< От Матфея святое благовествование 26 >
1 И бысть, егда сконча Иисус вся словеса сия, рече учеником Своим:
Yesu atamaliza kuyankhula zonsezi, anati kwa ophunzira ake,
2 весте, яко по двою дню Пасха будет, и Сын Человеческий предан будет на пропятие.
“Monga mukudziwa, kwatsala masiku awiri kuti Paska ifike ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kuti apachikidwe.”
3 Тогда собрашася архиерее и книжницы и старцы людстии во двор архиереов, глаголемаго Каиафы,
Pamenepo akulu a ansembe ndi akuluakulu anasonkhana ku nyumba ya mkulu wa ansembe dzina lake Kayafa,
4 и совещаша, да Иисуса лестию имут и убиют:
ndipo anapangana kuti amugwire Yesu mobisa ndi kumupha.
5 глаголаху же: но не в праздник, да не молва будет в людех.
Ndipo anati, “Osati nthawi yaphwando chifukwa pangabuke chipolowe pakati pa anthu.”
6 Иисусу же бывшу в Вифании, в дому Симона прокаженнаго,
Yesu ali ku Betaniya mʼnyumba Simoni Wakhate,
7 приступи к Нему жена, сткляницу мира имущи многоценнаго, и возливаше на главу Его возлежаща.
mayi wina anabwera kwa Iye ndi botolo la mafuta onunkhira a mtengowapatali, amene anathira pa mutu pake Iye akudya pa tebulo.
8 Видевше же ученицы Его негодоваша, глаголюще: чесо ради гибель сия (бысть)?
Ophunzira ataona izi anayipidwa nafunsa kuti, “Chifukwa chiyani akuwononga chotere?
9 Можаше бо сие миро продано быти на мнозе и датися нищым.
Mafuta amenewa akanatha kugulitsidwa pa mtengo waukulu, ndipo ndalama zake zikanaperekedwa kwa osauka.”
10 Разумев же Иисус рече им: что труждаете жену? Дело бо добро содела о Мне:
Yesu podziwa izi anawawuza kuti, “Chifukwa chiyani mukumuvutitsa mayiyu? Wandichitira Ine chinthu chabwino.
11 всегда бо нищыя имате с собою, Мене же не всегда имате:
Osauka mudzakhala nawo nthawi zonse, koma simudzakhala ndi Ine nthawi zonse.
12 возлиявши бо сия миро сие на тело Мое, на погребение Мя сотвори:
Pamene wathira mafuta onunkhirawa pa thupi langa, wachita izi kukonzekera kuyikidwa kwanga mʼmanda.
13 аминь глаголю вам: идеже аще проповедано будет Евангелие сие во всем мире, речется и еже сотвори сия, в память ея.
Zoonadi, ndikuwuzani kuti kulikonse kumene Uthenga Wabwinowu udzalalikidwa ku dziko lonse lapansi, zimene wachitazi zidzanenedwanso pomukumbukira.”
14 Тогда шед един от обоюнадесяте, глаголемый Иуда Искариотский, ко архиереом,
Pamenepo mmodzi wa khumi ndi awiriwo wotchedwa Yudasi Isikarioti anapita kwa akulu a ansembe
15 рече: что ми хощете дати, и аз вам предам Его? Они же поставиша ему тридесять сребреник:
nafunsa kuti, “Kodi mundipatsa chiyani ngati nditamupereka Iye kwa inu?” Pamenepo anamuwerengera ndalama zokwanira masiliva makumi atatu.
16 и оттоле искаше удобна времене, да Его предаст.
Kuyambira pamenepo Yudasi anafunafuna nthawi yabwino yoti amupereke Yesu.
17 В первый же день опресночный приступиша ученицы ко Иисусу, глаголюще Ему: где хощеши уготоваем Ти ясти пасху?
Pa tsiku loyamba laphwando la buledi wopanda yisiti, ophunzira anabwera kwa Yesu ndi kumufunsa kuti, “Kodi mukufuna tikakonze kuti malo odyera Paska?”
