< Левит 12 >
1 И рече Господь к Моисею, глаголя:
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
2 глаголи сыном Израилевым и речеши к ним, глаголя: жена, яже аще зачнет и родит мужеск пол, нечиста будет седмь дний: по днем (естественнаго) разлучения скверны ея, нечиста будет:
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Mkazi akakhala woyembekezera, nabala mwana wa mwamuna, mkaziyo adzakhala wodetsedwa kwa masiku asanu ndi awiri, ngati pa masiku ake akusamba.
3 и в день осмый да обрежет плоть конечную его:
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, mwanayo achite mdulidwe.
4 и сидети будет тридесять и три дни в крови нечистей своей: всякой вещи святей да не прикоснется и в святилище да не внидет, дондеже скончаются дние очищения ея.
Mkaziyo adikire masiku ena 33 kuti ayeretsedwe ku matenda ake. Asakhudze kanthu kalikonse koyera kapena kulowa mʼmalo wopatulika mpaka masiku a kuyeretsedwa kwake atatha.
5 Аще же женск пол родит, и нечиста будет четыренадесять дний по (естественней) скверне ея, и шестьдесят и шесть дний сидети будет в крови нечистоты своея.
Ngati abala mwana wamkazi, adzakhala wodetsedwa kwa masabata awiri, monga zikhalira pa nthawi yake yosamba. Ndipo mkaziyo adikire masiku ena 66, kuti ayeretsedwe ku matenda akewo.
6 И егда исполнятся дние очищения ея о сыне ея или дщери, да принесет агнца непорочна единолетна во всесожжение, и птенца голубина или горлицу греха ради, пред двери скинии свидения к жерцу,
“‘Masiku ake wodziyeretsa akatha, kaya ndi a mwana wamwamuna kapena a mwana wamkazi, abwere kwa wansembe ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi pa khomo la tenti ya msonkhano kuti ikhale nsembe yopsereza. Abwerenso ndi chiwunda cha nkhunda kapena njiwa kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
7 и да принесет е пред Господа: и помолится о ней жрец и очистит ю от тока крове ея: сей закон раждающия мужеск пол или женск.
Wansembeyo apereke zimenezi pamaso pa Yehova pochita mwambo wopepesera mkaziyo. Ndipo mkaziyo adzakhala woyeretsedwa ku msambo wake. “‘Amenewa ndiwo malamulo a mkazi amene wabala mwana wamwamuna kapena wamkazi.
8 Аще же не обрящет рука ея доволнаго на агнца, и да возмет две горлицы или два птенца голубина, единаго на всесожжение и другаго греха ради: и помолится о ней жрец, и очистится.
Ngati mkaziyo sangathe kupeza mwana wankhosa, abwere ndi njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri: imodzi ikhale ya nsembe yopsereza ndipo inayo ikhale ya nsembe yopepesera machimo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera wa mkaziyo ndipo adzayeretsedwa.’”