pa malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa,
13 se je Jehú srečal z brati Judovega kralja Ahazjája in rekel: »Kdo ste?« Odgovorili so: »Mi smo Ahazjájevi bratje in gremo dol, da pozdravimo kraljeve otroke in otroke kraljice.«
Yehu anakumana ndi abale ena a Ahaziya mfumu ya Yuda nawafunsa kuti, “Kodi ndinu yani?” Iwo anayankha kuti, “Ndife abale ake a Ahaziya, ndipo tabwera kulonjera banja la mfumu ndi ana a mfumukazi.”
14 Rekel je: »Zgrabite jih žive.« Zgrabili so jih žive in jih usmrtili pri jami strižne hiše, celó dvainštirideset mož. Niti ni pustil nobenega izmed njih.
Yehu analamula kuti, “Atengeni amoyo!” Choncho anawatenga amoyo ndipo anakawaphera ku chitsime cha ku malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa; anthu onse 42. Iye sanasiyepo ndi mmodzi yemwe wamoyo.
15 Ko je odpotoval od tam, je naletel na Rehábovega sina Jonadába, ki je prihajal, da se sreča z njim. Pozdravil ga je in mu rekel: »Je tvoje srce iskreno, kakor je moje srce s tvojim srcem?« Jonadáb je odgovoril: »Je.« »Če je tako, mi podaj svojo roko.« Podal mu je svojo roko in vzel ga je gor k sebi na bojni voz.
Yehu atachoka kumeneko anakumana ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu, amene amabwera kudzakumana naye. Yehu anamulonjera nati kwa iye, “Kodi mtima wako uli bwino monga momwe mtima wanga ugwirizana nawo mtima wako?” Yehonadabu anayankha kuti, “Inde ndikugwirizana nawe.” Yehu anati, “Ngati ndi choncho, gwire dzanja.” Ndipo iye anaterodi, ndipo Yehu anamugwira dzanja namulowetsa mʼgaleta lake.
16 Rekel je: »Pridi z menoj in poglej mojo gorečnost za Gospoda.« Tako so ga primorali, da se pelje na njegovem bojnem vozu.
Yehu anati, “Tiye kuno uwone mmene ndikudziperekera kwa Yehova.” Ndipo anayenda naye mʼgaleta mwake.
17 Ko je prišel v Samarijo, je usmrtil vse, ki so Ahábu preostali v Samariji, dokler jih ni uničil, glede na Gospodovo besedo, ki jo je govoril Eliju.
Yehu atafika ku Samariya, anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Samariya; anawawonongeratu potsata mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Eliya.
18 Jehú je vse ljudstvo zbral skupaj in jim rekel: »Aháb je malo služil Báalu, toda Jehú mu bo bolj služil.
Ndipo Yehu anasonkhanitsa anthu onse pamodzi nawawuza kuti, “Ahabu ankatumikira Baala pangʼono chabe; Yehu adzamutumikira kwambiri.
19 Zdaj torej pokličite k meni vse Báalove preroke, vse njegove služabnike in vse njegove duhovnike. Naj nihče ne manjka, kajti imam veliko klavno daritev, da jo opravim Báalu. Kdorkoli bo manjkal, ta ne bo živel.« Toda Jehú je to storil v premetenosti, z namenom, da bi lahko uničil Báalove oboževalce.
Tsopano itanani aneneri a Baala onse, atumiki ake onse ndi ansembe ake onse. Pasapezeke ndi mmodzi yemwe wotsala chifukwa ine ndidzapereka nsembe yayikulu kwa Baala. Aliyense amene alephere kubwera adzaphedwa.” Koma Yehu anachita zimenezi mwachinyengo ndi cholinga choti awononge atumiki onse a Baala.
20 Jehú je rekel: »Razglasite slovesen zbor za Báala.« In to so razglasili.
Yehu anati, “Itanitsani msonkhano wodzalemekeza Baala.” Ndipo analengeza za msonkhanowo.
21 Jehú je poslal po vsem Izraelu in prišli so vsi Báalovi oboževalci, tako da ni ostalo nobenega človeka, ki ne bi prišel. Prišli so v Báalovo hišo in Báalova hiša je bila polna od enega konca do drugega.
Pamenepo Yehu anatumiza mawu ku dziko lonse la Israeli ndipo atumiki onse a Baala anabwera; palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala. Iwo anadzaza nyumba ya Baala. Nyumbayo inadzaziratu kuchokera ku khoma lina mpaka ku khoma lina.
22 Tistemu, ki je bil nad oblačilnico, je rekel: »Prinesi talarje za vse Báalove oboževalce.« In prinesel jim je talarje.
Ndipo Yehu anawuza munthu wosunga mikanjo kuti, “Bweretsa mikanjo yokwanira atumiki onse a Baala.” Ndipo iye anabweretsa mikanjoyo.
