< Книга Иисуса Навина 13 >
1 Иисус же состареся прошед дни. И рече Господь ко Иисусу: ты состарелся еси денми, и земля остася многа в наследие:
Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
2 и сия земля оставшаяся: пределы Филистимли, Гесури и Хананей,
“Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
3 от Необитаемыя, яже от лица Египта даже до предел Аккаронских ошуюю Хананеов, причисляется пятим областем Филистимским: Газеу и Азотию, и Аскалониту и Гетфею, и Аккарониту и Евею:
kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
4 от Феман и всей земли Ханаанстей прямо Газе, и Сидонии даже до Афека, даже до предел Аморрейских:
Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
5 и всю землю Гавли Филистимлю, и весь Ливан от восток солнца, от Галгал под горою Аермон даже до входа Емаф:
Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
6 всяк обитающий в горней от Ливана даже до Масрефофмаима, всех Сидонян Аз потреблю от лица Израилева: но раздай ю во жребий Израилю, якоже заповедах тебе:
“Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
7 и ныне раздели землю сию в наследие девяти племеном и полплемени Манассиину от Иордана даже до моря великаго, к западу солнца даси ю: море великое предел будет.
Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
8 Дву же племеном и полуплемени Манассиину, Рувиму и Гаду, даде Моисей об ону страну Иордана: к востоком солнца даде им Моисей раб Господень,
Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
9 от Ароира, иже есть на устии водотечи Арнони, и град иже посреде дебри, и весь Мисор от Медавана:
Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
10 вся грады Сиона царя Аморрейска, иже царствова во Есевоне, даже до предел сынов Аммоних:
Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
11 и Галаад, и пределы Гесури, и Махафи, всю гору Аермон, и всю Васанитску до Елхи:
Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
12 все царство Огово в Васанитиде, иже царствова во Астарофе и во Едраине: сей остася (един) от Исполинов, и уби его Моисей, и потреби.
Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
13 И не потребиша сынове Израилевы Гесура и Махафа и Хананеа: и живяше царь Гесури и Махафи в сынех Израилевых даже до сего дне.
Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
14 Токмо племени Левиину не дадеся наследие: Господь Бог Израилев, сам наследие их, якоже рече им Господь. И сие разделение, еже раздели Моисей сыном Израилевым (по племеном их) во Аравофе Моавли об ону страну Иордана противу Иерихона.
Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
15 И даде Моисей племени сынов Рувимлих по сонмом их:
Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
16 и быша им пределы от Ароира, иже есть прямо дебри Арнонския, и град, иже есть в дебри Арнонстей,
Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
17 и всю землю Мисорску даже до Есевона, и вся грады иже суть в мисоре, и Девор, и Вамоф-Ваал, и домы Веелмони,
Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
18 и Иасса и Кедимофа и Мифааф,
Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
19 и Кариафем и Севама, и Сарф и Сиор на горе Енак,
Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
20 и Веффогор и Асидоф-Фасга и Вифсимуф,
Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
21 и вся грады Мисорски, и все царство Сиона царя Аморрейска, егоже уби Моисей самаго, и старейшины Мадиамли, и Евиа и Рокома, и Сура и Ура и ровека, князи Сиорския, и живущих на земли (той):
Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
22 и Валаама сына Веорова волхва убиша мечем сынове Израилевы в сражении.
Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
23 Быша же пределы Рувимли, Иордан предел. Сие наследие сынов Рувимлих по сонмом их, грады их и села их.
Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
24 Даде же Моисей сыном Гадовым по сонмом их,
Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
25 и быша им пределы Иазир: вси гради Галаади и полземли сынов Аммоних до Ароира, иже есть пред лицем Раввафа:
Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
26 и от Есевона до Рамофа к Масфе, и Вотаниму, и Манаиму до предел Давировых,
ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
27 и во емеке Вифарам и Вифнамра, и Сохоф и Сафон, и прочее царство Сиона царя Есевонска: и Иордан определяет даже до страны моря Хенереф, об ону страну Иордана от восток.
Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
28 Сие наследие сынов Гадовых по сонмом их и по градом их и селам их.
Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
29 И даде Моисей полуплемени Манассиину по сонмом их,
Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
30 и быша пределы их от Манаима, и все царство Васанско, и все царство Ога царя Васанска, и вся веси Иаира, яже суть в Васанитиде, шестьдесят градов:
Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
31 и пол Галаада, и во Астарофе, и во Едраине, грады царства Огова в Васанитиде: и дашася сыном Махировым, сыном Манассииным, и половине сынов Махировых по сонмом их.
Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
32 Сии суть, имже даде наследие Моисей об ону страну Иордана во Аравофе Моавли, прямо Иерихона на востоки.
Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
33 Племени же Левиину не даде Моисей наследия: понеже Сам Господь Бог Израилев наследие Его есть, якоже глагола им.
Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.