18 Он же рече: идите во град ко онсице, и рцыте ему: Учитель глаголет: время Мое близ есть: у тебе сотворю пасху со ученики Моими.
Iye anayankha kuti, “Pitani mu mzinda kwa munthu wakutiwakuti ndipo kamuwuzeni kuti, ‘Aphunzitsi akuti, nthawi yanga yoyikidwa yayandikira. Ine ndidzadya phwando la Paska ndi ophunzira anga ku nyumba kwako.’”
19 И сотвориша ученицы, якоже повеле им Иисус, и уготоваша пасху.
Pamenepo ophunzira ake anachita monga momwe Yesu anawawuzira ndipo anakonza Paska.
20 Вечеру же бывшу, возлежаше со обеманадесяте ученикома:
Kutada, Yesu ndi ophunzira ake khumi ndi awiriwo anakhala pa tebulo nʼkumadya.
21 и ядущым им, рече: аминь глаголю вам, яко един от вас предаст Мя.
Akudya, Iye anati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mmodzi wa inu adzandipereka.”
22 И скорбяще зело, начаша глаголати Ему един кийждо их: еда аз есмь, Господи?
Iwo anamva chisoni kwambiri ndipo anayamba kuyankhulana naye mmodzimmodzi nati, “Kodi nʼkukhala ine Ambuye?”
23 Он же отвещав рече: омочивый со Мною в солило руку, той Мя предаст:
Yesu anayankha nati, “Iye amene akusunsa mʼmbale pamodzi ndi Ine, yemweyo adzandipereka.
24 Сын убо Человеческий идет, якоже есть писано о Нем: горе же человеку тому, имже Сын Человеческий предастся: добро бы было ему, аще не бы родился человек той.
Mwana wa Munthu adzaphedwa monga mmene kunalembedwera za Iye. Koma tsoka kwa munthu amene apereka Mwana wa Munthu! Kukanakhala bwino kwa iye akanapanda kubadwa.”
25 Отвещав же Иуда предаяй Его, рече: еда аз есмь, Равви? Глагола ему: ты рекл еси.
Ndipo Yudasi amene anamupereka Iye anati, “Monga nʼkukhala ine Aphunzitsi?” Yesu anayankha nati, “Iwe watero.”
26 Ядущым же им, приемь Иисус хлеб и благословив преломи, и даяше учеником, и рече: приимите, ядите: сие есть Тело Мое.
Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, “Tengani, idyani; ili ndi thupi langa.”
27 И приемь чашу и хвалу воздав, даде им, глаголя: пийте от нея вси:
Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo nati, “Imwani nonsenu.
28 сия бо есть Кровь Моя, Новаго Завета, яже за многия изливаема во оставление грехов.
Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri kuti akhululukidwe machimo.
29 Глаголю же вам, яко не имам пити отныне от сего плода лознаго, до дне того, егда е пию с вами ново во Царствии Отца Моего.
Ndikuwuzani kuti sindidzamwanso kuchokera ku chipatso cha mtengo wa mpesa kuyambira lero mpaka tsiku ilo pamene ndidzamwenso mwatsopano ndi inu mu ufumu wa Atate anga.”
30 И воспевше изыдоша в гору Елеонску.
Atayimba nyimbo, anatuluka kupita ku phiri la Olivi.
31 Тогда глагола им Иисус: вси вы соблазнитеся о Мне в нощь сию: писано бо есть: поражу пастыря, и разыдутся овцы стада:
Pamenepo Yesu anawawuza kuti, “Usiku omwe uno inu nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa: “‘Kantha mʼbusa, ndipo nkhosa zidzabalalika.’
32 по воскресении же Моем варяю вы в Галилеи.
Koma ndikadzauka, ndidzatsogola kupita ku Galileya.”
33 Отвещав же Петр рече Ему: аще и вси соблазнятся о Тебе, аз никогдаже соблажнюся.
Petro anayankha nati, “Ngakhale onsewa atakuthawani, ine ndekha ayi.”
