< От Иоанна святое благовествование 16 >
1 Сия глаголах вам, да не соблазнитеся.
“Ine ndakuwuzani zonsezi kuti musadzakhumudwe.
2 От сонмищ ижденут вы: но приидет час, да всяк, иже убиет вы, возмнится службу приносити Богу:
Iwo adzakuchotsani mʼsunagoge mwawo. Kunena zoona, nthawi ikubwera imene aliyense amene adzakuphani adzaganiza kuti akutumikira Mulungu.
3 и сия сотворят, яко не познаша Отца, ни Мене.
Iwo adzachita zoterozo chifukwa sanadziwe Atate kapena Inenso.
4 Но сия глаголах вам, да, егда приидет час, воспомянете сия, яко Аз рех вам: сих же вам исперва не рех, яко с вами бех.
Ine ndakuwuzani izi kuti nthawi ikadzafika mudzakumbukire kuti Ine ndinakuchenjezani kale. Ine sindinakuwuzeni izi poyamba paja chifukwa ndinali nanu.”
5 Ныне же иду к Пославшему Мя, и никтоже от вас вопрошает Мене: камо идеши?
“Tsopano Ine ndikupita kwa Iye amene anandituma koma palibe wina mwa inu akundifunsa kuti, ‘Kodi mukupita kuti?’
6 Но яко сия глаголах вам, скорби исполних сердца ваша.
Muli ndi chisoni kwambiri chifukwa ndakuwuzani zimene.
7 Но Аз истину вам глаголю: уне есть вам, да Аз иду: аще бо не иду Аз, Утешитель не приидет к вам: аще (ли) же иду, послю Его к вам,
Komatu ndakuwuzani zoona. Ine ndikuti kuli bwino kwa inu kuti ndichoke. Ngati sindichoka, Nkhosweyo sidzabwera kwa inu, koma ngati Ine ndipita, ndidzamutumiza kwa inu.
8 и пришед Он обличит мир о гресе и о правде и о суде:
Iye akabwera, adzatsutsa dziko lapansi za uchimo, zachilungamo ndi zachiweruzo.
9 о гресе убо, яко не веруют в Мя:
Za uchimo, chifukwa anthu sakhulupirira Ine.
10 о правде же, яко ко Отцу Моему иду, и ктому не видите Мене:
Za chilungamo, chifukwa Ine ndi kupita kwa Atate, kumene simudzandionanso.
11 о суде же, яко князь мира сего осужден бысть.
Za chiweruzo, chifukwa wolamulira dziko lino lapansi waweruzidwa tsopano.
12 Еще много имам глаголати вам, но не можете носити ныне:
“Ine ndili ndi zambiri zoti ndiyankhule nanu, koma simungathe kuzilandira tsopano.
13 егда же приидет Он, Дух истины, наставит вы на всяку истину: не от Себе бо глаголати имать, но елика аще услышит, глаголати имать, и грядущая возвестит вам:
Koma pamene Iye, Mzimu wachoonadi, abwera, adzakutsogolerani mʼchoonadi chonse. Iye sadzayankhula mwa Iye yekha, adzayankhula zokhazo zimene wamva ndipo Iye adzakuwuzani zimene zikubwera.
14 Он Мя прославит, яко от Моего приимет и возвестит вам.
Iye adzalemekeza Ine chifukwa adzatenga za Ine nadzakudziwitsani.
15 Вся, елика имать Отец, Моя суть: сего ради рех, яко от Моего приимет и возвестит вам.
Zonse za Atate ndi zanga. Ichi nʼchifukwa chake Ine ndanena kuti Mzimu Woyera adzatenga kwa Ine zanga kuti muzidziwe.”
16 Вмале, и (ктому) не видите Мене: и паки вмале, и узрите Мя, яко иду ко Отцу.
Yesu anapitiriza kuyankhula kuti, “Mwa kanthawi kochepa, simudzandionanso, ndipo patatha nthawi pangʼono mudzandionanso.”
17 Реша же от ученик Его к себе: что есть сие, еже глаголет нам: вмале, и не видите Мене: и паки вмале, и узрите Мя: и: яко Аз иду ко Отцу?
Ena a ophunzira ake anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi Iye akutanthauza chiyani ponena kuti, ‘Mwa kanthawi kochepa, simudzandionanso,’ ndi ‘ndipo patatha nthawi pangʼono mudzandionanso,’ ndiponso ‘chifukwa ndikupita kwa Atate?’”
18 Глаголаху убо: что сие есть, еже глаголет: вмале? Не вемы, что глаголет.
Iwo anapitiriza kufunsana kuti, “Kodi akutanthauza chiyani, ‘kanthawi kochepa?’ Ife sitikumvetsetsa chimene Iye akuyankhula.”
19 Разуме же Иисус, яко хотяху Его вопрошати, и рече им: о сем ли стязаетеся между собою, яко рех: вмале, и не видите Мене: и паки вмале, и узрите Мя?
