< Книга Иисуса Навина 9 >

1 Егда же услышаша вси царие Аморрейстии, иже об ону страну Иордана, иже в горней и иже в равней, и иже во всем примории моря великаго и иже при Антиливане, и Хеттеи и Аморреи, и Гергесеи и Хананеи, и Ферезеи и Евеи и Иевусеи,
Mafumu onse okhala kumadzulo kwa Yorodani atamva zimenezi pamodzi ndi mafumu okhala ku mayiko a ku mapiri, mu zigwa, mʼmbali mwa Nyanja yayikulu mpaka ku Lebanoni (mafumu a Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi, ndi Ayebusi),
2 снидошася вкупе сещися со Иисусом и со Израилем единомысленно.
anapangana kuti achite nkhondo ndi Yoswa ndi Israeli.
3 И живущии в холме в Гаваоне слышаша вся, елика сотвори Господь Иерихону и Гаю,
Koma Ahivi ena a ku Gibiyoni atamva zomwe Yoswa anachitira mizinda ya Yeriko ndi Ai,
4 и сотвориша и сии с лукавством, и шедше уготоваша брашна и уготовашася: и вземше вретища ветха на ослы своя, и мехи вина ветхи и разседшыяся завязаны:
anaganiza zochita zachinyengo. Anapita nasenzetsa abulu awo chakudya mʼmatumba akalekale ndiponso matumba a vinyo achikopa ongʼambikangʼambika.
5 и сапоги ветхи и заплачены на ногу их, и ризы обветшаны на них, и хлебы брашна их беша пресохли и сплеснели и сдроблени.
Anthuwa anavala nsapato zakutha ndi zazigamba ndiponso anavala sanza. Buledi wawo yense anali wowuma ndi wowola.
6 И приидоша ко Иисусу в полк Израилев в Галгалы, и рекоша ко Иисусу и всему Израилю: от земли дальния приидохом, и ныне завещайте нам завет.
Ndipo anapita kwa Yoswa ku msasa ku Giligala ndikumuwuza kuti, pamodzi ndi Aisraeli onse, “Ife tachokera ku dziko lakutali, ndipo tikufuna kuti muchite mgwirizano ndi ife.”
7 И рекоша сынове Израилевы к Хоррею: виждь, не посреде ли нас живеши, и како тебе завещаю завет?
Koma Aisraeli anayankha Ahiviwo kuti, “Mwinatu inu mukukhala pafupi ndi ife. Tsono ife tingachite bwanji mgwirizano ndi inu?”
8 И рекоша ко Иисусу: раби есмы твои. И рече к ним Иисус: откуду есте? И откуду приидосте?
Iwo anati kwa Yoswa, “Ife ndife akapolo anu.” Tsono Yoswa anawafunsa kuti, “Inu ndinu yani ndipo mukuchokera kuti?”
9 И рекоша к нему: от дальния земли зело приидохом раби твои во имя Господа Бога твоего: слышахом бо имя Его и вся, елика сотвори во Египте,
Iwo anayankha kuti, “Akapolo anufe tachokera ku dziko lakutali chifukwa tamva za Yehova Mulungu wanu. Tamva mbiri yonse ya zimene Iye anachita ku Igupto,
10 и вся, елика сотвори двоим царем Аморрейским, иже быша об ону страну Иордана, Сиону царю Есевонску и Огу царю Васанску, иже живяше во Астарофе и во Едраине.
ndi zonse zimene anachita kwa mafumu awiri a Aamori kummawa kwa Yorodani, mfumu Sihoni ya Hesiboni ndi Ogi mfumu ya Basani amene amalamulira ku Asiteroti.
11 И слышавше рекоша к нам старцы наши и вси живущии на земли нашей, глаголюще: возмите себе брашно на путь и идите противу им, и рцыте к ним: раби есмы ваши, и ныне завещайте нам завет:
Tsono akuluakulu athu ndi onse amene akukhala mʼdziko lathu anati kwa ife. Tengani chakudya cha pa ulendo wanu. Pitani mukakumane nawo ndipo mukati kwa iwo, ‘Ife ndife akapolo anu, ndipo tikufuna kuti mugwirizane nafe za mtendere.’”
12 сии хлебы наши, теплыя на путь взяхом их от домов наших, в оньже день изыдохом приити к вам: ныне же пресхоша и быша содроблени:
Buledi wathuyu anali wotentha pamene timanyamuka ku mudzi kubwera kwa inu. Koma tsopano taonani ali gwaa ndiponso wawola.
13 и сии меси вина, ихже налияхом новы, и сии разседошася: и ризы нашя сия и обувища наша обетшаша от долгаго пути зело.
Zikopa zimene tinathiramo vinyozi zinali zatsopano, koma taonani zathetheka. Zovala zathu ndi nsapato zathu zatha chifukwa cha kutalika kwa ulendo.
14 И взяша князи брашно их, а Господа не вопросиша.
