< Песнь песней Соломона 7 >

1 что украсишася стопы твоя во обутиих твоих, дщи Надавля? Чины бедру твоею подобни усеряземь, делу рук художника:
Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola mu nsapato wavalazo! Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali, ntchito ya manja ya mmisiri waluso.
2 пуп твой чаша источена, не лишаемая мста: чрево твое яко стог пшеницы, огражден в кринах:
Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo. Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu utazunguliridwa ndi maluwa okongola.
3 два сосца твоя, яко два млада близнецы серны:
Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala, ngati mphoyo zamapasa.
4 выя твоя яко столп слоновый: очи твои яко езера во Есевоне, во вратах дщерей многих: нос твой яко столп Ливанский, сматряяй лице Дамаска:
Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu. Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni, amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu. Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni, yoyangʼana ku Damasiko.
5 глава твоя на тебе яко Кармил (гора), и заплетение главы твоея яко багряница, царь увязан в преристаниих.
Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli. Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu; mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.
6 Что украсилася еси, и что усладилася еси, любы, во сладостех твоих?
Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa, iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!
7 Сие величество твое: уподобилася еси финику, и сосца твоя грезном.
Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa, ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.
8 Рекох: взыду на финик, удержу высоту его: и будут сосцы твои яко грезнове винограда, и воня ноздрей твоих яко яблока:
Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa; ndidzathyola zipatso zake.” Mawere ako ali ngati maphava a mphesa, fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,
9 и гортань твой яко вино благо, ходящее брату моему в правость, доволно устнам моим и зубом.
ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri. Mkazi Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga, ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.
10 Аз брату моему, и ко мне обращение его.
Wokondedwayo ine ndine wake, ndipo chilakolako chake chili pa ine.
11 Прииди, брате мой, и взыдем на село, водворимся в селех:
Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi, tikagone ku midzi.
12 ураним в винограды, увидим аще процвете виноград, процветоша ли овощие, процветоша ли яблока? Тамо дам тебе сосца моя.
Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa, tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira, ngati maluwa ake ayamba kuoneka, komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa. Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.
13 Мандрагоры даша воню, и при дверех наших вси плоды новии: до ветхих, брате мой, соблюдох ти.
Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino, ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma, zatsopano ndi zakale zomwe, zimene ndakusungira wokondedwa wanga.

< Песнь песней Соломона 7 >