23 Jehú in Rehábov sin Jonadáb sta odšla v Báalovo hišo in Báalovim oboževalcem rekla: »Preiščite in poglejte, da ni tukaj z vami kakega Gospodovega služabnika, temveč samo Báalovi oboževalci.«
Kenaka Yehu ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu analowa mʼnyumba ya Baala. Yehu anawawuza atumiki a Baala kuti, “Yangʼanitsitsani ndipo muone kuti muno musapezeke atumiki a Yehova, koma mukhale atumiki okhawo a Baala.”
24 Ko so vstopili, da darujejo klavne daritve in žgalne daritve, je Jehú zunaj določil osemdeset mož in rekel: » Če katerikoli izmed mož, ki sem jih privedel v vaše roke, pobegne, kdor mu pusti oditi, bo njegovo življenje za življenje od tistega.«
Choncho Yehu analowa kukapereka nsembe zina ndi nsembe zopsereza. Nthawi iyi nʼkuti Yehu atayika anthu 80 kunja kwa nyumbayo ndi chenjezo lakuti, “Ngati wina aliyense wa inu adzathawitsa wina aliyense wa anthu amene ndayika kuti muziwayangʼanira, munthu woteroyo adzaphedwa.”
25 Pripetilo se je, takoj ko je končal z darovanjem žgalne daritve, da je Jehú rekel straži in poveljnikom: »Vstopite in jih pobijte; naj nihče ne pride naprej.« In udarili so jih z ostrino meča. Straža in poveljniki so jih vrgli ven in odšli v mesto Báalove hiše.
Yehu atangotsiriza kupereka nsembe yopsereza, analamula alonda ndi akulu a ankhondo kuti, “Lowani ndipo mukawaphe ndipo musalole kuti wina athawe.” Choncho iwo anawapha ndi lupanga. Alonda ndi akulu a ankhondo anaponya mitembo ya anthuwo panja ndipo anakalowa mʼkati mwenimweni mwa nyumba ya Baala.
26 Iz Báalove hiše so prinesli podobe in jih sežgali.
Iwo anakatulutsa mwala wopatulika umene unali mʼnyumba ya Baala ndipo anawutentha.
27 Porušili so Báalovo podobo, zrušili Báalovo hišo in jo naredili za straniščno hišo do današnjega dne.
Anawononga mwala wopatulika wa Baala ndi kugwetsa nyumba ya Baala, ndipo anthu anayisandutsa chimbudzi mpaka lero lino.
28 Tako je Jehú uničil Báala iz Izraela.
Motero Yehu anawononga Baala mu Israeli.
29 Vendar se od grehov Nebátovega sina Jerobeáma, ki je Izraela pripravil, da greši, Jehú ni odvrnil od sledenja za njimi, namreč zlatih telet, ki sta bila v Betelu in v Danu.
Koma Yehuyo sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati amene anachimwitsa nawo Israeli kupembedza mafano a golide a ana angʼombe ku Beteli ndi ku Dani.
30 Gospod je rekel Jehúju: »Ker si storil dobro v izvrševanju tega, kar je pravilno v mojih očeh in si Ahábovi hiši storil glede na vse, kar je bilo na mojem srcu, bodo tvoji otroci četrtega rodu sedeli na Izraelovem prestolu.«
Yehova anati kwa Yehu, “Chifukwa wachita bwino pokwaniritsa kuchita zabwino pamaso panga ndipo wachitira banja la Ahabu zonse zimene zinali mʼmaganizo anga, zidzukulu zako zidzakhala pa mpando waufumu wa Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
31 Toda Jehú ni pazil, da bi se z vsem srcem ravnal po postavi Gospoda, Izraelovega Boga, kajti ni se oddvojil od Jerobeámovih grehov, ki je Izraela pripravil, da greši.
Komatu Yehu sanasamalire kusunga lamulo la Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wake wonse. Iyeyo sanaleke machimo a Yeroboamu amene anachimwitsa nawo Israeli.
32 V tistih dneh je Gospod začel obsekavati Izraela in Hazaél jih je udaril po vseh Izraelovih pokrajinah;
Masiku amenewo Yehova anayamba kuchepetsa dziko la Israeli. Hazaeli anagonjetsa Aisraeli,
33 od Jordana proti vzhodu, vso deželo Gileád, Gádovce, Rubenovce in Manásejce, od Aroêrja, ki je pri reki Arnón, celo Gileád in Bašán.
kuyambira kummawa kwa Yorodani, dziko lonse la Giliyadi (chigawo cha Gadi, Rubeni ndi Manase), kuchokera ku Aroeri pafupi ndi chigwa cha Arinoni kudutsa Giliyadi mpaka ku Basani.
34 Torej preostala izmed Jehújevih dejanj in vse, kar je storil in vsa njegova moč, mar niso zapisana v kroniški knjigi Izraelovih kraljev?
Ntchito zina za Yehu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
35 Jehú je zaspal s svojimi očeti in pokopali so ga v Samariji. Namesto njega je zakraljeval njegov sin Joaház.
Yehu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ku Samariya. Ndipo Yehowahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
36 Časa, ko je Jehú kraljeval nad Izraelom, v Samariji, je bilo osemindvajset let.
Yehu analamulira Aisraeli ku Samariya zaka 28.