< Числа 1 >

1 И глагола Господь к Моисею в пустыни Синайстей, в скинии свидения, в первый день месяца втораго, втораго лета изшедшым им от земли Египетския, глаголя:
Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
2 возмите сочтение всего сонма сынов Израилевых по сродством их, по домом отечества их, по числу имен их, по главам их:
“Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
3 всяк мужеск пол от двадесяти лет и вышше, всяк исходяй с силою Израилевою, соглядайте их с силою их, ты и Аарон созирайте их:
Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
4 и с вами да будут с силою своею кийждо, кийждо по племени коегождо от князей, по домом отечеств да будут.
Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
5 И сия имена мужей, иже станут с вами: от Рувима Елисур сын Седиуров,
Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
6 от Симеона Саламиил сын Сурисадаев,
Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
7 от Иуды Наассон сын Аминадавль,
Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
8 от Иссахара Нафанаил сын Согаров,
Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
9 от Завулона Елиав сын Хелонь,
Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
10 от сынов Иосифовых, иже от Ефрема, Елисам сын Семиудов, от Манассии Гамалиил сын Фадассуров,
Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
11 от Вениаминя Авидан сын Гадеониев,
Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
12 от Дана Ахиезер сын Амисадаев,
Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
13 от Асира Фагаиил сын Ехранов,
Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
14 от Гада Елисаф сын Рагуилов,
Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
15 от Неффалима Ахирей сын Енань.
Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
16 Сии нареченнии сонма князи от племен, по отечествам их, тысященачалницы Израилевы суть.
Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
17 И поя Моисей и Аарон мужы сия нареченныя именем.
Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
18 И весь сонм собраша в первый день месяца втораго лета, и соглядаша я по родом их, по отечествам их, по числу имен их, от двадесяти лет и вышше, всяк мужеск пол по главам их,
ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
19 якоже повеле Господь Моисею: и соглядашася сии в пустыни Синайстей.
monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
20 И быша сынове Рувима, первенца Израилева, по сродством их, по сонмом их, по домом отечеств их, по числу имен их, по главам их, всяк мужеск пол от двадесяти лет и вышше, всяк исходяй с силою,
Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
21 соглядание их от племене Рувимля четыредесять шесть тысящ и пять сот.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
22 Сынов Симеоновых по сродством их, по сонмом их, по домом отечеств их, по числу имен их, по главам их, всяк мужеск пол от двадесяти лет и вышше, всяк исходяй с силою,
Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
23 соглядание их от племене Симеоня пятьдесят девять тысящ и триста.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
24 Сынов Иудиных по сродством их, по сонмом их, по домом отечеств их, по числу имен их, по главам их, всяк мужеск пол от двадесяти лет и вышше, всяк исходяй с силою,
Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
25 соглядание их от племене Иудина седмьдесят четыри тысящы и шесть сот.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
26 От сынов Иссахаровых по сродством их, по сонмом их, по домом отечеств их, по числу имен их, по главам их, всяк мужеск пол от двадесяти лет и вышше, всяк исходяй с силою,
Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
27 соглядание их от племене Иссахарова пятьдесят и четыри тысящы и четыре ста.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
28 От сынов Завулоних по сродством их, по сонмом их, по домом отечеств их, по числу имен их, по главам их, всяк мужеск пол от двадесяти лет и вышше, всяк исходяй с силою,
Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
29 соглядание их от племене Завулоня пятьдесят седмь тысящ и четыре ста.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
30 От сынов Иосифовых, сынов Ефремлих по сродством их, по сонмом их, по домом отечеств их, по числу имен их, по главам их, всяк мужеск пол от двадесяти лет и вышше, всяк исходяй с силою,
Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
31 соглядание их от племене Ефремля четыредесять тысящ и пять сот.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
32 От сынов Манассииных по сродством их, по сонмом их, по домом отечеств их, по числу имен их, по главам их, всяк мужеск пол их от двадесяти лет и вышше, всяк исходяй с силою,
Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
33 соглядание их от племене Манассиина тридесять и две тысящи и двести.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
34 От сынов Вениаминовых по сродством их, по сонмом их, по домом отечеств их, по числу имен их, по главам их, всяк мужеск пол их от двадесяти лет и вышше, всяк исходяй с силою,
Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
35 соглядание их от племене Вениаминя тридесять и пять тысящ и четыре ста.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
36 От сынов Гадовых, по сродством их, по сонмом их, по домом отечеств их, по числу имен их, по главам их, всяк мужеский пол их от двадесяти лет и вышше, всяк исходяй с силою,
Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
37 соглядание их от племене Гадова четыредесять пять тысящ и шесть сот пятьдесят.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
38 От сынов Дановых по сродством их, по сонмом их, по домом отечеств их, по числу имен их, по главам их, всяк мужеск пол их от двадесяти лет и вышше, всяк исходяй с силою,
Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
39 соглядание их от племене Данова шестьдесят и две тысящы и седмь сот.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
40 От сынов Асировых по сродством их, по сонмом их, по домом отечеств их, по числу имен их, по главам их, всяк мужеск пол их от двадесяти лет и вышше, всяк исходяй с силою,
Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
41 соглядание их от племене Асирова четыредесять едина тысяща и пять сот.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
42 От сынов Неффалимлих по сродством их, по сонмом их, по домом отечеств их, по числу имен их, по главам их, всяк мужеск пол их от двадесяти лет и вышше, всяк исходяй с силою,
Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
43 соглядание их от племене Неффалимля пятьдесят и три тысящы и четыре ста.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
44 Сие сочисление, еже соглядаша Моисей и Аарон и князи Израилевы, дванадесять мужей, муж един от племене единаго, по племени домов отечества их быша.
Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
45 И бысть всего соглядания сынов Израилевых с силою их, от двадесяти лет и вышше, всяк исходяй ополчатися во Израили,
Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
46 шесть сот тысящ и три тысящы и пять сот и пятьдесят.
Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
47 Левити же от племене отечества их не сочислишася в сынех Израилевых.
Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
48 И рече Господь к Моисею, глаголя:
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
49 виждь, плеюмене Левиина да на сочислиши, и числа их да не приимеши среди сынов Израилевых:
“Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
50 и ты пристави левиты к скинии свидения и ко всем сосудом ея, и ко всем, елика суть в ней: да носят сии скинию и вся сосуды ея, и тии да служат в ней, и окрест скинии да ополчаются:
Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
51 и внегда воздвизати скинию, да снимают ю левити, и внегда поставити скинию, да возставят: и иноплеменник приступаяй да умрет.
Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
52 И да ополчаются сынове Израилевы, всяк в своем чине и всяк по своему старейшинству, с силою своею:
Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
53 левити же да ополчаются сопротив, окрест скинии свидения, и не будет согрешения в сынех Израилевых, и да стрегут левити сами стражу скинии свидения.
Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
54 И сотвориша сынове Израилевы по всем, елика заповеда Господь Моисею и Аарону, тако сотвориша.
Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.

< Числа 1 >