< Книга Иова 10 >

1 Труждаюся душею моею, стеня испущу на мя глаголы моя, возглаголю горестию души моея одержимь
“Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
2 и реку ко Господеви: не учи мя нечествовати, и почто ми сице судил еси?
Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
3 Или добро Ти есть, аще вознеправдую, яко презрел еси дела руку Твоею, совету же нечестивых внял еси?
Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
4 Или якоже человек видит, видиши? Или якоже зрит человек, узриши?
Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
5 Или житие Твое человеческо есть? Или лета Твоя яко дние мужа?
Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
6 Яко истязал еси беззаконие мое и грехи моя изследил еси.
kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
7 Веси бо, яко не нечествовах: но кто есть изимаяй из руку Твоею?
ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
8 Руце Твои сотвористе мя и создасте мя: потом же преложив, поразил мя еси.
“Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
9 Помяни, яко брение мя создал еси, в землю же паки возвращаеши мя.
Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
10 Или не якоже млеко измелзил мя еси, усырил же мя еси равно сыру?
Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
11 Кожею же и плотию мя облекл еси, костьми же и жилами сшил мя еси:
Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
12 живот же и милость положил еси у мене, посещение же Твое сохрани мой дух.
Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
13 Сия имеяй в Тебе, вем, яко вся можеши, и невозможно Тебе ничтоже.
“Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
14 Аще бо согрешу, храниши мя, от беззакония же не безвинна мя сотворил еси.
Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
15 Аще бо нечестив буду, люте мне, аще же буду праведен, не могу возникнути: исполнен бо есмь безчестия,
Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
16 ловимь бо есмь аки лев на убиение: паки же преложив, люте убиваеши мя.
Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
17 Обновляяй на мя испытание мое, гнева бо великаго на мя употребил еси и навел еси на мя искушения.
Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
18 Почто убо мя из чрева извел еси, и не умрох, око же мене не видело бы,
“Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
19 и бых бы аки не был? Почто убо из чрева во гроб не снидох?
Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
20 Или не мало есть время жизни моея? Остави мене почити мало,
Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
21 прежде даже отиду, отнюдуже не возвращуся, в землю темну и мрачну,
ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
22 в землю тмы вечныя, идеже несть света, ниже видети живота человеческаго.
ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”

< Книга Иова 10 >