< Книга Иисуса Навина 4 >
1 И егда скончаша вси людие преходяще Иордан, и рече Господь к Иисусу, глаголя:
Anthu onse atatha kuwoloka Yorodani, Yehova anati kwa Yoswa,
2 поими дванадесять мужей от людий, мужа единаго от коегождо племене,
“Sankha amuna khumi ndi awiri, mmodzi pa fuko lililonse.
3 повели им, глаголя: возмите от среды Иордана, идеже стояша нози жречестии, готовых дванадесять каменей, и изнесше я с собою, положите в полце вашем, идеже станете тамо в нощи.
Tsono uwalamule kuti, ‘Tengani miyala khumi ndi iwiri pakati penipeni pa mtsinje wa Yorodani, pamalo pamene ansembe anayimirirapo. Miyalayo muwoloke nayo ndi kudzayitula pamalo pamene mukagone usiku uno.’”
4 И призвав Иисус дванадесять мужей славных от сынов Израилевых, единаго от коегождо племене, рече им:
Choncho Yoswa anayitana amuna khumi ndi awiri amene anawasankha aja kuchokera pakati pa Aisraeli, mmodzi pa fuko lililonse,
5 идите предо мною пред лицем Господним в средину Иордана: и взем оттуду кийждо камень един да возложит на рамена своя, по числу племен (сынов) Израилевых:
ndipo anawawuza kuti, “Lowani pakati pa mtsinje wa Yorodani, patsogolo pa Bokosi la Yehova Mulungu wanu. Ndipo aliyense wa inu atenge mwala pa phewa lake, monga mwa chiwerengero cha mafuko a Aisraeli,
6 да будут вам сии в знамение посреде вас лежаще всегда, да егда вопросит тебе утро сын твой, глаголя: что суть камение сие вам?
kuti ikhale chizindikiro kwa inu. Mʼtsogolo muno ana anu akamadzakufunsani kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
7 И ты возвестиши сыну твоему, глаголя: яко оскуде Иордан река от лица кивота завета Господа всея земли, егда прехождаше его, и изсяче вода Иорданова: и будут вам камение сие в память сынов Израилевых даже до века.
Muzidzawawuza kuti, ‘Madzi a Yorodani analeka kuyenda pamene Bokosi la Chipangano la Yehova linkawoloka mtsinjewo. Miyala iyi idzakhala chikumbutso kwa anthu a Israeli kwa muyaya.’”
8 И сотвориша тако сынове Израилевы, якоже заповеда Господь Иисусу: и вземше дванадесять каменей от среды Иордана, якоже заповеда Господь Иисусу в скончании прехождения сынов Израилевых, и принесоша их с собою в полк, и положиша их тамо.
Aisraeli anachitadi monga Yoswa anawalamulira. Iwo ananyamula miyala khumi ndi iwiri kuchokera pakati pa Yorodani, fuko lililonse la Israeli mwala wake, monga Yehova analamulira Yoswa. Miyalayo anapita nayo ku misasa yawo nakayikhazika kumeneko.
9 Постави же Иисус и другия дванадесять каменей в самем Иордане на месте, идеже стояху нози жерцев воздвизающих кивот завета Господня, и суть тамо даже до сего дне.
Yoswa anayimika miyala khumi ndi iwiri imene inali pakati pa Yorodani pamalo pamene ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anayimapo. Ndipo miyalayo ili pamalo pomwepo mpaka lero lino.
10 Стояху же жерцы воздвизающии кивот завета Господня во Иордане, дондеже сконча Иисус вся, елика заповеда Господь Иисусу поведати людем, по всем, елика заповеда Моисей Иисусу: и потщашася людие, и преидоша.
Ansembe onyamula Bokosi lija anayimirirabe pakati pa Yorodani mpaka zonse zimene Yehova analamulira Yoswa kuti awuze anthu zinatha. Zimenezi zinali monga momwe Mose anamufotokozera Yoswa. Tsono anthu anawoloka mtsinjewo mofulumira.
11 И бысть егда скончаша вси людие преходити (Иордан), прейде и кивот завета Господня, и камение пред ними.
Anthu atatha kuwoloka, ansembe anatsogolera anthuwo atanyamula Bokosi la Yehova.
12 И преидоша сынове Рувимли и сынове Гадовы и пол племене Манассиина устроены пред сынми Израилевы, якоже заповеда им Моисей:
Anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawoloka patsogolo pa Aisraeli ali ndi zida, monga momwe Mose anawalamulira.
13 четыредесять тысящ вооружени на рать преидоша пред Господем на брань ко граду Иерихону.
Asilikali pafupifupi 40,000 anawoloka napita kukayima mʼchigwa cha Yeriko kukonzekera nkhondo.
14 В той день возвеличи Господь Иисуса пред всем родом Израилевым: и бояхуся его, якоже бояхуся Моисеа, елико время поживе.
Zimene Yehova anachita tsiku limeneli zinapatsa anthu mtima wolemekeza Yoswa. Ndipo anamulemekeza masiku onse a moyo wake, monga momwe analemekezera Mose.
15 И рече Господь ко Иисусу, глаголя:
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa,
16 заповеждь жерцем, воздвизающым кивот завета свидения, изступити из Иордана.
“Lamula ansembe onyamula Bokosi la Chipanganowo kuti atuluke mu Yorodani.”
17 И заповеда Иисус жерцем, глаголя: изыдите из Иордана.
Choncho Yoswa anawalamuladi ansembe aja kuti atuluke mu Yorodani muja.
18 И бысть егда изыдоша жерцы воздвизающии кивот завета Господня от среды Иордана, и поставиша ноги на сусе, и устремися вода Иорданова на место и пойде якоже вчера и третияго дне по всему краю.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova aja atangotuluka mu mtsinje muja nʼkuponda powuma, madzi a mu Yorodani anayambanso kuyenda ngati poyamba mpaka kumasefukira.
19 И людие взыдоша от Иордана в десятый день перваго месяца: и ополчишася сынове Израилевы в Галгалех на стране, яже на восток солнца от Иерихона.
Aisraeli anawoloka Yorodani tsiku lakhumi la mwezi woyamba ndipo anakamanga misasa yawo ku Giligala mbali ya kummawa kwa Yeriko.
20 И дванадесять камения сия, яже взя от Иордана, постави Иисус в Галгалех, и рече к сыном Израилевым, глаголя:
Ku Giligala, Yoswa anayimikako miyala khumi ndi iwiri imene anayitenga mu Yorodani ija.
21 егда вопросят вас сынове ваши, глаголюще: что суть камение сие?
Ndipo iye anati kwa Aisraeli, “Mʼtsogolo muno pamene adzukulu anu adzafunsa makolo awo kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
22 Возвестите сыном вашым: яко по суху прейде Израиль Иордан сей,
Muzidzawawuza kuti, ‘Aisraeli anawoloka Yorodani pansi pali powuma.’
23 изсушившу Господу Богу вашему воду Иорданю пред ними, дондеже преидоша, якоже сотвори Господь Бог ваш Чермному морю, еже изсуши Господь Бог ваш пред вами, дондеже преидохом:
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye anawumitsa Yorodani pamaso panu mpaka inu mutawoloka. Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yorodani monga mmene anachitira ndi Nyanja Yofiira mpaka ife tinawoloka powuma.
24 да уведят вси языцы земнии, яко рука Господня крепка есть, и вы да чтете Господа Бога вашего во всякое время.
Iye anachita zimenezi kuti anthu onse pa dziko lapansi adziwe kuti dzanja la Yehova ndi lamphamvu, ndi kuti inu muziopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.”