< 1 Samuel 27 >

1 David je v svojem srcu rekel: »Sedaj bom nekega dne umrl po Savlovi roki. Zame ni nič boljšega, kakor da bi hitro pobegnil v deželo Filistejcev in Savel bo obupal nad menoj, da me še išče v kateremkoli območju Izraela. Tako bom pobegnil iz njegove roke.«
Davide anaganiza mu mtima mwake nati, “Tsiku lina ine ndidzaphedwa ndi Sauli. Palibe chabwino ndingachite, koma kuthawira ku dziko la Afilisti. Kotero Sauli adzasiya kundifunafuna mʼdziko lonse la Israeli, ndipo ndidzapulumuka.”
2 David se je dvignil in šel preko s šeststo možmi, ki so bili z njim, k Ahíšu, Maóhovemu sinu, kralju Gata.
Choncho Davide ndi anthu 600 amene anali nawo anachoka napita kwa Akisi mwana wa Maoki mfumu ya ku Gati.
3 David je prebival z Ahíšem v Gatu, on in njegovi možje, vsak mož s svojo družino, David s svojima dvema ženama, Jezreélko Ahinóam in Karmelčanko Abigájilo, Nabálovo ženo.
Davide anakhala ndi Akisi ku Gati pamodzi ndi ankhondo ake, aliyense ndi banja lake. Davide ali ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli wa ku Karimeli, mkazi wamasiye wa Nabala.
4 To je bilo povedano Savlu, da je David pobegnil v Gat in ni ga več ponovno iskal.
Sauli anamva kuti Davide wathawira ku Gati, ndipo sanamufunefunenso.
5 David je rekel Ahíšu: »Če sem torej našel milost v tvojih očeh, naj mi dajo prostor v nekem mestu v deželi, da bom tam lahko prebival, kajti zakaj bi tvoj služabnik prebival s teboj v kraljevem mestu?«
Kenaka Davide anawuza Akisi kuti, “Ngati ndapeza kuyanja pamaso panu mundipatse malo dera limodzi la dziko lanu kuti ndizikhala kumeneko. Mtumiki wanu adzakhala mu mzinda waufumu chifukwa chiyani?”
6 Potem mu je Ahíš ta dan izročil Ciklág. Zato Ciklág pripada Judovim kraljem do tega dne.
Choncho tsiku limenelo Akisi anamupatsa Zikilagi ndipo mzindawo wakhala wa mafumu a Yuda mpaka lero.
7 Časa, ko je David prebival v deželi Filistejcev, je bil polno leto in štiri mesece.
Davide anakhala mʼdziko la Afilisti kwa chaka chimodzi ndi miyezi inayi.
8 David in njegovi možje so odšli gor in vdrli h Gešuréjcem, Girzéjcem in Amalečanom, kajti ti narodi so bili od davnine prebivalci dežele, kakor greš v Šur, celo v egiptovsko deželo.
Tsono Davide ndi anthu ake ankapita kukathira nkhondo Agesuri, Agirizi ndi Aamaleki. (Mitundu ya anthu imeneyi kuyambira kale inkakhala mʼdziko la pakati pa Suri ndi Igupto).
9 David je udaril deželo in ni pustil živega niti moškega niti ženske in odvedel ovce, vole, osle, kamele, obleke in se vrnil in prišel k Ahíšu.
Davide ankati akathira nkhondo dera lina, sankasiya munthu wamoyo, mwamuna kapena mkazi, koma ankatenga nkhosa, ngʼombe, abulu, ngamira ndi zovala, pambuyo pake nʼkubwerera kwa Akisi.
10 Ahíš je rekel: »Kam ste danes vpadli?« David je rekel: »Zoper južni Juda in zoper jug Jerahmeélovcev in zoper jug Kenéjcev.«
Akisi akafunsa kuti, “Kodi lero unapita kukathira nkhondo kuti?” Davide ankayankha kuti, “Ndinapita kukathira nkhondo kummwera kwa Yuda,” mwinanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Ayerahimeeli” kapenanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Akeni.”
11 David ni rešil živega niti moškega niti ženske, da prinesejo novice v Gat, rekoč: »Da ne bi povedali o nas, rekoč: ›Tako je storil David in takšen bo njegov način, vse dokler on prebiva v deželi Filistejcev.‹«
Davide sankasiya mwamuna kapena mkazi wamoyo kuti akafotokozere anthu a ku Gati zochitikazo kuopa kuti opulumukawo akhoza kudzanena kuti “Davide watichita zakutizakuti.” Tsono izi ndi zimene Davide ankachita pamene ankakhala mʼdziko la Afilisti.
12 Ahíš je verjel Davidu, rekoč: »Svojemu ljudstvu Izraelu je storil, da ga popolnoma prezira, zato bo on moj služabnik na veke.«
Akisi ankamukhulupirira Davide ndipo ankati mu mtima mwake, “Davide wadzisandutsa munthu woyipa kwambiri pakati pa anthu ake omwe, Aisraeli. Tsono adzakhala mtumiki wanga mpaka kalekale.”

< 1 Samuel 27 >