< 1 Samuel 15 >
1 Samuel je tudi rekel Savlu: » Gospod me je poslal, da te mazilim, da bi bil kralj nad njegovim ljudstvom, nad Izraelom. Sedaj torej prisluhni glasu Gospodovih besed.
Samueli anawuza Sauli kuti, “Yehova anandituma ine kuti ndikudzozeni kukhala mfumu ya anthu ake, Aisraeli. Tsopano imvani zimene Yehova akunena.
2 Tako govori Gospod nad bojevniki: ›Spomnim se tega, kar je Amálek storil Izraelu, kako je prežal nanj na poti, ko je prišel gor iz Egipta.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzalanga Aamaleki chifukwa cha zimene anawachita Aisraeli. Paja iwo analimbana ndi Aisraeli pa njira pamene Aisraeliwo ankachoka ku Igupto.
3 Sedaj pojdi in udari Amáleka in popolnoma uniči vse, kar imajo in ne prizanesi jim, temveč ubij tako moškega kakor žensko, otroka in dojenčka, vola in ovco, kamelo in osla.‹«
Tsopano pita kathire nkhondo Aamaleki ndi kuwononga kwathunthu zinthu zonse zimene ali nazo. Musakasiyeko munthu ndi mmodzi yemwe. Mukaphe amuna ndi akazi, ana ndi makanda, ngʼombe ndi nkhosa, ngamira ndi abulu.’”
4 Savel je ljudstvo zbral skupaj in jih preštel v Telaímu, dvesto tisoč pešcev in deset tisoč mož iz Juda.
Kotero Sauli anayitana ankhondo ake nawawerenga ku Telaimu. Ankhondo oyenda pansi analipo 200,000 ndipo mwa iwowa 10,000 anali a fuko la Yuda.
5 Savel je prišel do mesta Amálečanov in prežal v dolini.
Sauli anapita ku mzinda wa Aamaleki nawubisalira mʼkhwawa.
6 Savel je Kenéjcem rekel: »Pojdite, odidite dol izmed Amálečanov, da vas ne bi uničil z njimi, kajti izkazali ste prijaznost vsem Izraelovim otrokom, ko so prišli gor iz Egipta.« Tako so Kenéjci odšli izmed Amalečanov.
Tsono Sauli anawuza Akeni kuti, “Samukani, muchoke pakati pa Aamaleki kuti ine ndisakuwonongeni pamodzi ndi iwo pakuti inu munaonetsa kukoma mtima kwa Aisraeli onse pamene ankatuluka mʼdziko la Igupto,” Choncho Akeni anachoka pakati pa Aamaleki.
7 Savel je udaril Amalečane od Havíle, dokler ne prideš do Šura, ki je nasproti Egiptu.
Tsono Sauli anakantha Aamaleki kuchokera ku Havila mpaka ku Suri, kummawa kwa Igupto.
8 Agága, kralja Amalečanov, je zajel živega in z ostrino meča popolnoma uničil vse ljudstvo.
Sauli anatenga Agagi mfumu ya Aamaleki, koma anthu ake onse anawapha ndi lupanga.
9 Toda Savel in ljudstvo je prizaneslo Agágu in najboljšemu od ovc, od volov, od pitancev in jagnjet in vsega, kar je bilo dobro in niso jih želeli popolnoma uničiti. Toda vsako stvar, ki je bila ničvredna in zavrnjena, to so popolnoma uničili.
Koma Sauli ndi ankhondo ake sanaphe Agagi, sanaphenso nkhosa ndi ngʼombe zabwino ngakhalenso ana angʼombe ndi ana ankhosa onenepa. Chilichonse chimene chinali chabwino sanachiphe. Koma zonse zimene zinali zoyipa ndi zachabechabe anaziwononga.
10 Potem je prišla Gospodova beseda Samuelu, rekoč:
Kenaka Yehova anawuza Samueli kuti,
11 »To me je pokesalo, da sem postavil Savla, da bi bil kralj, kajti obrnil se je nazaj od sledenja meni in ni izvršil mojih zapovedi.« To je užalostilo Samuela in ta je vso noč klical h Gospodu.
“Ine ndikumva chisoni chifukwa ndinayika Sauli kukhala mfumu. Wabwerera mʼmbuyo, waleka kunditsata ndipo sanamvere malangizo anga.” Samueli anapsa mtima, ndipo analira kwa Yehova usiku wonse.
