< Псалтирь 144 >
1 Благословен Господь Бог мой, научаяй руце мои на ополчение, персты моя на брань.
Salimo la Davide. Atamandike Yehova Thanthwe langa, amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; zala zanga kumenya nkhondo.
2 Милость моя и прибежище мое, заступник мой и Избавитель мой, защититель мой, и на Него уповах: повинуяй люди моя под мя.
Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa, linga langa ndi mpulumutsi wanga, chishango changa mmene ine ndimathawiramo, amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.
3 Господи, что есть человек, яко познался еси ему? Или сын человечь, яко вменяеши его?
Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira, mwana wa munthu kuti muzimuganizira?
4 Человек суете уподобися: дние его яко сень преходят.
Munthu ali ngati mpweya; masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.
5 Господи, преклони небеса, и сниди: коснися горам, и воздымятся:
Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi; khudzani mapiri kuti atulutse utsi.
6 блесни молнию, и разженеши я: посли стрелы Твоя, и смятеши я.
Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani; ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.
7 Посли руку Твою с высоты, изми мя и избави мя от вод многих, из руки сынов чуждих,
Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba; landitseni ndi kundipulumutsa, ku madzi amphamvu, mʼmanja mwa anthu achilendo,
8 ихже уста глаголаша суету, и десница их десница неправды.
amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
9 Боже, песнь нову воспою Тебе, во псалтири десятоструннем пою Тебе:
Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu; ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,
10 дающему спасение царем, избавляющему Давида раба Своего от меча люта.
kwa Iye amene amapambanitsa mafumu, amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.
11 Избави мя и изми мя из руки сынов чуждих, ихже уста глаголаша суету, и десница их десница неправды:
Landitseni ndi kundipulumutsa, mʼmanja mwa anthu achilendo, amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
12 ихже сынове их яко новосаждения водруженая в юности своей, дщери их удобрены, преукрашены яко подобие храма:
Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino, ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.
13 хранилища их исполнена, отрыгающая от сего в сие: овцы их многоплодны, множащыяся во исходищих своих: волове их толсти:
Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza ndi zokolola za mtundu uliwonse. Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda pa mabusa athu.
14 несть падения оплоту, ниже прохода, ниже вопля в стогнах их.
Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera. Sipadzakhala mingʼalu pa makoma, sipadzakhalanso kupita ku ukapolo, mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.
15 Ублажиша люди, имже сия суть: блажени людие, имже Господь Бог их.
Odala anthu amene adzalandira madalitso awa; odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.