< Книга Неемии 10 >
1 И в печатлеющих быша сии: Неемиа Артасаста сын Ахалиев и Седекиа
Amene anasindikiza chidindo anali awa: Nehemiya, bwanamkubwa uja, mwana wa Hakaliya. Zedekiya,
2 сын Араиев, и Азариа и Иеремиа,
Seraya, Azariya, Yeremiya
Pasuri, Amariya, Malikiya,
4 Аттус, Севаниа, Маллух,
Hatusi, Sebaniya, Maluki,
Harimu, Meremoti, Obadiya,
6 Даниил, Ганафон, Варух,
Danieli, Ginetoni, Baruki,
7 Месуллам, Авиа, Миамин,
Mesulamu, Abiya, Miyamini
8 Маазиа, Велгаи, Самаиа: сии священницы.
Maziya, Biligai ndi Semaya Awa anali ansembe.
9 Левити же: Иисус сын Азариин, Ваней от сынов Инададовых, Кадмиил
Alevi anali awa: Yesuwa mwana wa Azaniya, Binuyi wa fuko la Henadadi, Kadimieli,
10 и братия его Саваниа, Одуиа, Калитан, Фелиа, Анан,
ndi abale awo awa: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,
12 Закхор, Саравиа, Севаниа,
Zakuri, Serebiya, Sebaniya,
14 Началницы людий: Форос, Фааф-Моав, Илам, Зафуиа,
Atsogoleri a anthu anali awa: Parosi, Pahati-Mowabu, Elamu, Zatu, Bani,
15 сынове Ванниины Азгад, Вивай,
Buni, Azigadi, Bebai,
20 Мегафис, Месуллам, Изир,
Magipiyasi, Mesulamu, Heziri
21 Месозевил, Садук, Иеддуа,
Mesezabeli, Zadoki, Yaduwa
Pelatiya, Hanani, Ananiya,
Halohesi, Piliha, Sobeki,
25 Раум, Ессавана, Маасиа
Rehumu, Hasabiya, Maaseya,
Maluki, Harimu ndi Baana.
28 И прочии от людий, священницы, левити, дверницы, певцы, нафиними и всяк приходяй от людий земских ко закону Божию, жены их, сынове их, дщери их, всяк ведяй и разумеяй,
Ife otsalafe, ndiye kuti ansembe, Alevi, alonda a ku Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu, onse amene anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina kuti atsate malamulo a Yehova, pamodzi ndi akazi athu, ana athu ndi onse amene ali ndi nzeru,
29 укрепляхуся над братиею своею, и заклинаша их, и внидоша в клятву и в роту, еже ходити в законе Божии, иже дан есть рукою Моисеа раба Божия, да сотворят и сохранят вся заповеди Господни и судбы Его и повеления Его,
tikuphatikana ndi abale athu wolemekezeka, ndipo tikulonjeza molumbira kuti tidzayenda motsata malamulo a Mulungu amene anapereka kudzera mwa Mose mtumiki wa Mulungu. Tilonjeza kumvera ndi kutsata bwino mawu onse, miyambo yonse ndi malangizo onse a Yehova. Yehova atilange ngati sitidzachita zimenezi.
30 и еже не дати дщерей наших людем земским, и дщерей их не возмем сыновом нашым:
“Ife tikulonjeza kuti sitidzapereka ana athu aakazi kuti akwatiwe ndi amuna a mayiko ena kapena kutenga ana awo aakazi kuti akwatiwe ndi ana athu aamuna.
31 людие же земли носящии продаемая и вся купуемая во дни субботы продавати, не купим от них в субботы, ни в день святый: и оставим лето седмое, и даяние всех рук.
“Ngati anthu a mitundu ina abwera ndi zinthu za malonda, monga tirigu, kudzagulitsa pa tsiku la Sabata, sitidzawagula pa tsiku la Sabata kapena pa tsiku lina lililonse loyera. Pa chaka chilichonse cha chisanu ndi chiwiri tidzagoneka munda wosawulima ndipo tidzafafaniza ngongole zonse.