34 Рече ему Иисус: аминь глаголю тебе, яко в сию нощь, прежде даже алектор не возгласит, трикраты отвержешися Мене.
Yesu anayankha nati, “Zoonadi, ndikukuwuza kuti usiku omwe uno, asanalire tambala, udzandikana Ine katatu.”
35 Глагола Ему Петр: аще ми есть и умрети с Тобою, не отвергуся Тебе. Такожде и вси ученицы реша.
Koma Petro ananenetsa nati, “Ngakhale kutakhala kufa nanu pamodzi, sindidzakukanani.” Ndipo ophunzira onse ananena chimodzimodzi.
36 Тогда прииде с ними Иисус в весь, нарицаемую Гефсиманиа, и глагола учеником: седите ту, дондеже шед помолюся тамо.
Kenaka Yesu anapita ku malo otchedwa Getsemani, ndipo anawawuza kuti, “Khalani pano pamene Ine ndikukapemphera apo.”
37 И поемь Петра и оба сына Зеведеова, начат скорбети и тужити.
Anatenga Petro ndi ana awiri a Zebedayo, ndipo anayamba kumva chisoni ndi kuvutika mu mtima.
38 Тогда глагола им Иисус: прискорбна есть душа Моя до смерти: пождите зде и бдите со Мною.
Pamenepo anawawuza kuti, “Moyo wanga uli ndi chisoni chofa nacho. Khalani pano ndipo dikirani pamodzi ndi Ine.”
39 И прешед мало, паде на лицы Своем, моляся и глаголя: Отче Мой, аще возможно есть, да мимоидет от Мене чаша сия: обаче не якоже Аз хощу, но якоже Ты.
Atapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi chafufumimba napemphera kuti, “Atate anga, ngati ndikotheka, chikho ichi chichotsedwe kwa Ine. Koma osati monga mmene ndifunira, koma monga mufunira Inu.”
40 И пришед ко учеником, и обрете их спящих, и глагола Петрови: тако ли не возмогосте единаго часа побдети со Мною?
Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nawapeza ali mtulo. Iye anafunsa Petro kuti, “Kodi anthu inu, simukanakhala maso pamodzi ndi Ine kwa ora limodzi lokha?
41 Бдите и молитеся, да не внидете в напасть: дух убо бодр, плоть же немощна.
Khalani maso ndi kupemphera kuti musagwe mʼmayesero. Mzimu ukufuna koma thupi ndi lofowoka.”
42 Паки вторицею шед помолися, глаголя: Отче Мой, аще не может сия чаша мимоити от Мене, аще не пию ея, буди воля Твоя.
Anachokanso nakapemphera kachiwiri kuti, “Atate anga, ngati chikhochi sichingandichoke, mpaka nditamwa, kufuna kwanu kuchitike.”
43 И пришед обрете их паки спящих: беста бо им очи отяготене.
Atabweranso anawapeza ali mtulo chifukwa zikope zawo zinalemedwa ndi tulo.
44 И оставль их, шед паки, помолися третицею, тожде слово рек.
Choncho anawasiya napitanso kukapemphera kachitatu nanenanso chimodzimodzi.
45 Тогда прииде ко учеником Своим и глагола им: спите прочее и почивайте: се, приближися час, и Сын Человеческий предается в руки грешников:
Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nati kwa iwo, “Kodi mukanagonabe ndi kupumula? Taonani, ora layandikira ndipo Mwana wa Munthu akuperekedwa mʼmanja mwa ochimwa.
46 востаните, идем: се, приближися предаяй Мя.
Imirirani, tiyeni tizipita! Wondipereka Ine wafika!”
47 И еще Ему глаголющу, се, Иуда, един от обоюнадесяте, прииде, и с ним народ мног со оружием и дрекольми, от архиерей и старец людских.
Akuyankhula choncho, Yudasi mmodzi mwa khumi ndi awiriwo anafika. Pamodzi ndi iye panali gulu lalikulu la anthu ali ndi mikondo ndi zibonga otumidwa ndi akulu a ansembe ndi akuluakulu.
