< Псалтирь 2 >
1 Вскую шаташася языцы, и людие поучишася тщетным?
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 Предсташа царие земстии, и князи собрашася вкупе на Господа и на Христа Его.
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 Расторгнем узы их и отвержем от нас иго их.
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 Живый на небесех посмеется им, и Господь поругается им.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 Тогда возглаголет к ним гневом Своим и яростию Своею смятет я:
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 Аз же поставлен есмь Царь от Него над Сионом, горою святою Его,
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 возвещаяй повеление Господне. Господь рече ко Мне: Сын Мой еси Ты, Аз днесь родих Тя:
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 проси от Мене, и дам ти языки достояние Твое, и одержание Твое концы земли:
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 упасеши я жезлом железным, яко сосуды скудельничи сокрушиши я.
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 И ныне, царие, разумейте, накажитеся вси судящии земли.
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Работайте Господеви со страхом, и радуйтеся Ему со трепетом.
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 Приимите наказание, да не когда прогневается Господь, и погибнете от пути праведнаго, егда возгорится вскоре ярость Его: блажени вси надеющиися Нань.
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.