Yesu anadziwa kuti ankafuna kuti amufunse za zimenezi, choncho anawafunsa kuti, “Kodi mukufunsana wina ndi mnzake chimene Ine ndimatanthauza pamene ndinati, ‘Mwa kanthawi kochepa simudzandionanso,’ ndi ‘patatha nthawi pangʼono mudzandionanso?’
20 Аминь, аминь глаголю вам, яко восплачетеся и возрыдаете вы, а мир возрадуется: вы же печальни будете, но печаль ваша в радость будет:
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti inu mudzalira ndi kubuma pomwe dziko lapansi lidzakhale likukondwera. Inu mudzamva chisoni, koma chisoni chanu chidzasandulika chimwemwe.
21 жена егда раждает, скорбь имать, яко прииде год ея: егда же родит отроча, ктому не помнит скорби за радость, яко родися человек в мир:
Mayi akamabereka mwana amamva ululu chifukwa nthawi yake yafika; koma mwana wake akabadwa amayiwala ululu wake chifukwa cha chimwemwe chake chakuti mwana wabadwa mʼdziko lapansi.
22 и вы же печаль имате убо ныне: паки же узрю вы, и возрадуется сердце ваше, и радости вашея никтоже возмет от вас:
Chimodzimodzinso ndi inu. Tsopano ino ndi nthawi yanu yomva chisoni, koma Ine ndidzakuonaninso ndipo inu mudzasangalala, ndipo palibe amene adzachotsa chimwemwe chanu.
23 и в той день Мене не воспросите ничесоже. Аминь, аминь глаголю вам, яко елика аще (чесо) просите от Отца во имя Мое, даст вам:
Tsiku limenelo inu simudzandipemphanso kalikonse. Ine ndikukuwuzani zoona kuti Atate anga adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa.
24 доселе не просисте ничесоже во имя Мое: просите, и приимете, да радость ваша исполнена будет.
Mpaka tsopano simunapemphe kalikonse mʼdzina langa. Pemphani ndipo mudzalandira, ndipo chimwemwe chanu chidzakhala chathunthu.
25 Сия в притчах глаголах вам: но приидет час, егда ктому в притчах не глаголю вам, но яве о Отце возвещу вам.
“Ngakhale ndakhala ndikuyankhula mʼmafanizo, nthawi ikubwera imene Ine sindidzagwiritsanso ntchito mafanizo otere koma ndidzakuwuzani momveka za Atate anga.
26 В той день во имя Мое воспросите, и не глаголю вам, яко Аз умолю Отца о вас:
Tsiku limenelo inu mudzapempha mʼdzina langa. Ine sindikunena kuti ndidzapempha Atate mʼmalo mwanu ayi.
27 Сам бо Отец любит вы, яко вы Мене возлюбисте и веровасте, яко Аз от Бога изыдох.
Atate mwini anakukondani chifukwa inu mwandikonda Ine ndipo mwakhulupirira kuti Ine ndinabwera kuchokera kwa Atate.
28 Изыдох от Отца и приидох в мир: (и) паки оставляю мир и иду ко Отцу.
Ine ndinabwera kuchokera kwa Atate ndi kulowa mʼdziko lapansi. Tsopano ndikulisiya dziko lapansi kubwerera kwa Atate.”
29 Глаголаша Ему ученицы Его: се, ныне не обинуяся глаголеши, а притчи ни коеяже не глаголеши:
Kenaka ophunzira ake anati, “Tsopano mukuyankhula momveka bwino ndi mopanda mafanizo.
30 ныне вемы, яко веси вся и не требуеши, да кто Тя вопрошает: о сем веруем, яко от Бога изшел еси.
Tsopano ife tikuona kuti Inu mumadziwa zinthu zonse ndi kuti sipafunika wina aliyense kukufunsani. Mwa ichi ife takhulupirira kuti Inu munachokera kwa Mulungu.”
31 Отвеща им Иисус: ныне ли веруете?
Yesu anawafunsa kuti, “Kodi tsopano mwakhulupirira?”
32 Се, грядет час, и ныне прииде, да разыдетеся кийждо во своя и Мене единаго оставите: и несмь един, яко Отец со Мною есть:
Koma nthawi ikubwera ndipo yafika, pamene inu mudzabalalitsidwa, aliyense ku nyumba yake. Inu mudzandisiya ndekhandekha. Koma Ine sindili ndekha, pakuti Atate anga ali nane.
33 сия глаголах вам, да во Мне мир имате: в мире скорбни будете: но дерзайте, (яко) Аз победих мир.
“Ine ndakuwuzani izi kuti mwa Ine mukhale nawo mtendere. Mʼdziko lapansi mudzakhala nawo mavuto. Koma limbikani mtima! Ine ndaligonjetsa dziko lapansi.”