< Книга пророка Исаии 22 >
1 Что бысть тебе, яко ныне возлезосте вси на храмины тщетныя?
Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya: Kodi chachitika nʼchiyani, kuti nonsenu mukwere pa madenga?
2 Наполнися град вопиющих, уязвленнии твои не мечьми уязвлени, ниже мертвецы твои умерщвлени ратию:
Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya, iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera? Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga, kapena kufera pa nkhondo.
3 вси князи твои побегоша, и плененнии жестоце суть связани, и крепцыи в тебе далече отбежаша.
Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi; koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe. Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo, ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.
4 Сего ради рекох: оставите мене, да горце восплачуся: не належите утешати мя о сокрушении дщере рода моего:
Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga; ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa. Musayesere kunditonthoza chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”
5 яко день мятежа и пагубы и попрания, и смятение от Господа Саваофа: в дебри Сиони скитаются, от мала даже до велика скитаются по горам.
Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo mʼChigwa cha Masomphenya. Malinga agumuka, komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.
6 Еламите же взяша тулы, и всадницы человецы на конех, и собор ополчения.
Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja. Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.
7 И будут избранны дебри твоя, наполнятся колесниц, конницы же заступят врата твоя
Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta, ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;
8 и открыют врата Иудина, и воззрят в той день во избранныя домы града,
zonse zoteteza Yuda zachotsedwa. Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;
9 и открыют сокровенная домов краеградия Давидова, и узрят, яко множайшии суть, и яко отвратиша воду древния купели во град,
inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide anali ndi malo ambiri ogumuka; munasunga madzi mu chidziwe chakumunsi.
10 и яко разориша домы Иерусалимли на утверждение стене градней.
Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.
11 И сотвористе себе воду между двема стенама, внутрьуду купели древния, и не воззресте на Сотворившаго ю исперва, и Сограждшаго ю не видесте.
Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale, koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi, kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.
12 И призва Господь, Господь Саваоф в той день плачь и рыдание, и острижение и препоясание во вретища:
Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi; kumeta mutu wanu mpala ndi kuvala ziguduli.
13 тии же сотвориша радость и веселие, закалающе телцы и жруще овцы, яко ясти мяса и пити вино, глаголюще: да ямы и пием, утре бо умрем.
Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala; munapha ngʼombe ndi nkhosa; munadya nyama ndi kumwa vinyo. Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa pakuti mawa tifa!”
14 И откровенна сия суть во ущию Господа Саваофа, яко не оставится вам той грех, дондеже умрете.
Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
15 Сице глаголет Господь Саваоф: иди в кущу ко Сомнану строителю дому и рцы ему:
Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo, amene amayangʼanira nyumba yaufumu:
16 что ты зде, и что тебе зде, яко истесал еси себе зде гроб и сотворил еси себе на высоце гроб, и написал еси себе на камени кущу?
Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo kuti udzikumbire manda kuno, kudzikumbira manda pa phiri ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?
17 Се, ныне Господь Саваоф извержет и сотрет мужа, и отимет утварь твою и венец твой славный,
“Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.
18 и повержет тя во страну велику и безмерну, и тамо умреши: и положит колесницу твою добрую в безчестие и дом князя твоего в попрание:
Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu. Kumeneko ndiko ukafere ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako. Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.
19 и извержешися от строителства твоего и от степене твоего.
Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.
20 И будет в той день, и призову раба Моего Елиакима сына Хелкиева
“Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
21 и облеку его во утварь твою, и венец твой дам ему и державу твою, и строителство твое дам в руце его, и будет яко отец живущым во Иерусалиме и живущым во Иудеи.
Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
22 И дам ему славу Давидову, и обвладеет, и не будет противоглаголющаго: и дам ему ключь дому Давидова на рамо его, и отверзет, и не будет затворяющаго, и затворит, и не будет отверзающаго.
Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
23 И поставлю его князя на месте верне, и будет на престоле славы дому отца своего.
Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
24 И будет уповаяй на него всяк славный в дому отца его, от мала даже до велика: и будут зависяще на нем.
Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
25 В той день, сия глаголет Господь Саваоф, подвигнется человек утвержден на месте верне, и отимется, и падет, и потребится слава, яже на нем, яко Господь глагола.
“Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’” Yehova wayankhula chomwechi.