< Книга Иисуса Навина 5 >
1 И бысть егда услышаша царие Аморрейстии, иже бяху об ону страну Иордана, и царие Финическии, иже бяху близ моря, яко изсуши Господь Бог Иордан реку пред сыны Израилевыми, внегда преходити им, и истаяша мысли их, и ужасошася, и не бяше в них смышления ни единаго от лица сынов Израилевых.
Mafumu onse a Aamori, a kummawa kwa Yorodani ndi mafumu onse a Akanaani a mʼmbali mwa Nyanja anamva momwe Yehova anawumitsira Yorodani pamene Aisraeli ankawoloka. Choncho anachita mantha ndi kutayiratu mtima chifukwa cha Aisraeliwo.
2 В сие же время рече Господь Иисусу: сотвори себе ножи каменны от камене остраго, и сед обрежи сыны Израилевы второе.
Tsono Yehova anati kwa Yoswa, “Panga mipeni ya miyala ndipo uchitenso mwambo wa mdulidwe pa Aisraeli.”
3 И сотвори Иисус себе ножи каменны остры и обреза сыны Израилевы на месте нареченнем Холм обрезания.
Choncho Yoswa anapanga mipeni ya miyala ndi kuchita mdulidwe Aisraeli ku Gibeyati Haaraloti.
4 И тако обреза Иисус сыны Израилевы: елицы тогда родишася на пути, и елицы тогда не обрезани быша от изшедших из Египта, всех сих обреза Иисус: вси людие изшедшии из Египта мужеска полу, вси мужие ратнии измроша в пустыни на пути, внегда изыдоша из Египта:
Chifukwa chimene Yoswa anachitira izi ndi ichi: Onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto, amuna onse amene anali oyenera kumenya nkhondo anatha kufa mʼchipululu atatuluka mʼdziko la Igupto.
5 яко обрезани быша вси людие изшедшии, вси же людие, иже родишася в пустыни на пути, егда изыдоша из Египта, не обрезани быша:
Anthu onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto anali atachita mwambo wa mdulidwe, koma onse amene anabadwira mʼchipululu, pa ulendo wochoka ku Igupto, sanachite.
6 четыредесять бо и два лета хождаше Израиль в пустыни Мавдаритиде: сего ради не обрезани быша мнози от тех воинов изшедших из земли Египетския, не послушавшии заповедий Господних, имже и определи Господь не видети земли, еюже клятся Господь отцем их дати нам землю кипящую медом и млеком:
Aisraeli anakhala akuyenda mʼchipululu kwa zaka makumi anayi mpaka amuna onse amene potuluka mʼdziko la Igupto anali a msinkhu woyenera kupita ku nkhondo anamwalira. Iwo anafa chifukwa sanamvere mawu a Yehova. Yehova anawalumbirira kuti sadzalowa konse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi limene analonjeza kwa makolo awo kuti adzatipatsa.
7 вместо же сих постави сыны их, ихже обреза Иисус, яко скончаныя плоти бяху им, яко родишася на пути не обрезани:
Koma ana awo amene analowa mʼmalo mwawo ndiwo amene Yoswa anawachita mdulidwe popeza sanachite pamene anali pa ulendo wawo mʼchipululu muja.
8 обрезавшеся же покой имяху тамо седяще в полце, дондеже исцелишася.
Atamaliza kuchita mdulidwe uja, anthu onse anakakhala ku misasa yawo kudikira kuti zilonda zipole.
9 И рече Господь Иисусу: в днешний день отях поношение Египетско от вас. И нарече имя месту тому Галгала, даже до сего дне.
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Kuyambira tsopano anthu a ku Igupto sadzakunyozaninso.” Nʼchifukwa chake malowa anatchedwa Giligala mpaka lero.
10 И ополчишася сынове Израилевы в Галгалех и сотвориша Пасху в четвертыйнадесять день месяца от вечера на западе на поли Иерихонстем,
Akupumulabe ku Giligala kuja mʼchigwa cha Yeriko, Aisraeli anachita chikondwerero cha Paska madzulo pa tsiku la 14 la mwezi woyamba womwewo.
11 и ядоша от пшеницы земли оноя опресноки и новая:
Mmawa mwake ndi pamene anayamba kudya zakudya za mʼdziko la Kanaani. Anaphika buledi wopanda yisiti ndi kukazinga tirigu tsiku lomwelo.
12 в той день преста манна, повнегда ядоша от пшеницы земли, и ктому не бысть сыном Израилевым манны: но ядоша от плодов земли Финическия в лето оное.
Atangodya chakudya cha mʼdzikomo, mana anasiya kugwa, ndipo sanapezekenso. Kuyambira nthawi imeneyo Aisraeli anayamba kudya chakudya cha mʼdziko la Kanaani.
13 И бысть егда бяше Иисус у Иерихона, и воззрев очима своима, виде человека стояща пред ним, и мечь его обнажен в руце его. И приступив Иисус, рече ему: наш ли еси, или от сопостат наших?
Tsiku lina pamene Yoswa anali pafupi ndi Yeriko, anakweza maso ake ndipo mwadzidzidzi anaona munthu atayima patsogolo pake ndi lupanga losolola mʼdzanja lake. Yoswa anapita pamene panali munthuyo ndipo anamufunsa kuti, “Kodi uli mbali yathu kapena ya adani athu?”
14 Он же рече ему: аз архистратиг силы Господни, ныне приидох (семо). И Иисус паде лицем своим на землю и поклонися ему, и рече: господи, что повелеваеши рабу твоему?
Iye anayankha kuti “Sindili mbali iliyonse. Ndabwera monga mkulu wa asilikali a Yehova.” Pomwepo Yoswa anadzigwetsa chafufumimba kupereka ulemu, ndipo anamufunsa, “Kodi mbuye wanga muli ndi uthenga wotani kwa mtumiki wanu?”
15 И рече архистратиг Господень ко Иисусу: иззуй сапог с ногу твоею: место бо, на немже ты стоиши, свято есть. И сотвори Иисус тако.
Mkulu wa asilikali a Yehova uja anayankha kuti, “Vula nsapato zako, pakuti wayima pa malo wopatulika.” Ndipo Yoswa anachitadi zimene anawuzidwazo.