< Псалтирь 50 >
1 Бог Богов Господь глагола, и призва землю от восток солнца до запад.
Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
2 От Сиона благолепие красоты Его:
Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
3 Бог яве приидет, Бог наш, и не премолчит: огнь пред Ним возгорится, и окрест Его буря зелна.
Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
4 Призовет небо свыше, и землю, разсудити люди Своя.
Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
5 Соберите Ему преподобныя Его, завещающыя завет Его о жертвах.
Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
6 И возвестят небеса правду Его: яко Бог судия есть.
Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
7 Услышите, людие Мои, и возглаголю вам, Израилю, и засвидетелствую тебе: Бог, Бог твой есмь Аз.
Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
8 Не о жертвах твоих обличу тя, всесожжения же твоя предо Мною суть выну:
Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
9 не прииму от дому твоего телцев, ниже от стад твоих козлов.
Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
10 Яко Мои суть вси зверие дубравнии, скоти в горах и волове:
pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
11 познах вся птицы небесныя, и красота селная со Мною есть.
Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
12 Аще взалчу, не реку тебе: Моя бо есть вселенная и исполнение ея.
Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
13 Еда ям мяса юнча? Или кровь козлов пию?
Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
14 Пожри Богови жертву хвалы и воздаждь Вышнему молитвы твоя:
“Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
15 и призови Мя в день скорби твоея, и изму тя, и прославиши Мя.
Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
16 Грешнику же рече Бог: вскую ты поведаеши оправдания Моя и восприемлеши завет Мой усты твоими?
Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
17 Ты же возненавидел еси наказание и отвергл еси словеса Моя вспять.
Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
18 Аще видел еси татя, текл еси с ним, и с прелюбодеем участие твое полагал еси:
Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
19 уста твоя умножиша злобу, и язык твой сплеташе льщения:
Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
20 седя на брата твоего клеветал еси и на сына матере твоея полагал еси соблазн.
Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
21 Сия сотворил еси, и умолчах, вознепщевал еси беззаконие, яко буду тебе подобен: обличу тя и представлю пред лицем твоим грехи твоя.
Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
22 Разумейте убо сия, забывающии Бога, да не когда похитит, и не будет избавляяй.
“Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
23 Жертва хвалы прославит Мя, и тамо путь, имже явлю ему спасение Мое.
Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”