< Книга пророка Исаии 9 >

1 Сие прежде испий, скоро твори, страно Завулоня и земле Неффалимля, и прочии при мори живущии, и об ону страну Иордана, Галилеа языков.
Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.
2 Людие ходящии во тме видеша свет велий: живущии во стране и сени смертней, свет возсияет на вы.
Anthu oyenda mu mdima awona kuwala kwakukulu; kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani kuwunika kwawafikira.
3 Множайшии людие, яже извел еси, в веселии Твоем: и возвеселятся пред тобою, якоже веселящиися в жатву, и якоже веселятся делящии корысти.
Inu mwauchulukitsa mtundu wanu ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo. Iwo akukondwa pamaso panu, ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola, ngatinso mmene anthu amakondwera pamene akugawana zolanda ku nkhondo.
4 Зане отятся ярем лежай на них, и жезл, иже на выи их: жезл бо истязующих разсыпа Господь, якоже в день, иже на Мадиама.
Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani, inu mwathyola goli limene limawalemera, ndodo zimene amamenyera mapewa awo, ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.
5 Яко всякую одежду собранну лестию и ризу с примирением отдадут, и восхотят, да быша огнем сожжены были.
Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo, ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi zidzatenthedwa pa moto ngati nkhuni.
6 Яко отроча родися нам, Сын, и дадеся нам, егоже началство бысть на раме Его: и нарицается имя Его: велика совета Ангел, Чуден, Советник, Бог крепкий, Властелин, Князь мира, Отец будущаго века: приведу бо мир на князи, мир и здравие Ему.
Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife, ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake. Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.
7 И велие началство Его, и мира Его несть предела на престоле Давидове и на царстве его, исправити е и заступити его в суде и правде, отныне и до века: ревность Господа Саваофа сотворит сия.
Ulamuliro ndi mtendere wake zidzakhala zopanda malire. Iye adzalamulira ufumu wake ali pa mpando waufumu wa Davide, ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza kuchita zimenezi.
8 Смерть посла Господь на Иакова, и прииде на Израиля:
Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo; ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
9 и уразумеют вси людие Ефремовы и живущии в Самарии, в досаждении и высоцем сердцы глаголюще:
Anthu onse okhala mu Efereimu ndi okhala mu Samariya, adzadziwa zimenezi. Iwo amayankhula modzikuza kuti,
10 плинфы падоша, но приидите, изсечем камение и посечем черничие и кедры, и созиждем себе столп.
“Ngakhale njerwa zagumuka, koma ife tidzamanga ndi miyala yosema. Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa, koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
11 И разрушит Бог востающыя на гору Сионю, и враги его разсыплет:
Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
12 Сирию от восток солнца и Еллины от запада солнца, поядающыя Израиля всеми усты. Во всех сих не отвратися ярость Его, но еще рука Его высока.
Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo ayasama pakamwa kuti adye a Israeli. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
13 И людие не обратишася, дондеже язвени быша, и Господа не взыскаша.
Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja, ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
14 И отят Господь от Израиля главу и ошиб, велика и мала, во един день:
Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe, nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
15 старца и чудящихся лицам, сие начало: и пророка учаща беззаконная, сей ошиб.
mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka, mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
16 И будут блажащии людий сих льстяще, и льстят, яко да поглотят я.
Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa, ndipo otsogoleredwa amatayika.
17 Сего ради о юношах их не возвеселится Господь, и сирот их и вдовиц их не помилует: яко вси беззаконнии и лукавии, и всякая уста глаголют неправду. Во всех сих не отвратися ярость Его, но еще рука Его высока.
Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata, ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye, pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo aliyense amayankhula zopusa. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
18 И разгорится яко огнь беззаконие, и яко троскот сухий пояден будет огнем, и разгорится в чащах дубравных и пояст, яже окрест холмов вся.
Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto; moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga, umayatsa nkhalango yowirira, ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
19 За ярость гнева Господня сгоре вся земля, и будут людие яко огнем пожжени: человек брата своего не помилует,
Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse, dziko lidzatenthedwa ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto; palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
20 но уклонится на десно, яко взалчет, и снесть от шуиих, и не насытится человек ядый плоти мышцы своея: снесть бо Манассий Ефремово, и Ефрем Манассиино, яко вкупе повоюют Иуду.
Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya, koma adzakhalabe ndi njala; kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya, koma sadzakhuta. Aliyense azidzadya ana ake omwe.
21 Во всех сих не отвратися ярость (Его), но еще рука Его высока.
Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase; onsewa pamodzi adzadya Yuda. Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.

< Книга пророка Исаии 9 >