48 Предаяй же Его даде им знамение, глаголя: Егоже аще лобжу, Той есть: имите Его.
Womuperekayo anawawuziratu chizindikiro anthuwo kuti, “Amene ndidzapsompsona ndi iyeyo; mugwireni.”
49 И абие приступль ко Иисусови, рече: радуйся, Равви. И облобыза Его.
Pamenepo Yudasi anapita kwa Yesu nati, “Moni, Aphunzitsi!” Ndipo anapsompsona Iye.
50 Иисус же рече ему: друже, (твори, ) на неже еси пришел. Тогда приступльше возложиша руце на Иисуса и яша Его.
Yesu anayankha kuti, “Bwenzi langa, chita chimene wabwerera.” Pamenepo anthuwo anabwera patsogolo namugwira Yesu ndi kumumanga.
51 И се, един от сущих со Иисусом, простер руку, извлече нож свой, и удари раба архиереова, и уреза ему ухо.
Pa chifukwa ichi, mmodzi wa anzake a Yesu anagwira lupanga lake, nalisolola ndi kutema wantchito wa mkulu wa ansembe, nadula khutu lake.
52 Тогда глагола ему Иисус: возврати нож твой в место его: вси бо приемшии нож ножем погибнут:
Yesu anati kwa iye, “Bwezera lupanga lako mʼchimake, chifukwa onse amene amapha ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
53 или мнится ти, яко не могу ныне умолити Отца Моего, и представит Ми вящше неже дванадесяте легеона Ангел?
Kodi mukuganiza kuti sindingathe kupempha Atate anga ndipo nthawi yomweyo nʼkundipatsa magulu a angelo oposa khumi ndi awiri?
54 Како убо сбудутся Писания, яко тако подобает быти?
Koma nanga malemba akwaniritsidwa bwanji amene akuti ziyenera kuchitika motere?”
55 В той час рече Иисус народом: яко на разбойника ли изыдосте со оружием и дрекольми яти Мя? По вся дни при вас седех учя в церкви, и не ясте Мене.
Pa nthawi yomweyo Yesu anati kwa gululo, “Kodi ndine mtsogoleri wa anthu owukira kuti mwabwera ndi malupanga ndi zibonga kudzandigwira? Tsiku ndi tsiku ndimakhala mʼNyumba ya Mulungu kuphunzitsa, koma simunandigwire.
56 Се же все бысть, да сбудутся писания пророческая. Тогда ученицы вси оставльше Его бежаша.
Koma zonsezi zachitika kuti zolembedwa ndi aneneri zikwaniritsidwe.” Pamenepo ophunzira anamusiya nathawa.
57 (Воини) же емше Иисуса ведоша к Каиафе архиереови, идеже книжницы и старцы собрашася.
Iwo amene anamugwira Yesu anamutengera kwa Kayafa, mkulu wa ansembe, kumene aphunzitsi amalamulo ndi akuluakulu anasonkhana.
58 Петр же идяше по Нем издалеча до двора архиереова: и вшед внутрь, седяше со слугами, видети кончину.
Koma Petro anamutsatira Iye patali, mpaka ku bwalo la mkulu wa ansembe. Analowa nakhala pansi pamodzi ndi alonda kuti aone zotsatira.
59 Архиерее же и старцы и сонм весь искаху лжесвидетелства на Иисуса, яко да убиют Его,
Akulu a ansembe ndi akulu olamulira Ayuda amafunafuna umboni wonama wofuna kuphera Yesu.
60 и не обретаху: и многим лжесвидетелем приступльшым, не обретоша. Послежде же приступивша два лжесвидетеля,
Koma sanathe kupeza uliwonse, angakhale kuti mboni zambiri zabodza zinapezeka. Pomalizira mboni ziwiri zinabwera patsogolo.
61 реста: Сей рече: могу разорити церковь Божию и треми денми создати ю.
Ndipo zinati, “Munthu uyu anati, ‘Ndikhoza kupasula Nyumba ya Mulungu ndi kuyimanganso mʼmasiku atatu.’”