12 Ko je Samuel zgodaj vstal, da bi zjutraj srečal Savla, je bilo Samuelu povedano, rekoč: »Savel je prišel v Karmel in glej, postavil si je kraj in potem je šel naokrog, šel naprej in odšel dol do Gilgála.«
Samueli anadzuka mmamawa ndipo anapita kukakumana ndi Sauli. Koma anthu anamuwuza kuti, “Sauli anabwera ku Karimeli, ndipo kumeneko wadziyimikira mwala wachikumbutso cha iye mwini. Tsopano wachokako ndipo wapita ku Giligala.”
13 Samuel je prišel k Savlu in Savel mu je rekel: »Blagoslovljen bodi od Gospoda. Izpolnil sem Gospodovo zapoved.«
Samueli atamupeza Sauli, Sauliyo anati kwa Samueli, “Yehova akudalitseni! Ndachita zonse zimene Yehova analamula.”
14 Samuel pa je rekel: »Kaj potem pomeni to blejanje ovc v mojih ušesih in mukanje volov, ki ga slišim?«
Koma Samueli anati, “Nanga bwanji ndikumva kulira kwa nkhosa ndi ngʼombe?”
15 Savel je rekel: »Privedli so jih od Amalečanov, kajti ljudstvo je prizaneslo najboljšim izmed ovc in izmed volov, da žrtvujejo Gospodu, tvojemu Bogu, preostalo pa smo popolnoma uničili.«
Sauli anayankha, “Zimenezi Asilikali azitenga kuchokera kwa Aamaleki. Iwo anasungako nkhosa ndi ngʼombe zabwino kuti akapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma zina zonse anaziwononga.”
16 Potem je Samuel rekel Savlu: »Ostani in povedal ti bom kaj mi je to noč povedal Gospod.« In rekel mu je: »Povej.«
Koma Samueli anati kwa Sauli, “Khala chete! Ima ndikuwuze zimene Yehova wandiwuza usiku wathawu.” Sauli anayankha kuti, “Ndiwuzeni.”
17 Samuel je rekel: »Ko si bil majhen v svojem lastnem pogledu, ali nisi bil narejen za poglavarja Izraelovim rodovom in te je Gospod mazilil za kralja nad Izraelom?
Apo Samueli anati, “Munali wamngʼono pa maso pa anthu, koma tsopano mwasanduka mtsogoleri wa mafuko a Israeli. Yehova anakudzozani kuti mukhale mfumu yolamulira Aisraeli.
18 Gospod te je poslal na pot in rekel: ›Pojdi in popolnoma uniči grešnike Amalečane in se bori proti njim, dokler ne bodo použiti.‹
Ndipo Yehova anakutumani kuti, ‘Pitani mukawononge kwathunthu Aamaleki, anthu oyipa aja. Mukachite nawo nkhondo mpaka kuwatheratu.’
19 Zakaj potem nisi ubogal Gospodovega glasu, temveč si se vrgel na plen in storil zlo v Gospodovih očeh?«
Chifukwa chiyani simunamvere mawu a Yehova? Chifukwa chiyani munathamangira zofunkha ndi kuchita choyipira Yehova?”
20 Savel je rekel Samuelu: »Da, ubogal sem Gospodov glas in sem šel na pot, na katero me je poslal Gospod in privedel sem Agága, kralja Amalečanov in popolnoma sem uničil Amálečane.
Koma Saulo anawuza Samueli kuti, “Ine ndinamveradi mawu a Yehova. Ndinapita kukachita zimene Yehova anandituma. Ndinabwera naye Agagi, mfumu ya Amaleki, koma Aamaleki ena onse anaphedwa.
21 Toda ljudstvo je vzelo od plena, ovce in vole, glavne izmed stvari, ki naj bi bile popolnoma uničene, da žrtvujejo Gospodu, tvojemu Bogu v Gilgálu.«
Koma pa zofunkhazo anthu anatengapo nkhosa, ngʼombe ndi zabwino zina zoyenera kuwonongedwa kuti akapereke ngati nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ku Giligala.”
22 Samuel je rekel: »Ali ima Gospod tako veliko zadovoljstvo v žgalnih daritvah in klavnih daritvah, kot v ubogljivosti Gospodovemu glasu? Glej, ubogati je bolje kot klavna daritev in poslušati [bolje] kot tolšča ovnov.
Koma Samueli anayankha kuti, “Kodi Yehova amakondwera ndi nsembe zopsereza ndi nsembe zina kapena kumvera mawu a ake? Taona, kumvera ndi kwabwino kuposa nsembe, ndipo kutchera khutu ndi kwabwino kuposa kupereka mafuta a nkhosa.
