< Псалтирь 48 >

1 Псалом песни сынов Кореовых, вторыя субботы. Велий Господь и хвален зело во граде Бога нашего, в горе святей Его,
Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
2 благокоренным радованием всея земли: горы Сионския, ребра северова, град Царя великаго.
Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
3 Бог в тяжестех его знаемь есть, егда заступает и.
Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
4 Яко се, царие земстии собрашася, снидошася вкупе:
Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
5 тии видевше тако, удивишася, смятошася, подвигошася:
iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
6 трепет прият я тамо, болезни яко раждающия.
Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
7 Духом бурным сокрушиши корабли Фарсийския.
Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
8 Якоже слышахом, тако и видехом во граде Господа сил, во граде Бога нашего: Бог основа и в век.
Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
9 Прияхом, Боже, милость Твою посреде людий Твоих.
Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
10 По имени Твоему, Боже, тако и хвала Твоя на концах земли: правды исполнь десница Твоя.
Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
11 Да возвеселится гора Сионская, и да возрадуются дщери Иудейския, судеб ради Твоих, Господи.
Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
12 Обыдите Сион и обымите его, поведите в столпех его:
Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
13 положите сердца ваша в силу его, и разделите домы его, яко да повесте в роде инем.
Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
14 Яко Той есть Бог наш во век и в век века: Той упасет нас во веки.
Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.

< Псалтирь 48 >