< Псалтирь 103 >

1 Благослови, душе моя, Господа, и вся внутренняя моя, имя святое Его:
Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
2 благослови, душе моя, Господа, и не забывай всех воздаяний Его:
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
3 очищающаго вся беззакония твоя, изцеляющаго вся недуги твоя,
Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
4 избавляющаго от истления живот твой, венчающаго тя милостию и щедротами,
amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
5 исполняющаго во благих желание твое: обновится яко орля юность твоя.
amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
6 Творяй милостыни Господь и судбу всем обидимым.
Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
7 Сказа пути Своя Моисеови, сыновом Израилевым хотения Своя.
Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
8 Щедр и милостив Господь, долготерпелив и многомилостив.
Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
9 Не до конца прогневается, ниже во век враждует:
Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
10 не по беззаконием нашым сотворил есть нам, ниже по грехом нашым воздал есть нам.
satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
11 Яко по высоте небесней от земли, утвердил есть Господь милость Свою на боящихся Его:
Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
12 елико отстоят востоцы от запад, удалил есть от нас беззакония наша.
monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
13 Якоже щедрит отец сыны, ущедри Господь боящихся Его.
Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
14 Яко Той позна создание наше, помяну, яко персть есмы.
pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
15 Человек, яко трава дние его, яко цвет селный, тако оцветет:
Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
16 яко дух пройде в нем, и не будет, и не познает ктому места своего.
koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
17 Милость же Господня от века и до века на боящихся Его,
Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
18 и правда Его на сынех сынов, хранящих завет Его и помнящих заповеди Его творити я.
iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
19 Господь на небеси уготова престол Свой, и царство Его всеми обладает.
Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
20 Благословите Господа, вси Ангели Его, сильнии крепостию, творящии слово Его, услышати глас словес Его.
Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
21 Благословите Господа, вся силы Его, слуги Его, творящии волю Его.
Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
22 Благословите Господа, вся дела Его на всяком месте владычества Его: благослови, душе моя, Господа.
Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

< Псалтирь 103 >