< Псалтирь 71 >
1 На Тя, Господи, уповах, да не постыжуся в век.
Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
2 Правдою Твоею избави мя и изми мя: приклони ко мне ухо Твое и спаси мя.
Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
3 Буди ми в Бога защитителя и в место крепко спасти мя: яко утверждение мое и прибежище мое еси Ты.
Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
4 Боже мой, избави мя из руки грешнаго, из руки законопреступнаго и обидящаго:
Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
5 яко Ты еси терпение мое, Господи, Господи, упование мое от юности моея.
Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
6 В Тебе утвердихся от утробы, от чрева матере моея Ты еси мой покровитель: о Тебе пение мое выну.
Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
7 Яко чудо бых многим: и Ты помощник мой крепок.
Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
8 Да исполнятся уста моя хваления, яко да воспою славу Твою, весь день великолепие Твое.
Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
9 Не отвержи мене во время старости: внегда оскудевати крепости моей, не остави мене.
Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
10 Яко реша врази мои мне, и стрегущии душу мою совещаша вкупе,
Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
11 глаголюще: Бог оставил есть его, пожените и имите его, яко несть избавляяй.
Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
12 Боже мой, не удалися от мене: Боже мой, в помощь мою вонми.
Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
13 Да постыдятся и изчезнут оклеветающии душу мою, да облекутся в студ и срам ищущии злая мне.
Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
14 Аз же всегда возуповаю на Тя, и приложу на всяку похвалу Твою.
Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
15 Уста моя возвестят правду Твою, весь день спасение Твое, яко не познах книжная.
Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
16 Вниду в силе Господни: Господи, помяну правду Тебе единаго.
Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
17 Боже мой, имже научил мя еси от юности моея, и доныне возвещу чудеса Твоя.
Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
18 И даже до старости и престарения, Боже мой, не остави мене, дондеже возвещу мышцу Твою роду всему грядущему,
Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
19 силу Твою и правду Твою, Боже, даже до вышних, яже сотворил ми еси величия: Боже, кто подобен Тебе?
Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
20 Елики явил ми еси скорби многи и злы? И обращься оживотворил мя еси и от бездн земли возвел мя еси.
Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
21 Умножил еси на мне величествие твое, и обращься утешил мя еси, и от бездн земли паки возвел мя еси.
Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
22 Ибо аз исповемся Тебе в людех, Господи, в сосудех псаломских истину Твою, Боже: воспою Тебе в гуслех, Святый Израилев.
Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
23 Возрадуетеся устне мои, егда воспою Тебе, и душа моя, юже еси избавил:
Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
24 еще же и язык мой весь день поучится правде Твоей, егда постыдятся и посрамятся ищущии злая мне.
Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.