< Книга Иова 5 >

1 Призови же, аще кто тя услышит, или аще кого от святых Ангел узриши.
“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
2 Безумнаго бо убивает гнев, заблуждшаго же умерщвляет рвение.
Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
3 Аз же видех безумных укореняющихся, но абие поядено бысть их жилище.
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
4 Далече да будут сынове их от спасения, и да сотрутся при дверех хуждших, и не будет изимаяй.
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
5 Иже бо они собраша, праведницы поядят, сами же от зол не изяти будут: изможденна буди крепость их.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
6 Не имать бо от земли изыти труд, ни от гор прозябнути болезнь:
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
7 но человек раждается на труд, птенцы же суповы высоко парят.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
8 Обаче же аз помолюся Богови, Господа же всех Владыку призову,
“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
9 Творящаго велия и неизследимая, славная же и изрядная, имже несть числа:
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 дающаго дождь на землю, посылающаго воду на поднебесную:
Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
11 возносящаго смиренныя на высоту и погибшыя воздвизающаго во спасение:
Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 расточающаго советы лукавых, да не сотворят руце их истины.
Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 Уловляяй премудрых в мудрости их, совет же коварных разори.
Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 Во дни обымет их тма, в полудне же да осяжут якоже в нощи,
Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 и да погибнут на брани: немощный же да изыдет из руки сильнаго.
Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 Буди же немощному надежда, неправеднаго же уста да заградятся.
Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
17 Блажен же человек, егоже обличи Бог, наказания же Вседержителева не отвращайся:
“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Той бо болети творит и паки возставляет: порази, и руце Его изцелят:
Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 шестижды от бед измет тя, в седмем же не коснеттися зло:
Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 во гладе избавит тя от смерти, на брани же из руки железа изрешит тя:
Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 от бича языка скрыет тя, и не убоишися от зол находящих:
Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 неправедным и беззаконным посмеешися, от дивиих же зверей не убоишися,
Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 зане с камением дивиим завет твой: зверие бо дивии примирятся тебе.
Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Потом уразумееши, яко в мире будет дом твой, жилище же храмины твоея не имать согрешити:
Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 уразумееши же, яко много семя твое, и чада твоя будут яко весь злак селный:
Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 внидеши же во гроб якоже пшеница созрелая во время пожатая, или якоже стог гумна во время свезенный.
Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
27 Се, сия сице изследихом: сия суть, яже слышахом: ты же разумей себе, аще что сотворил еси.
“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”

< Книга Иова 5 >