62 И востав архиерей рече Ему: ничесоже ли отвещаваеши, что сии на Тя свидетелствуют?
Pamenepo mkulu wa ansembe anayimirira nati kwa Yesu, “Kodi suyankha? Kodi umboni umenewu ndi otani umene anthu awa akupereka kukutsutsa Iwe?”
63 Иисус же молчаше. И отвещав архиерей рече Ему: заклинаю Тя Богом живым, да речеши нам, аще Ты еси Христос, Сын Божий?
Koma Yesu anakhalabe chete. Mkulu wa ansembe anati kwa Iye, “Ndikulamulira Iwe ndi lumbiro pamaso pa Mulungu wa Moyo: utiwuze ife ngati ndiwe Khristu Mwana wa Mulungu.”
64 Глагола ему Иисус: ты рекл еси: обаче глаголю вам: отселе узрите Сына Человеческаго седяща одесную силы и грядуща на облацех небесных.
Yesu anayankha nati, “Mwanena ndinu. Koma ndikunena kwa inu nonse: mʼtsogolomo mudzaona Mwana wa Munthu atakhala kudzanja lamanja la Wamphamvuzonse ndipo akubwera ndi mitambo ya kumwamba.”
65 Тогда архиерей растерза ризы своя, глаголя, яко хулу глагола: что еще требуем свидетелей? Се, ныне слышасте хулу Его:
Pamenepo mkulu wa ansembe anangʼamba zovala zake nati, “Wanyoza Mulungu! Tifuniranji mboni zina? Taonani, tsopano mwamva mwano wake.
66 что вам мнится? Они же отвещавше реша: повинен есть смерти.
Mukuganiza bwanji?” Iwo anayankha kuti, “Ayenera kuphedwa!”
67 Тогда заплеваша лице Его и пакости Ему деяху: овии же за ланиту удариша,
Kenaka anamulavulira kumaso namumenya ndi zibakera. Ena anamumenya makofi.
68 глаголюще: прорцы нам, Христе, кто есть ударей Тя?
Ndipo anati, “Tanenera kwa ife, Khristu. Wakumenya ndani?”
69 Петр же вне седяше во дворе. И приступи к нему едина рабыня, глаголющи: и ты был еси со Иисусом Галилейским.
Tsopano Petro anakhala ku bwalo la nyumbayo, ndipo mtsikana wantchito anabwera kwa iye nati, “Iwenso unali ndi Yesu wa ku Galileya.”
70 Он же отвержеся пред всеми, глаголя: не вем, что глаголеши.
Koma iye anakana pamaso pawo nati, “Sindikudziwa chimene ukunena.”
71 Изшедшу же ему ко вратом, узре его другая, и глагола сущым тамо: и сей бе со Иисусом Назореом.
Kenaka anachoka kupita ku khomo la mpanda, kumene mtsikana wina anamuonanso nawuza anthu nati, “Munthu uyu anali ndi Yesu wa ku Nazareti.”
72 И паки отвержеся с клятвою, яко не знаю Человека.
Iye anakananso molumbira kuti, “Sindimudziwa munthuyu!”
73 Помале же приступивше стоящии, реша Петрови: воистинну и ты от них еси, ибо беседа твоя яве тя творит.
Patapita kanthawi pangʼono, amene anayimirira pamenepo anapita kwa Petro nati, “Zoonadi, ndiwe mmodzi wa iwo, popeza mayankhulidwe ako akukuwulula.”
74 Тогда начат ротитися и клятися, яко не знаю Человека. И абие петель возгласи.
Pamenepo anayamba kudzitemberera ndipo analumbira kwa iwo nati, “Sindimudziwa munthu ameneyo!” Nthawi yomweyo tambala analira.
75 И помяну Петр глаголгол Иисусов, реченный ему, яко прежде даже петель не возгласит, трикраты отвержешися Мене. И изшед вон плакася горько.
Ndipo Petro anakumbukira mawu amene Yesu anayankhula kuti, “Tambala asanalire, udzandikana Ine katatu.” Ndipo anatuluka panja nakalira kwambiri.