Aisraeli anatengako chakudya chawo koma sanafunse kwa Yehova.
15 И сотвори Иисус с ними мир, и устави к ним завет, еже снабдети их: и кляшася им князи сонма.
Choncho Yoswa anapangana nawo za mtendere kuti sadzawapha, ndipo atsogoleri a gulu anavomereza pochita lumbiro.
16 И бысть по триех днех по завещании к ним завета, услышаша, яко близ их суть и яко посреде их живут.
Patatha masiku atatu atachita mgwirizano wa mtendere ndi Agibiyoni, Aisraeli anamva kuti anali anansi awo, anthu amene amakhala nawo pafupi.
17 И восташа сынове Израилевы и внидоша во грады их в третий день: гради же их (бяху) Гаваон и Кефира, и Вирот и град Иарим.
Tsono Aisraeli ananyamuka ulendo ndipo tsiku lachitatu anafika ku mizinda ya Gibiyoni, Kefira, Beeroti ndi Kiriati-Yearimu.
18 И не сотвориша с ними рати (Иисус и) сынове Израилевы, яко кляшася им вси князи сонма Господем Богом Израилевым. И ропташа весь сонм Израилев на князей.
Koma Aisraeli sanawaphe anthuwo chifukwa atsogoleri awo anali atalonjeza mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli za Agibiyoniwo. Koma anthu onse anatsutsana ndi atsogoleriwo.
19 И рекоша вси князи всему сонму: мы кляхомся им Господем Богом Израилевым, и ныне не возможем коснутися их:
Koma atsogoleriwo anayankha kuti, “Ife tinawalonjeza mʼdzina la Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo tsopano sitingawaphe.
20 сие сотворим им, еже живити их, и снабдим их, и не будет на нас гнева клятвы ради, еюже кляхомся им.
Chimene tidzachita nawo ndi ichi: Tidzawasiya akhale ndi moyo kuti mkwiyo wa Yehova usatigwere chifukwa chophwanya lonjezo limene tinawalonjeza.”
21 И рекоша им князи: да живут сии, и будут древосечцы и водоносцы всему сонму. И сотвори весь сонм, якоже рекоша им князи.
Anapitiriza kunena kuti “Asiyeni akhale ndi moyo, komabe akhale otidulira mitengo ndi kutitungira madzi ogwiritsa ntchito pa chipembedzo.” Lonjezo la atsogoleriwo linasungidwa.
22 И созва их Иисус и рече им, глаголя: почто прельстисте мя, глаголюще: далече есмы от тебе зело? Вы же населницы есте от живущих в нас:
Kenaka Yoswa anayitanitsa Agibiyoni aja nawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani inu munatinyenga ponena kuti mumachokera kutali pamene zoona zake nʼzoti mumakhala pafupi pomwe pano?
23 и ныне прокляти есте: и не оскудеет от вас раб, ниже древосечец, ниже водоносец мне и Богу моему.
Tsopano popeza mwachita izi, Mulungu wakutembererani ndipo palibe wina mwa inu amene akhale mfulu. Nthawi zonse inu muzidzatidulira nkhuni ndi kutitungira madzi ku Nyumba ya Yehova.”
24 И отвещаша Иисусу, глаголюще: понеже возвестися нам (рабом твоим), елика заповеда Господь Бог твой Моисею рабу Своему, дати вам землю сию и потребити нас и вся живущыя на ней от лица вашего, сего ради убояхомся зело от душах наших от лица вашего, и сотворихом дело сие:
Iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife akapolo anufe tinachita zimenezi chifukwa tinamva bwino lomwe kuti Yehova Mulungu wanu analamula Mose mtumiki wake kuti adzakupatsani dziko lonseli ndi kuti anthu onse okhalamo adzaphedwe. Tsono ife tinachita mantha aakulu ndipo tinachita zimenezi pofuna kupulumutsa miyoyo yathu.
25 и ныне, се, мы подручни вам, якоже угодно есть вам, и якоже вам мнится, творите нам.
Tsopanotu ife tili mʼmanja mwanu, ndipo inu chitani nafe monga kukukomerani.”
26 И сотвориша им сице: и избави я Иисус в той день от руку сынов Израилевых, и не убиша их.
Tsono Yoswa anawapulumutsa mʼmanja mwa Aisraeli ndipo sanawaphe.
27 И постави я Иисус в той день древосечцы и водоносцы всему сонму и олтарю Божию. Сего ради быша живущии в Гаваоне древосечцы и водоносцы олтарю Божию, даже до днешняго дне, и на месте еже аще изберет Господь.
Kuyambira tsiku limenelo Agibiyoni aja anasanduka odula nkhuni zaguwa lansembe la Yehova ndiponso otunga madzi. Mpaka lero lino iwo akuchitabe zimenezi kulikonse kumene Yehova anasankha.

< Книга Иисуса Навина 9 >