32 И поставим над нами заповедь даяти нам третию часть дидрахмы на лето, на дело дому Бога нашего,
“Tikulonjezanso molumbira kuti chaka ndi chaka tizipereka magalamu anayi a siliva kuti zithandize ntchito ya ku Nyumba ya Mulungu wathu.
33 на хлебы предложения и на жертвы повседневныя, и во всесожжение присное суббот, новомесячий, в праздники и во святая, и яже о гресех, помолитися за Израиля, и на дела дому Бога нашего.
Ndalamayi izithandiza kulipirira buledi wa pa tebulo, chopereka cha chakudya cha nthawi zonse, zopereka zopsereza za nthawi zonse, zopereka za pa tsiku la Sabata, za pachikondwerero cha Mwezi Watsopano, za pa masiku a chikondwerero osankhika, zopereka za zinthu zopatulika, zopereka za nsembe yopepesera machimo a Aisraeli ndi ntchito ina iliyonse ya ku Nyumba ya Mulungu.
34 И жребий метнухом о ношении древес, священницы и левити и людие, носити в дом Бога нашего, по домом отечеств наших, от времене до времене, от лета до лета возжигати на олтари Господу Богу нашему, якоже писано есть в законе,
“Ife ansembe, Alevi ndi anthu onse, tachita maere kuti tidziwe pamene banja lathu lililonse lidzabweretsa ku nyumba ya Mulungu wathu pa nthawi yoyikika ya chaka zopereka za nkhuni zoyaka pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wathu, monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo.”
35 и приносити первородная земли нашея и первородная плода всякаго древа, от лета до лета, в дом Господень,
“Tilonjezanso kuti tidzabwera ndi zipatso zoyamba kucha za mʼminda yathu ndi zipatso zoyamba kucha za mtengo uliwonse wa zipatso chaka ndi chaka kuti tidzapereke ku Nyumba ya Mulungu wathu.”
36 и первенцы сынов наших и скотов наших, якоже писано есть в законе, и первенцы волов наших и стад наших приносити в дом Бога нашего, священником служащым в дому Бога нашего:
“Tidzabweranso nawo ku Nyumba ya Mulungu, kwa ansembe amene amatumikira ku Nyumba ya Mulungu ana athu aamuna oyamba kubadwa ndi ana angʼombe oyamba kubadwa monga zalembedwera mu Malamulo. Tidzaperekanso ana oyamba kubadwa a ziweto zathu ndi ana ankhosa oyamba kubadwa.”
37 и начатки жит наших и плод всякаго древа, вина и елеа, приносити будем священником в сокровище дому Божия, и десятину земли нашея левитом, и тии левити десятину приемлют во всех градех дел наших.
“Ndiponso ku zipinda za Nyumba ya Mulungu wathu, kwa ansembe tidzaperekanso mtanda wathu wa buledi wa ufa ndi mphatso zina monga zipatso za mtengo uliwonse, vinyo ndi mafuta. Tidzaperekanso kwa alevi chakhumi cha mbewu zathu pakuti alevi ndiwo amasonkhanitsa chakhumi mʼmidzi yathu yonse.
38 Будет же священник сын Ааронов с левиты в десятинах левитов, и левити имут приносити десятую часть десятины в дом Бога нашего в сокровище дому Божия,
Wansembe, mdzukulu wa Aaroni azikhala pamodzi ndi Alevi pamene akulandira chakhumi. Ndipo Alevi azibwera ndi chakhumicho ku nyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda zosungiramo chuma.”
39 яко в сокровища принесут сынове Израилевы и сынове левитстии начатки пшеницы и вина и елеа, и тамо (будут) сосуди святии, и священницы и служителие и дверницы и певцы, и не оставим дому Бога нашего.
Choncho Israeli, kuphatikiza zidzukulu za Alevi, azipititsa zopereka za tirigu, vinyo ndi mafuta ku zipinda zosungiramo katundu wopatulika, komanso kokhala ansembe amene akutumikira pamodzi ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu ndi anthu oyimba nyimbo. “Kwambiri ife sitidzaleka kusamala Nyumba ya Mulungu.”