< Числа 9 >

1 И глагола Господь к Моисею в пустыни Синайстей, во второе лето изшедшым им из земли Египетския, в первый месяц, глаголя:
Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai pa mwezi woyamba wa chaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, nati,
2 рцы да сотворят сынове Израилстии Пасху во время ея,
“Aisraeli azichita Paska pa nthawi yake yoyikika.
3 в четвертыйнадесять день месяца перваго к вечеру, и сотвориши ю во время ея: по закону ея и по уставу ея сотвориши ю.
Muzichita Paska pa nthawi yake yoyikika, madzulo a tsiku la 14 la mwezi uno, potsata malamulo ndi malangizo ake.”
4 И рече Моисей сыном Израилтеским сотворити Пасху.
Choncho Mose anawuza Aisraeli kuti azichita Paska,
5 И сотвориша Пасху, начинающуся первому месяцу в четвертыйнадесять день в пустыни Синайстей: якоже повеле Господь Моисею, тако сотвориша сынове Израилевы.
ndipo anachitadi Paskayo mʼchipululu cha Sinai madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba. Aisraeli anachita zonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
6 И приидоша мужие, иже бяху нечисти о души человечи, и не можаху сотворити Пасхи в той день: и приидоша пред Моисеа и Аарона в той день.
Koma ena a iwo sanathe kuchita nawo Paska pa tsiku limenelo chifukwa anali odetsedwa chifukwa chokhudza mtembo. Choncho anabwera kwa Mose ndi Aaroni tsiku lomwelo,
7 И рекоша мужие Онии к нему: мы нечисти есмы о души человечи: еда убо лишимся принести дар Господу во время свое посреде сынов Израилевых?
ndipo anawuza Moseyo kuti, “Ife tadetsedwa chifukwa cha mtembo wa munthu. Nʼchifukwa chiyani taletsedwa kupereka nsembe kwa Yehova pamodzi ndi Aisraeli ena pa nthawi yake?”
8 И рече Моисей к ним: станите ту, да яслышу, что повелит Господь о вас.
Mose anawayankha kuti, “Dikirani mpaka nditamva zimene Yehova walamula zokhudza Inu.”
9 И рече Господь к Моисею, глаголя:
Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
10 рцы сыном Израилевым, глаголя: человек человек, иже аще будет нечист о души человечи, или на пути далече, или в вас, или в родех ваших, и да сотворит Пасху Господу,
“Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene wina mwa inu kapena zidzukulu zanu adetsedwa chifukwa chokhudza mtembo wa munthu, kapena akakhala pa ulendo, akhoza kuchita nawo Paska ya Yehova.
11 в месяц вторый, в четвертыйнадесять день (месяца) к вечеру да сотворят ю, со опресноки и с горьким зелием да снедят ю:
Azichita chikondwererochi madzulo a pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Azidya mwana wankhosa wamwamuna pamodzi ndi buledi wopanda yisiti ndi ndiwo zowawa zamasamba.
12 да не оставят от нея на утрие, и кости да не сокрушат от нея, по всему закону Пасхи да сотворят ю.
Iwo asasiye nyama ina iliyonse mpaka mmawa. Asaswe mafupa aliwonse. Pamene akuchita chikondwerero cha Paska, atsate malangizo onse.
13 И человек, иже аще чист будет, и на пути далече несть, и оставит сотворити Пасху, потребится душа та от людий своих: яко дара Господви не принесе во время свое, грех свой приимет человек той.
Koma ngati munthu wina ali woyeretsedwa ndipo sali pa ulendo koma alephera kuchita Paska, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake chifukwa sanabweretse chopereka cha Yehova pa nthawi yake. Munthu ameneyo adzalangidwa chifukwa cha tchimo lake.
14 Аще же приидет к вам пришлец в землю вашу и сотворит Пасху Господу, по закону Пасхи и по чину ея, тако сотворит ю: закон един да будет вам и пришелцу и туземцу.
“‘Mlendo amene akukhala pakati panu, nafuna kuchita nawo Paska ya Yehova, achite nawo motsata malamulo ndi malangizo ake. Muzikhala ndi malangizo ofanana a Paska; mbadwa kapena mlendo.’”
15 И в день, в оньже поставися скиния, покры облак скинию и дом свидения: от вечера же бяше над скиниею аки вид огнен до заутрия:
Pa tsiku limene anayimika chihema, tenti ya umboni, mtambo unaphimba chihemacho. Kuyambira madzulo mpaka mmawa, mtambo umene unali pamwamba pa chihemacho unkaoneka ngati moto.
16 тако бываше всегда: облак покрываше ю в день, и вид огнен нощию: ,
Zinkachitika motere mosalekeza: mtambo unkakhala pamwamba pa chihema, ndipo usiku unkaoneka ngati moto.
17 и егда восхождаше облак от скинии, и по сих воздвизахуся сынове Израилтестии: и на месте, на немже стояше облак, тамо ополчахуся сынове Израилевы.
Nthawi ina iliyonse mtambo ukachoka pamwamba pa chihema, Aisraeli ankasamukanso, ndipo paliponse pamene mtambo wayima, Aisraeli ankamangapo misasa.
18 По повелению Господню да ополчаются сынове Израилевы и повелением Господним да воздвизаются: во вся дни, в няже осеняет облак над скиниею, да ополчаются сынове Израилевы:
Aisraeli ankasamuka pamalopo Yehova akawalamula, ndipo ankamanganso misasa Iyeyo akawalamula. Nthawi yonse imene mtambowo wayima pa chihema, ankakhalabe mʼmisasa yawo.
19 и егда премедлит облак над скиниею дни многи, да стрегут сынове Израилтестии стражу Господню и да не воздвижутся:
Mtambowo ukakhala pa chihema nthawi yayitali, Aisraeli ankasungabe lamulo la Yehova ndipo iwo sankasamukanso.
20 и будет егда покрыет облак дни числа над скиниею, глаголголом Господним да ополчаются и повелением Господним да воздвижутся:
Nthawi zina mtambowo unkakhala pa chihemapo masiku owerengeka. Aisraeli ankamanga misasa molamulidwa ndi Yehova ndipo ankasamukanso molamulidwa ndi Iyeyo.
21 и будет егда пребудет облак от вечера до заутрия, и аще воздвигнется облак заутра, да воздвигнутся днем или нощию,
Nthawi zina mtambo unkakhala kuyambira madzulo mpaka mmawa ndipo unkachoka mmawa mwake, ankasamuka. Kaya ndi masana kapena usiku, pamene mtambo wachoka, ankasamuka.
22 и аще воздвигнется облак, да пойдут: или день или месяц дний умножит облак осеняющь над нею, да ополчатся сынове Израилевы, и да не воздвизаются: во отступлении его, воздвизахуся:
Ngakhale mtambo ukhale pa chihema masiku awiri kapena mwezi kapena chaka, Aisraeli ankakhalabe pa msasa osachoka. Koma ukachoka, ankasamuka.
23 яко повелением Господним да ополчаются и повелением Господним да воздвизаются: стражу Господню стрежаху по повелению Господню рукою Моисеовою.
Molamulidwa ndi Yehova ankamanga misasa yawo ndipo ankasamukanso Yehova akawalamula. Ankamvera lamulo la Yehova kudzera mwa Mose.

< Числа 9 >