23 Kajti upor je kakor greh čaranja in trmoglavost je kakor krivičnost in malikovanje. Ker si zavrnil Gospodovo besedo, je tudi on zavrnil tebe, da bi bil kralj.«
Pakuti kuwukira kuli ngati tchimo lowombeza, ndipo kukhala nkhutukumve kuli ngati tchimo lopembedza mafano. Chifukwa mwakana mawu a Yehova. Iyenso wakukana kuti iweyo ukhale mfumu.”
24 Savel je rekel Samuelu: »Grešil sem, kajti prekršil sem Gospodovo zapoved in tvoje besede, ker sem se bal ljudstva in ubogal njihov glas.
Tsono Sauli anati kwa Samueli, “Ine ndachimwa. Ndaphwanya malamulo a Yehova ndiponso malangizo anu. Ndinkaopa anthu ndipo ndinawamvera.
25 Zdaj torej, prosim te, odpusti moj greh in se ponovno obrni z menoj, da lahko obožujem Gospoda.«
Tsopano ndikukupemphani, khululukireni tchimo langa ndipo mubwerere nane kuti ndikapembedze Yehova.”
26 Samuel pa je rekel Savlu: »Ne bom se vrnil s teboj, kajti zavrnil si Gospodovo besedo in Gospod je zavrnil tebe, da bi bil kralj nad Izraelom.«
Koma Samueli anawuza Sauli kuti, “Ine sindibwerera nawe. Inu mwakana mawu a Yehova. Choncho Iyenso wakukanani kuti musakhale mfumu yolamulira Aisraeli.”
27 Medtem ko se je Samuel obrnil naokoli, da gre proč, je zgrabil krajec njegovega plašča in ga odtrgal.
Samueli akutembenuka kuti azipita, Sauli anagwira mpendero wa mkanjo wake, ndipo unangʼambika.
28 Samuel pa mu je rekel: » Gospod je ta dan odtrgal Izraelovo kraljestvo od tebe in ga izročil tvojemu bližnjemu, ki je boljši kakor ti.
Samueli anati kwa iye, “Yehova wangʼamba ufumu wanu kuchoka kwa inu, ndipo waupereka kwa mnzanu woposa inu.
29 Tudi Močni Izraelov ne bo lagal niti se kesal, kajti on ni človek, da bi se kesal.«
Mulungu wa ulemerero wa Israeli sanama kapena kusintha maganizo ake; pakuti iye si munthu, kuti asinthe maganizo ake.”
30 Potem je rekel: »Grešil sem. Vendar me sedaj počasti, prosim te, pred starešinami mojega ljudstva in pred Izraelom in se ponovno obrni z menoj, da bom lahko oboževal Gospoda, tvojega Boga.«
Sauli anati, “Ine ndachimwa. Komabe, chonde mundilemekeze pamaso pa akuluakulu, anthu anga, ndiponso pamaso pa Israeli. Mubwerere nane kuti ndikapembedze Yehova Mulungu wanu.”
31 Tako se je Samuel ponovno obrnil za Savlom, in Savel je oboževal Gospoda.
Pamenepo Samueli anabwerera ndi Sauli, ndipo Sauli anapembedza Yehova.
32 Potem je Samuel rekel: »Privedite sèm k meni Agága, kralja Amalečanov.« Agág je prefinjeno prišel k njemu. In Agág je rekel: »Zagotovo je grenkoba smrti minila.«
Kenaka Samueli anati, “Bwera nayeni kuno Agagi, mfumu ya Amaleki ija.” Choncho Agagi anapita kwa Samueli mokondwa chifukwa ankaganiza kuti, “Ndithu zowawa za imfa zapita.”
33 Samuel je rekel: »Kakor je tvoj meč naredil ženske brez otrok, tako bo tvoja mati brez otroka med ženskami.« In Samuel je Agága razsekal na koščke pred Gospodom v Gilgálu.
Koma Samueli anati, “Monga momwe lupanga lako linasandutsira amayi kukhala wopanda ana, momwemonso amayi ako adzakhala opanda mwana pakati pa amayi.” Ndipo Samueli anapha Agagi pamaso pa Yehova ku Giligala.
34 Potem je Samuel odšel v Ramo, Savel pa je odšel gor, do svoje hiše, v Savlovo Gíbeo.
Ndipo Samueli anapita ku Rama, koma Sauli anapita ku mudzi kwawo ku Gibeya wa Sauli.
35 Samuel ni več prišel, da bi videl Savla, do dneva svoje smrti, vendar je Samuel žaloval za Savlom. In Gospod se je pokesal, da je Savla postavil [za] kralja nad Izraelom.
Samueli sanamuonenso Sauli mpaka imfa yake ngakhale kuti ankamulira Sauliyo. Yehova anamva chisoni kuti anasankha Sauli kuti akhale mfumu ya Israeli.