< 2 Kroniška 28 >

1 Aház je bil star dvajset let, ko je začel kraljevati in v Jeruzalemu je kraljeval šestnajst let, toda ni delal tega, kar je bilo pravilno v Gospodovih očeh, kakor njegov oče David.
Ahazi anali ndi zaka makumi awiri pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Iye sanachite zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide kholo lake.
2 Kajti hodil je po poteh Izraelovih kraljev in prav tako je naredil ulite podobe za Báale.
Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo anawumbanso mafano a chipembedzo cha Abaala.
3 Poleg tega je zažigal kadilo v dolini Hinómovega sina in svoje otroke sežigal v ognju, po ogabnostih poganov, ki jih je Gospod pregnal pred Izraelovimi otroki.
Iye amapsereza nsembe ku chigwa cha Hinomu, ndipo anaperekanso ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza kutsatira njira zonyansa za mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
4 Tudi daroval je in zažigal kadilo na visokih krajih, na hribih in pod vsakim zelenim drevesom.
Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzerapo mafano, pamwamba pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu.
5 Zato ga je Gospod, njegov Bog, izročil v roko sirskega kralja in udarili so ga in izmed njih odvedli veliko množico ujetnikov in jih privedli v Damask. Izročen je bil tudi v roko Izraelovega kralja, ki ga je udaril z velikim pokolom.
Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu wake anamupereka mʼmanja mwa mfumu ya Aramu. Aaramu anamugonjetsa ndipo anagwira ukapolo anthu ake ambiri napita nawo ku Damasiko. Yehova anamuperekanso mʼmanja mwa mfumu ya Israeli, imene inamuzunza ndi kumuphera anthu ake ambiri.
6 Kajti Remaljájev sin Pékah jih je v Judu v enem dnevu ubil sto dvajset tisoč, ki so bili vsi hrabri možje, ker so zapustili Gospoda, Boga svojih očetov.
Pa tsiku limodzi, Peka mwana wa Remaliya anapha asilikali 120,000 mu Yuda chifukwa Yuda anasiya Yehova, Mulungu wa makolo awo.
7 Zihrí, mogočen mož iz Efrájima, je usmrtil kraljevega sina Maasejája, voditelja hiše Azrikáma in Elkanája, ki je bil poleg kralja.
Zikiri msilikali wa ku Efereimu, anapha Maaseya mwana wa mfumu, Azirikamu woyangʼanira nyumba yaufumu, ndi Elikana wachiwiri kwa mfumu.
8 Izraelovi otroci so odvedli ujetnike izmed njihovih bratov, dvesto tisoč žensk, sinov in hčera ter od njih odvzeli tudi mnogo plena in plen prinesli v Samarijo.
Aisraeli anagwira ukapolo abale awo, akazi, ana aamuna ndi ana aakazi okwanira 200,000. Iwo anafunkhanso katundu wambiri amene anapita naye ku Samariya.
9 Toda tam je bil Gospodov prerok, katerega ime je bilo Odéd in ta je šel ven pred vojsko, ki je prišla do Samarije ter jim rekel: »Glejte, ker je bil Gospod, Bog vaših očetov, besen na Juda, jih je izročil v vašo roko in vi ste jih umorili v besnenju, ki sega do nebes.
Koma kumeneko kunali mneneri wa Yehova dzina lake Odedi, ndipo anapita kukakumana ndi gulu lankhondo pamene linabwerera ku Samariya. Iye anawawuza kuti, “Chifukwa Yehova, Mulungu wa makolo anu anakwiyira Ayuda, Iye anawapereka mʼdzanja lanu. Koma inu mwawapha mwaukali, ukali wake wofika mpaka kumwamba.
10 In sedaj ste se namenili, da obdržite Judove in jeruzalemske otroke, podrejene sebi za sužnje in sužnjice. Toda ali niso z vami, celo z vami, grehi zoper Gospoda, vašega Boga?
Ndipo tsopano mukufuna kuti amuna ndi akazi a ku Yuda ndi ku Yerusalemu akhale akapolo anu.
11 Sedaj me torej poslušajte in ponovno osvobodite ujetnike, ki ste jih zajeli izmed svojih bratov, kajti nad vami je ogorčen Gospodov bes.
Tsono mvereni! Abwezeni abale anu amene mwawagwira ukapolo, pakuti mkwiyo wa Yehova uli pa inu.”
12 Potem so nekateri izmed poglavarjev Efrájimovih otrok, Johanánov sin Azarjá, Mešilemótov sin Berehjá, Šalúmov sin Hizkijá in Hadlájev sin Amasá vstali zoper tiste, ki so prišli iz vojne
Tsono atsogoleri ena a ku Efereimu, Azariya mwana wa Yehohanani, Berekiya mwana wa Mesilemoti, Yehizikiya mwana wa Salumu, ndi Amasa mwana wa Hadilayi anatsutsana nawo amene ankachokera ku nkhondo kuja.
13 ter jim rekli: »Ujetnikov ne boste privedli sèm, kajti kakor smo že grešili zoper Gospoda, ste se vi namenili, da dodate še več k našim grehom in k našemu prestopku, kajti naš prestopek je velik in zoper Izraela je ogorčen bes.
Iwo anati, “Musabweretse akapolowo kuno, pakuti ife tidzakhala olakwa pamaso pa Yehova. Kodi mukufuna kuwonjezera pa machimo athu ndi kulakwa kwathu? Pakuti zolakwa zathu ndi zambiri kale ndipo mkwiyo wake woopsa uli pa Israeli.”
