< Псалтирь 25 >
1 К Тебе, Господи, воздвигох душу мою, Боже мой, на Тя уповах, да не постыжуся во век, ниже да посмеютмися врази мои:
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 ибо вси терпящии Тя не постыдятся.
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 Да постыдятся беззаконнующии вотще.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Пути Твоя, Господи, скажи ми и стезям Твоим научи мя.
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 Настави мя на истину Твою и научи мя: яко Ты еси Бог спас мой, и Тебе терпех весь день.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Помяни щедроты Твоя, Господи, и милости Твоя, яко от века суть.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 Грех юности моея и неведения моего не помяни: по милости Твоей помяни мя Ты, ради благости Твоея, Господи.
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Благ и прав Господь, сего ради законоположит согрешающым на пути.
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 Наставит кроткия на суд, научит кроткия путем Своим.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 Вси путие Господни милость и истина, взыскающым завета Его и свидения Его.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Ради имене Твоего, Господи, и очести грех мой, мног бо есть.
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 Кто есть человек бояйся Господа? Законоположит ему на пути, егоже изволи.
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 Душа его во благих водворится, и семя его наследит землю.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 Держава Господь боящихся Его, и завет Его явит им.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Очи мои выну ко Господу, яко Той исторгнет от сети нозе мои.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Призри на мя и помилуй мя, яко единород и нищь есмь аз.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 Скорби сердца моего умножишася, от нужд моих изведи мя.
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Виждь смирение мое и труд мой, и остави вся грехи моя.
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Виждь враги моя, яко умножишася, и ненавидением неправедным возненавидеша мя.
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Сохрани душу мою и избави мя, да не постыжуся, яко уповах на Тя.
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Незлобивии и правии прилепляхуся мне, яко потерпех Тя, Господи.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 Избави, Боже, Израиля от всех скорбей его.
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!