< Книга Иова 42 >

1 Отвещав же Иов, рече ко Господу:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova kuti,
2 вем, яко вся можеши, невозможно же Тебе ничтоже.
“Ndikudziwa kuti Inu mungathe kuchita zinthu zonse; chimene mufuna kuchita wina sangaletse konse.
3 Кто есть таяй от Тебе совет, щадяй же словеса и от Тебе мнится утаити? Кто же возвестит ми, ихже не ведех, велия и дивная, ихже не знах?
Munandifunsa kuti, ‘Kodi ndiwe yani amene ukufuna kusokoneza uphungu wanga ndi mawu opanda nzeru? Zoonadi ndinayankhula zimene sindinazimvetse, zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine zimene sindinazidziwe.
4 Послушай же мене, Господи, да и аз возглаголю: вопрошу же Тя, ты же мя научи:
“Inu munandiwuza kuti, ‘Mvetsetsa tsopano ndipo ndidzayankhula; ndidzakufunsa ndipo iwe udzandiyankhe.’
5 слухом убо уха слышах Тя первее, ныне же око мое виде Тя:
Ndinkangomva za Inu ndi makutu anga, koma tsopanonso ndakuonani ndi maso anga.
6 темже укорих себе сам, и истаях, и мню себе землю и пепел.
Nʼchifukwa chake ndi kuchita manyazi, ndikulapa podzithira fumbi ndi phulusa.”
7 Бысть же егда изглагола Господь вся глаголголы сия Иову, рече Господь ко Елифазу Феманитину: согрешил еси ты и оба друзие твои: не глаголасте бо предо Мною ничтоже истинно, якоже раб Мои Иов:
Yehova atayankhula ndi Yobu mawu amenewa anawuza Elifazi wa ku Temani kuti, “Ine ndakukwiyira pamodzi ndi abwenzi ako awiri, chifukwa simunayankhule zabwino za Ine, monga mmene wayankhulira mtumiki wanga Yobu.
8 ныне же возмите седмь телцев и седмь овнов и идите ко рабу Моему Иову, и сотворит жертву о вас: Иов же раб Мой помолится о вас, понеже точию лице его прииму: аще бо не его ради, погубил бых убо вас: не глаголасте бо истины на раба Моего Иова.
Kotero tsopano mutenge ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi kupita nazo kwa mtumiki wanga Yobu kuti mukapereke nsembe zopsereza. Mtumiki wanga Yobu adzakupemphererani, ndipo Ine ndidzalandira pemphero lake. Sindidzakuchitirani kanthu molingana ndi uchitsiru wanu. Inu simunayankhule zabwino za Ine, monga anayankhulira Yobu mtumiki wanga.”
9 Отиде же Елифаз Феманитин и Валдад Савхейский и Софар Минейский и сотвориша, якоже повеле им Господь. И отпусти грехи им Иова ради.
Motero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama anachita zimene Yehova anawawuza ndipo Yehova anamvera pemphero la Yobu.
10 Господь же возрасти Иова: молящуся же ему и о друзех своих, отпусти им грехи их, и даде Господь сугубая, елика бяху прежде Иову во усугубление.
Yobu atawapempherera abwenzi ake aja, Yehova anamubwezera chuma chake ndipo anamupatsa mowirikiza kuposa zomwe anali nazo kale.
11 Услышаша же вси братия его и сестры его вся случившаяся ему, и приидоша к нему, и вси елицы знаху его первее: ядше же и пивше у него, утешиша его и дивишася о всех, яже наведе нань Бог: даде же ему кийждо агницу едину и четыре драхмы злата назнаменована.
Abale ake ndi alongo ake onse, kuphatikizapo onse amene ankamudziwa kale, amabwera kwa iye nʼkudzadya naye chakudya mʼnyumba mwake. Iwo anamutonthoza ndi kumupepesa chifukwa cha mavuto onse amene Yehova analola kuti amugwere. Aliyense wa iwowa anamupatsa ndalama ndi mphete yagolide.
12 Господь же благослови последняя Иовля, неже прежняя: бяху же скоти его, овец четыренадесять тысящ, велблюдов шесть тысящ, супруг волов тысяща, ослиц стадных тысяща.
Yehova anadalitsa Yobu pa masiku ake otsirizawa kupambana poyamba paja. Iye anali ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ngʼombe zantchito 2,000 ndi abulu aakazi 1,000.
13 Родишажеся ему сынове седмь и дщери три:
Anaberekanso ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu.
14 и нарече первую убо День, вторую же Кассию, третию же Амалфеев Рог:
Mwana wake wamkazi woyamba anamutcha Yemima, wachiwiri anamutcha Keziya, wachitatu anamutcha Kereni Hapuki.
15 и не обретошася подобны в лепоте дщерем Иовлевым в поднебесней: даде же им отец наследие в братии их.
Mʼdziko monsemo munalibe akazi okongola ngati ana a Yobu, ndipo abambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi alongo awo.
16 Поживе же Иов по язве лет сто седмьдесят, всех же лет поживе двести четыредесять осмь. И виде Иов сыны своя и сыны сынов своих, даже до четвертаго рода.
Zitachitika zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140. Iye anaona zidzukulu zake mpaka mʼbado wachinayi.
17 И скончася Иов стар и исполнь дний.
Potsiriza, Yobu anamwalira ali nkhalamba ya zaka zochuluka kwambiri.

< Книга Иова 42 >