14 Tako so oboroženi možje pustili ujetnike in plen pred princi in pred vso skupnostjo.
Kotero asilikali aja anawasiya akapolowo pamodzi ndi katundu amene analanda ku nkhondo pamaso pa akuluakulu ndi gulu lonse la anthu.
15 Možje, ki so bili določeni po imenu, so vstali, vzeli ujetnike in s plenom oblekli vse, ki so bili med njimi nagi, jih odeli, obuli, jim dali jesti in piti ter jih mazilili in vse slabotne med njimi odvedli na oslih ter jih privedli do Jerihe, mesta palmovih dreves, do njihovih bratov. Potem so se vrnili v Samarijo.
Anthu amene atchulidwa mayina aja anatenga akapolowo, ndipo kuchokera pa zolanda ku nkhondo, anawaveka onse amene anali maliseche. Anawapatsa zovala ndi nsapato, chakudya ndi chakumwa ndi mankhwala. Onse amene anali ofowoka anawakweza pa abulu. Choncho anabwera nawo kwa abale awo ku Yeriko, Mzinda wa Migwalangwa, ndipo kenaka anawabweza ku Samariya.
16 Ob tistem času je kralj Aház poslal k asirskim kraljem, da mu pomagajo.
Pa nthawi imeneyo mfumu Ahazi inatumiza mawu kwa mfumu ya ku Asiriya kupempha chithandizo.
17 Kajti Edómci so ponovno prišli in udarili Juda in odvedli ujetnike.
Ankhondo a ku Edomu anabweranso ndi kuthira nkhondo Yuda ndi kugwira akapolo.
18 Filistejci so vdrli tudi v mesta spodnje dežele in jug Juda in zavzeli Bet Šemeš, Ajalón, Gederót, Sohó in njegove vasi, Timno z njenimi vasmi, tudi Gimzó in njegove vasi in tam prebivali.
Pamenepo nʼkuti Afilisti atathira nkhondo mizinda ya mʼmbali mwa phiri ndi ku Negevi ku Yuda. Iwo analanda mizindayo nakhala ku Beti-Semesi, Ayaloni ndi Gederoti, komanso Soko, Timna ndi Gimizo pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
19 Kajti Gospod je ponižal Juda zaradi Izraelovega kralja Aháza, kajti ta je slekel Juda in se hudo pregrešil zoper Gospoda.
Yehova anapeputsa Yuda chifukwa cha mfumu Ahazi ya Israeli, pakuti analimbikitsa zoyipa ku Yuda ndipo anali munthu wosakhulupirika kwambiri pamaso pa Yehova.
20 K njemu je prišel asirski kralj Tiglát Pilnéser in ga stiskal, toda ni ga okrepil.
Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera kwa iye, ndipo anabweretsa mavuto mʼmalo momuthandiza.
21 Kajti Aház je odvzel delež iz Gospodove hiše in iz kraljeve hiše in od princev in to dal asirskemu kralju, toda ta mu ni pomagal.
Ahazi anatenga zinthu zochokera mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba yaufumu ndi kwa atsogoleri ndipo anazipereka kwa mfumu ya ku Asiriya, koma zimenezo sizinamuthandize.
22 V času svoje stiske je še bolj grešil zoper Gospoda. To je ta kralj Aház.
Pa nthawi yake yamavutoyi mfumu Ahazi inapitirira kukhalabe yosakhulupirika pamaso pa Yehova.
23 Kajti žrtvoval je bogovom Damaska, ki so ga udarili in rekel: »Ker so jim pomagali bogovi sirskih kraljev, zato bom žrtvoval njim, da bi mi lahko pomagali.« Toda oni so bili propad njemu in vsemu Izraelu.
Ahazi ankapereka nsembe kwa milungu ya ku Damasiko, imene inamugonjetsa. Iye ankaganiza kuti, “Popeza milungu ya mafumu a Aaramu yawathandiza, ine ndidzapereka nsembe kwa iyo kuti indithandize.” Koma iyoyo inakhala kugwa kwake ndi kugwa kwa Aisraeli onse.
24 Aház je zbral skupaj posode iz Božje hiše, razbil na koščke posode iz Božje hiše in zaprl vrata Gospodove hiše ter si naredil oltarje na vsakem jeruzalemskem vogalu.
Ahazi anasonkhanitsa pamodzi zinthu zonse kuchokera mʼNyumba ya Mulungu ndipo anazitenga. Iye anatseka zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anayimika maguwa ansembe pa ngodya iliyonse ya msewu mu Yerusalemu.
25 V vsakem posameznem Judovem mestu je postavil visoke kraje, da zažigajo kadilo drugim bogovom in do jeze dražijo Gospoda, Boga svojih očetov.
Mu mzinda uliwonse wa Yuda anamangamo malo achipembedzo, operekerapo nsembe zopsereza kwa milungu ina ndipo anaputa mkwiyo wa Yehova, Mulungu wa makolo ake.
26 Torej ostala njegova dela in vse njegove poti, prve in zadnje, glej, zapisane so v knjigi Judovih in Izraelovih kraljev.
Zochitika zina pa ulamuliro wake ndi machitidwe ake onse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
27 Aház je zaspal s svojimi očeti in pokopali so ga v mestu, torej v Jeruzalemu. Toda niso ga prinesli v mavzoleje Izraelovih kraljev. Namesto njega je zakraljeval njegov sin Ezekíja.
Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mu mzinda wa Yerusalemu, koma sanamuyike mʼmanda a mafumu a Israeli. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Kroniška 28 >