< Книга Иова 33 >

1 Но послушай, Иове, словес моих и беседу мою внуши:
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 се бо, отверзох уста моя, и возглагола язык мой:
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 чисто сердце мое во словесех, разум же устну моею чистая уразумеет:
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 Дух Божий сотворивый мя, дыхание же Вседержителево поучающее мя:
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 аще можеши, даждь ми ответ к сим: потерпи, стани противу мене, и аз противу тебе.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 От брения сотворен еси ты, якоже и аз: от тогожде сотворения есмы:
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 не страх мой тя смятет, ниже рука моя тяжка будет на тя.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 Обаче рекл еси во ушы мои, и глас глагол твоих услышах, занеже глаголеши:
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 чист есмь аз, не согрешая, непорочен же есмь, ибо не беззаконновах:
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 зазор же на мя обрете и мнит мя, яко противника Себе:
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 вложи же ногу мою в древо и надсмотрял пути моя вся.
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 Како бо глаголеши, яко прав есмь, и не послуша мене? Вечен бо есть, иже над земными.
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Глаголеши бо: чесо ради правды моея не услыша всяко слово?
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 Единою бо возглаголет Господь, второе же во сне, или в поучении нощнем,
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 или, яко егда нападает страх лют на человеки, во дреманиих на ложи:
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 тогда открыет ум человеческий, виденьми страха тацеми их устрашит,
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 да возвратит человека от неправды, тело же его от падения избави,
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 пощаде же душу его от смерти, еже не пасти ему на брани.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 Паки же обличи его болезнию на ложи и множество костей его разслаби:
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 всякаго же брашна пшенична не возможет прияти, а душа его яди хощет,
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 дондеже согниют плоти его, и покажет кости его тощя:
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 приближися же на смерть душа его, и живот его во аде. (questioned)
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 Аще будет тысяща Ангел смертоносных, един от них не уязвит его: аще помыслит сердцем обратитися ко Господу, повесть же человеку свой зазор, и безумие свое покажет,
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 заступит е, еже не впасти ему в смерть, обновит же тело его якоже повапление на стене, кости же его исполнит мозга:
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 умягчит же его плоть якоже младенца, и устроит его возмужавша в человецех.
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 Помолится же ко Господу и прият им будет, внидет же лицем веселым со исповеданием, воздаст же человеком правду свою.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 Посем тогда зазрит человек сам себе, глаголя: яковая содевах? И не по достоинству истяза мя, о нихже согреших:
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 спаси душу мою, еже не внити во истление, и жизнь моя свет узрит.
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 Се, сия вся творит Крепкий (Бог) пути три с мужем:
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 но избави душу мою от смерти, да живот мой во свете хвалит его.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Внимай, Иове, и послушай мене, премолчи, и аз возглаголю:
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 и аще тебе суть словеса, отвещай ми: глаголи, хощу бо оправдитися тебе:
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 аще же ни, ты послушай мене, умолчи, и научу тя премудрости.
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< Книга Иова 33 >