< Притчи Соломона 22 >
1 Лучше имя доброе, неже богатство много, паче же сребра и злата благодать благая.
Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
2 Богат и нищь сретоста друг друга, обоих же Господь сотвори.
Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
3 Худог, видев лукаваго мучима крепко, сам наказуется: безумнии же мимошедше отщетишася.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
4 Род премудрости страх Господень, и богатство и слава и живот.
Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
5 Волчцы и сети на путех стропотных, храняй же свою душу избежит их.
Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
6 Богатии убогими имут обладати,
Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
7 и раби своим господем взаим дадут.
Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
8 Сеявый злая пожнет злая, язву же дел своих совершит.
Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
9 Мужа тиха и даятеля любит Господь, суету же дел его скончает.
Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
10 Милуяй нищаго сам препитается: от своих бо хлебов даде убогому. Победу и честь устрояет даяй дары, обаче душу погубляет стяжавших.
Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
11 Изжени от сонмища губителя, и изыдет с ним прение: егда бо сядет в сонмищи, всех безчестит.
Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
12 Любит Господь преподобная сердца, приятни же Ему вси непорочнии в путех своих: устнама пасет царь (люди своя).
Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
13 Очи Господни соблюдают чувство: презирает словеса законопреступный.
Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
14 Вины ищет и глаголет ленивый: лев на стезях, на путех же разбойницы.
Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
15 Яма глубока уста законопреступных: возненавиденый же от Господа впадется в ню. Суть путие злии пред мужем, и не любит возвратитися от них: возвратитися же подобает от пути стропотна и злаго.
Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
16 Безумие висит на сердцы юнаго: жезл же и наказание далече (отгонит) от него.
Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
17 Обидяй убогаго многая себе зла творит, дает же богатому во оскудение (себе).
Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
18 Ко словесем мудрых прилагай твое ухо, и услыши моя словеса: свое же сердце утверди (к ним), да разумееши, яко добра суть.
Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
19 И аще вложиши я в сердце твое, возвеслят тебе купно во твоих устнех.
Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
20 Да будет ти на Господа надежда, и покажет ти путь Свой.
Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
21 Ты же напиши я себе трижды, на совет и смысл и разум, на широте сердца твоего: учу бо тя истинному словеси, и разума благаго слушати на ответы словесем истинным предлагаемым тебе.
malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
22 Не насильствуй нищаго, зане убог есть, и не досаждай немощному во вратех:
Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
23 Господь бо имать судити его суд, и избавиши твою безбедную душу.
pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
24 Не бывай друг мужу гневливу и со другом жестокосердым не соводворяйся:
Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
25 да не когда научишися путем его и приимеши тенета души твоей.
kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
26 Не вдавайся в поручение, стыдяся лица:
Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
27 егда бо не будеши имети чим искупитися, возмут постелю, яже под ребры твоими.
ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
28 Не прелагай предел вечных, яже положиша отцы твои.
Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
29 Прозрителну человеку и острому в делех своих пред царьми подобает стояти, и не стояти пред мужми простыми.
Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.